Luka 10 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 10:1-42

Yesu Atuma Ophunzira 72

1Zitatha izi Ambuye anasankha enanso 72 ndi kuwatumiza awiriawiri patsogolo pake ku mzinda uliwonse ndi kumalo kumene Iye anatsala pangʼono kupitako. 2Iye anawawuza kuti, “Zokolola ndi zambiri, koma ogwira ntchito ndi ochepa. Pemphani Ambuye wa zokolola, kuti atumize antchito ku munda wake wa zokolola. 3Pitani! Ine ndikukutumizani ngati nkhosa pakati pa mimbulu. 4Musatenge chikwama kapena thumba kapena nsapato; ndipo musalonjere wina aliyense pa njira.

5“Mukamalowa mʼnyumba, poyamba nenani kuti, ‘Mtendere pa nyumba ino.’ 6Ngati mʼnyumbamo muli munthu wofuna mtendere, mtendere wanuwo udzakhala pa iyeyo; ngati mulibemo, mtendere wanuwo udzabwerera kwa inu. 7Khalani mʼnyumba yomweyo, idyani ndi kumwa chilichonse chimene akupatsani, pakuti wantchito ayenera kulandira malipiro ake. Musachoke kumene mwafikirako ndi kupita ku nyumba zina.

8“Mukamalowa mʼmudzi, ndi kulandiridwa, idyani chilichonse akukonzerani. 9Chiritsani odwala amene ali kumeneko ndipo muwawuze kuti, ‘Ufumu wa Mulungu wayandikira.’ 10Koma mukalowa mʼmudzi ndipo osalandiridwa bwino, kapiteni ku misewu mʼmudzimo nʼkukanena kuti, 11‘Tikukusansirani ngakhale fumbi la mʼmudzi wanuwu limene lamamatira ku mapazi athuwa. Komabe dziwani izi: Ufumu wa Mulungu wayandikira.’ 12Ine ndikuwuzani kuti adzachita chifundo polanga Sodomu pa tsikulo kusiyana ndi mudziwo.

13“Ndiwe watsoka, iwe Korazini! Ndiwe watsoka, iwe Betisaida! Kukanakhala kuti zodabwitsa zimene zinachitika mwa inu zinachitika ku Turo ndi Sidoni, iwo akanatembenuka mtima kale lomwe, atavala ziguduli ndi kudzola phulusa. 14Koma adzachita chifundo polanga Turo ndi Sidoni kusiyana ndi inu. 15Kodi iwe Kaperenawo, adzakukweza mpaka kumwamba? Ayi, adzakutsitsa mpaka ku Malo a anthu akufa.

16“Womvera inu, akumvera Ine; wokana inu, akukana Ine. Ndipo wokana Ine; akukana Iye amene anandituma Ine.”

17Anthu 72 aja anabwerera ndi chimwemwe ndipo anati, “Ambuye, ngakhale ziwanda zinatigonjera ife mʼdzina lanu.”

18Iye anayankha kuti, “Ndinaona Satana akugwa kuchokera kumwamba ngati mphenzi. 19Ine ndakupatsani ulamuliro woponda njoka ndi zinkhanira, ndi kugonjetsa mphamvu zonse za mdani; palibe chimene chidzakupwetekani. 20Komabe musakondwere chifukwa mizimu yoyipa inakugonjerani, koma kondwerani chifukwa mayina anu analembedwa kumwamba.”

21Nthawi imeneyo Mzimu Woyera anadzaza Yesu ndi chimwemwe ndipo anati, “Ine ndikulemekeza Inu, Atate Ambuye a kumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa mwawabisira anthu anzeru ndi ophunzira zinthu izi ndipo mwaziwulula kwa ana aangʼono. Inde, Atate, pakuti munachita zimenezi mwachifuniro chanu.

22“Atate anga anapereka zinthu zonse mʼmanja mwanga. Palibe amene amadziwa Mwana kupatula Atate yekha, ndipo palibe amene amadziwa Atate kupatula Mwana yekha, ndiponso amene Mwanayo akufuna kumuwululira.”

23Kenaka anatembenukira kwa ophunzira ake nawawuza iwo okha kuti, “Ndi odala maso amene akuona zimene mukuonazi. 24Pakuti kunena zoona aneneri ambiri ndi mafumu anafunitsitsa kuona zimene mukuonazi koma sanazione, ndi kumva zimene mukumvazi koma sanazimve.”

Fanizo la Msamariya Wachifundo

25Nthawi ina katswiri wa malamulo anayimirira kuti ayese Yesu. Iye anati, “Aphunzitsi, ndichite chiyani kuti ndikhale ndi moyo wosatha?”

26Yesu anayankha kuti, “Mwalembedwa chiyani mʼMalamulo, ndipo iwe umawerenga zotani?”

27Iye anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse, ndi moyo wako wonse, ndi mphamvu zako zonse ndi nzeru zako zonse, ndi kukonda mnansi wako monga iwe mwini.”

28Yesu anayankha kuti, “Iwe wayankha bwino, chita zimenezi ndipo udzakhala ndi moyo.”

29Koma iye anafuna kudzilungamitsa yekha, ndipo anamufunsanso Yesu kuti, “Kodi mnansi wanga ndani?”

30Yesu pomuyankha anati, “Munthu wina ankatsikira ku Yeriko kuchokera ku Yerusalemu. Pa njira anavulazidwa ndi achifwamba. Anamuvula zovala zake, namumenya ndi kuthawa, namusiya ali pafupi kufa. 31Wansembe ankapita pa njira yomweyo, ndipo ataona munthuyo, analambalala. 32Chimodzimodzinso, Mlevi wina pamene anafika pa malopo ndi kumuona, analambalalanso. 33Koma Msamariya wina, ali pa ulendo wake, anafika pamene panali munthuyo; ndipo atamuona, anamva naye chisoni. 34Anapita panali munthu wovulalayo, nathira mafuta ndi vinyo pa zilonda zake, nʼkuzimanga. Kenaka anamukweza pa bulu wake, napita naye ku nyumba ya alendo, namusamalira. 35Mmawa mwake anatenga ndalama ziwiri zasiliva nazipereka kwa woyangʼanira nyumbayo, nati, ‘Musamalireni munthuyu, ndipo pobwera ndidzakubwezerani zonse zimene mugwiritse ntchito.’

36“Kodi ukuganiza ndi ndani mwa atatuwa, amene anali mnansi wa munthu amene anavulazidwa ndi achifwambawo?”

37Katswiri wa Malamulo uja anayankha kuti, “Amene anamuchitira chifundo.”

Yesu anamuwuza kuti, “Pita, uzikachita chimodzimodzi.”

Marita ndi Mariya

38Yesu ndi ophunzira ake akuyenda, anafika pa mudzi kumene mayi wotchedwa Marita anamulandira Iye mʼnyumba mwake. 39Mayiyu anali ndi mchemwali wake wotchedwa Mariya, amene anakhala pa mapazi a Yesu kumverera zimene Iye ankanena. 40Koma Marita anatanganidwa ndi zokonzekera zonse zimene zimayenera kuchitika. Iye anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Ambuye, kodi simusamala kuti mchemwali wanga wandisiya kuti ndichite ntchito yonse ndekha? Muwuzeni andithandize!”

41Ambuye anati, “Marita, Marita, ukudandaula ndi kuvutika ndi zinthu zambiri, 42koma chofunika nʼchimodzi chokha. Mariya wasankha chinthu chabwino, ndipo palibe angamulande chimenechi.”

Persian Contemporary Bible

لوقا 10:1-42

مأموريت هفتاد شاگرد ديگر

1آنگاه، عيسای خداوند هفتاد نفر ديگر را تعيين كرد و ايشان را دو به دو به شهرها و نقاطی كه خود عازم آن بود، فرستاد، 2و به آنها فرمود: «مردم بيشماری آماده شنيدن كلام خدا هستند. بلی، محصول بی‌نهايت زياد است و كارگر كم! پس از صاحب محصول درخواست كنيد تا كارگران بيشتری به كمكتان بفرستد. 3برويد و فراموش نكنيد كه من شما را همچون بره‌ها به ميان گرگها می‌فرستم. 4با خود نه پول برداريد، نه كوله‌بار و نه حتی يک جفت كفش اضافی. در بين راه نيز وقت تلف نكنيد.

5«وارد هر خانه‌ای كه شديد، قبل از هر چيز بگوييد: بركت بر اين خانه باشد. 6اگر كسی در آنجا لياقت بركت را داشته باشد، بركت شامل حالش می‌شود و اگر لياقت نداشته باشد، بركت به خود شما برمی‌گردد. 7پس در همان خانه بمانيد و به دنبال جای بهتر، از خانه به خانه‌ای ديگر نقل مكان نكنيد. هر چه به شما می‌دهند، بخوريد و بنوشيد و از اينكه از شما پذيرايی می‌كنند، شرمسار نباشيد، چون كارگر مستحق مزد خويش است!

8‏-9«اگر اهالی شهری شما را پذيرا شوند، هر چه پيش شما بگذارند، بخوريد و بيماران را شفا دهيد و به ايشان بگوييد: ملكوت خدا به شما نزديک شده است.

10«اما اگر شهری شما را نپذيرفت، به كوچه‌های آن برويد و بگوييد: 11”ما حتی گرد و خاک شهرتان را كه بر پاهای ما نشسته، می‌تكانيم تا بدانيد كه آيندهٔ تاريكی در انتظار شماست. اما بدانيد كه درِ رحمت خدا به روی شما گشوده شده بود.“ 12حتی وضع شهر گناهكاری چون سدوم، در روز داوری، از وضع چنان شهری بهتر خواهد بود.

13«وای بر شما ای اهالی خورزين و بيت‌صيدا! چه سرنوشت وحشتناكی در انتظار شماست! چون اگر معجزاتی را كه برای شما كردم در شهرهای فاسدی چون صور و صيدون انجام می‌دادم، اهالی آنجا مدتها پيش به زانو درمی‌آمدند و توبه می‌كردند، و يقيناً پلاس می‌پوشيدند و خاكستر بر سر خود می‌ريختند، تا نشان دهند كه چقدر از كرده خود پشيمانند. 14بلی، در روز داوری، مجازات مردم صور و صيدون از مجازات شما بسيار سبكتر خواهد بود. 15ای مردم كفرناحوم، به شما چه بگويم؟ شما كه می‌خواستيد تا به آسمان سر برافرازيد، بدانيد كه به جهنم سرنگون خواهيد شد!»

16سپس به شاگردان خود گفت: «هر كه شما را بپذيرد، مرا پذيرفته است، و هر كه شما را رد كند، در واقع مرا رد كرده است، و هر كه مرا رد كند، خدايی را كه مرا فرستاده، رد كرده است.»

17پس از مدتی هفتاد شاگرد برگشتند و با خوشحالی به عيسی خبر داده، گفتند: «خداوندا، حتی ارواح پليد نيز به نام تو، از ما اطاعت می‌كنند!»

18عيسی فرمود: «بلی، من شيطان را ديدم كه همچون برق، از آسمان به زير افتاد! 19من به شما قدرت بخشيده‌ام تا بر همه نيروهای شيطان مسلط شويد و از ميان مارها و عقربها بگذريد و آنها را پايمال كنيد؛ و هيچ چيز هرگز به شما آسيب نخواهد رسانيد! 20با وجود اين، فقط از اين شادی نكنيد كه ارواح پليد از شما اطاعت می‌كنند، بلكه از اين شاد باشيد كه نام شما در آسمان ثبت شده است!»

دعای شکرگزاری عيسی

21آنگاه دل عيسی سرشار از شادی روح خدا گرديد و فرمود: «ای پدر، ای مالک آسمان و زمين، تو را سپاس می‌گويم كه اين امور را از اشخاص متفكر و دانای اين جهان پنهان كردی و به كسانی آشكار ساختی كه با سادگی، همچون كودكان به تو ايمان دارند. بلی، ای پدر، تو را شكر می‌كنم، چون خواست تو چنين بود.»

22سپس به شاگردان خود گفت: «پدرم، خدا، همه چيز را در اختيار من قرار داده است. پسر را هيچكس نمی‌شناسد به غیر از پدر، و پدر را نيز كسی براستی نمی‌شناسد، مگر پسر و آنانی كه از طريق پسر او را بشناسند.»

23سپس، در تنهايی به آن دوازده شاگرد فرمود: «خوشا به حال شما كه اين چيزها را می‌بينيد! 24چون پيامبران و پادشاهان زيادی در روزگاران گذشته، آرزو داشتند كه آنچه شما می‌بينيد و می‌شنويد، ببينند و بشنوند!»

بزرگترين دستور خدا

25روزی يكی از علمای دين كه می‌خواست اعتقادات عيسی را امتحان كند، از او پرسيد: «استاد، انسان چه بايد بكند تا حيات جاودانی را به دست بياورد؟»

26عيسی به او گفت: «در كتاب تورات، در اين باره چه نوشته شده است؟»

27جواب داد: «نوشته شده كه خداوند، خدای خود را با تمام دل، با تمام جان، با تمام قوت و با تمام فكرت دوست بدار. همسايه‌ات را نيز دوست بدار، همانقدر كه خود را دوست می‌داری!»

28عيسی فرمود: «بسيار خوب، تو نيز چنين كن تا حيات جاودانی داشته باشی.»

29اما او چون می‌خواست سؤال خود را موجه و بجا جلوه دهد، باز پرسيد: «خوب، همسايه من كيست؟»

داستان سامری نيکو

30عيسی در جواب، داستانی تعريف كرد و فرمود: «يک يهودی از اورشليم به شهر اريحا می‌رفت. در راه به دست راهزنان افتاد. ايشان لباس و پول او را گرفتند و او را كتک زده، نيمه جان كنار جاده انداختند و رفتند. 31از قضا، كاهنی يهودی از آنجا می‌گذشت. وقتی او را كنار جاده افتاده ديد، راه خود را كج كرد و از سمت ديگر جاده رد شد. 32سپس يكی از خادمان خانه خدا از راه رسيد و نگاهی به او كرد. اما او نيز راه خود را در پيش گرفت و رفت.

33«آنگاه يک سامری از راه رسيد (يهودی‌ها و سامری‌ها، با يكديگر دشمنی داشتند). وقتی آن مجروح را ديد، دلش به حال او سوخت، 34نزديک رفت و كنارش نشست، زخمهايش را شست و مرهم ماليد و بست. سپس او را بر الاغ خود سوار كرد و به مهمانخانه‌ای برد و از او مراقبت نمود. 35روز بعد، هنگامی كه آنجا را ترک می‌كرد، مقداری پول به صاحب مهمانخانه داد و گفت: از اين شخص مراقبت كن و اگر بيشتر از اين خرج كنی، وقتی برگشتم، پرداخت خواهم كرد!

36«حال، به نظر تو كدام يک از اين سه نفر، همسايه آن مرد بيچاره بود؟»

37جواب داد: «آنكه به او ترحم نمود و كمكش كرد.»

عيسی فرمود: «تو نيز چنين كن!»

اهميت گوش دادن به كلام خدا

38در سر راه خود به اورشليم، عيسی و شاگردان به دهی رسيدند. در آنجا زنی به نام مارتا ايشان را به خانهٔ خود دعوت كرد. 39او خواهری داشت به نام مريم. وقتی عيسی به خانه ايشان آمد، مريم با خيالی آسوده نشست تا به سخنان او گوش فرا دهد.

40اما مارتا كه برای پذيرايی از آن همه میهمان، پريشان شده و به تكاپو افتاده بود، نزد عيسی آمد و گفت: «سَروَر من، آيا اين دور از انصاف نيست كه خواهرم اينجا بنشيند و من به تنهايی همه كارها را انجام دهم؟ لطفاً به او بفرما تا به من كمک كند!»

41عيسای خداوند به او فرمود: «مارتا، تو برای همه چيز خود را ناراحت و مضطرب می‌كنی، 42اما فقط يک چيز اهميت دارد. مريم همان را انتخاب كرده است و من نمی‌خواهم او را از اين فيض محروم سازم!»