Levitiko 8 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 8:1-36

Mwambo Wodzoza Aaroni ndi Ana Ake

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Tenga Aaroni ndi ana ake, zovala zawo, mafuta wodzozera, ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo, nkhosa ziwiri zazimuna ndi dengu la buledi wopanda yisiti, 3ndipo usonkhanitse gulu la anthu pa khomo la tenti ya msonkhano.” 4Mose anachita zomwe Yehova anamulamula ndipo gulu la anthu linasonkhana pa khomo la tenti ya msonkhano.

5Mose anawuza gulu la anthuwo kuti, “Izi ndi zimene Yehova walamulira kuti zichitike.” 6Pamenepo Mose anabwera ndi Aaroni ndi ana ake nawasambitsa ndi madzi. 7Anamuveka Aaroni mwinjiro, ndi kumumanga lamba mʼchiwuno. Anamuvekanso mkanjo wa efodi ndi efodiyo. Anamangira lamba efodiyo amene analukidwa mwaluso uja, motero efodiyo analimba mʼchiwunomo. 8Anamuvekanso chovala chapachifuwa ndipo mʼchovalacho anayikamo Urimu ndi Tumimu. 9Kenaka anamuveka Aaroniyo nduwira kumutu ndipo patsogolo pa nduwirayo anayikapo duwa lagolide, chizindikiro chopatulika monga momwe Yehova analamulira Mose.

10Pamenepo Mose anatenga mafuta wodzozera nadzoza tenti ya msonkhano pamodzi ndi zonse zimene zinali mʼmenemo, ndipo potero anazipatula. 11Anawaza mafuta ena pa guwa kasanu ndi kawiri, nalidzoza guwalo pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso beseni ndi tsinde lake, nazipatula. 12Anathira mafuta wodzozera ena pamutu pa Aaroni ndipo anamudzoza ndi kumupatula. 13Kenaka anabwera ndi ana a Aaroni. Anawaveka minjiro, ndi kuwamanga malamba mʼchiwuno ndi kuwaveka nduwira kumutu monga momwe Yehova analamulira Mose.

14Kenaka Mose anabwera ndi ngʼombe yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, ndipo Aaroni ndi ana ake anasanjika manja awo pamutu pa ngʼombeyo. 15Mose anapha ngʼombeyo, ndi kutenga magazi ena angʼombeyo ndi kupaka ndi chala chake pa nyanga zaguwa lansembe, naliyeretsa. Magazi otsalawo anawakhuthulira pa tsinde laguwalo. Motero anachita mwambo wopepesera machimo. 16Mose anatenganso mafuta onse okuta matumbo, mafuta ophimba chiwindi, ndiponso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake, nazitentha pa guwapo. 17Koma nyama yangʼombeyo, chikopa chake ndi matumbo ake anaziwotcha kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.

18Kenaka anabwera ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopsereza, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake. 19Ndipo Mose anapha nkhosayo ndi kuwaza magazi ake mbali zonse zaguwalo. 20Anayidula nkhosayo nthulinthuli ndipo anatentha mutu wake, nthulizo ndi mafuta. 21Anatsuka matumbo ake ndi miyendo yake, ndi kutentha nkhosa yonseyo pa guwa lansembe kuti ikhale nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yachakudya yoperekedwa kwa Yehova monga Yehovayo analamulira Mose.

22Kenaka Mose anapereka nkhosa yayimuna ina pamwambo wodzoza ansembe, ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna anasanjika manja awo pamutu pake. 23Mose anayipha nkhosayo ndipo anatenga magazi ake ena ndi kupaka ndewere za khutu la kudzanja lamanja la Aaroni, pa chala chake chachikulu cha kudzanja lamanja, ndi pa chala chake chachikulu cha phazi lakumanja. 24Pambuyo pake Mose anabwera ndi ana aamuna a Aaroni ndi kupaka magazi pa ndewere za makutu awo akumanja, pa zala zawo zazikulu za dzanja lamanja, ndiponso pa zala zawo zazikulu za kuphazi lakumanja. Kenaka iye anawaza magazi otsalawo mbali zonse za guwalo. 25Anatenganso mafuta ake, mafuta a ku mchira wake, mafuta okuta matumbo, mafuta okuta chiwindi, impsyo zonse ziwiri ndi mafuta ake ndiponso ntchafu yakumanja. 26Ndipo mʼdengu la buledi wopanda yisiti limene linali pamaso pa Yehova, anatengamo buledi mmodzi, buledi mmodzi wokhala ndi mafuta a olivi, ndi buledi wopyapyala mmodzi. Zonsezi anaziyika pa mafuta aja ndi pa ntchafu ya ku dzanja lamanja ija. 27Mose anapereka zonsezi mʼmanja mwa Aaroni ndi ana ake amene anazipereka kwa Yehova kuti zikhale nsembe yoweyula. 28Kenaka Mose anazitenga mʼmanja mwawo ndipo anazipsereza pa guwa lansembe pamwamba penipeni pamodzi ndi nsembe yopsereza ija kuti ikhale nsembe yopereka pamwambo wodzoza ansembe, kuti ipereke fungo lokoma, chopereka chachakudya kwa Yehova. 29Mose anatenga chidale cha nkhosa yayimuna, chomwe ndi gawo lake pamwambo wodzoza ansembe, ndipo anachiweyula pamaso pa Yehova kuti chikhale nsembe yoweyula monga momwe Yehova analamulira Mose.

30Kenaka Mose anatenga mafuta wodzozera ansembe ndi magazi amene anali pa guwa nawaza pa Aaroni ndi zovala zake ndiponso ana ake aja ndi zovala zawo. Motero Mose anapatula Aaroni ndi zovala zake, ndiponso ana ake ndi zovala zawo.

31Mose anawuza Aaroni ndi ana ake kuti, “Phikani nyamayo pa khomo la tenti ya msonkhano, ndipo mudyere pomwepo pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu la zopereka za pamwambo wodzoza ansembe monga Yehova analamulira kuti, ‘Aaroni ndi ana ake azidya zimenezi.’ 32Ndipo nyama ndi buledi zotsalazo, muziwotche. 33Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano kwa masiku asanu ndi awiri mpaka masiku amwambo wokudzozani unsembe atatha, pakuti mwambowu ndi wa masiku asanu ndi awiri. 34Zimene zachitika lerozi analamula ndi Yehova kuti zichitike ngati nsembe yopepesera machimo anu. 35Muzikhala pa khomo la tenti ya msonkhano usana ndi usiku kwa masiku asanu ndi awiri. Ndipo muzichita zimene Yehova wakulamulani kuti musafe, pakuti zimenezi ndi zomwe Yehova wandilamulira.” 36Choncho Aaroni ndi ana ake anachita zonse zimene Yehova analamula kudzera mwa Mose.

Священное Писание

Левит 8:1-36

Посвящение Харуна и его сыновей на служение Вечному

(Исх. 29:1-37)

1Вечный сказал Мусе:

2– Приведи Харуна и его сыновей, возьми их одеяния, масло для помазания, молодого быка для жертвы за грех, двух баранов и корзину с пресным хлебом 3и собери всё общество к входу в шатёр встречи.

4Муса сделал, как повелел ему Вечный, и общество собралось к входу в шатёр встречи.

5Муса сказал собравшимся:

– Это повелел сделать Вечный.

6Муса вывел Харуна и его сыновей вперёд и омыл их водой. 7Он облачил Харуна в рубашку, обвязал его поясом, одел в верхнюю ризу и возложил на него ефод8:7 Ефод – своего рода передник, бывший частью облачения священнослужителя при исполнении им его обязанностей.. Он обвязал его по ефоду украшенным поясом, закрепив на нём ефод. 8Он возложил на него нагрудник, а на нагрудник – священный жребий8:8 Букв.: «урим («свет») и туммим («совершенство»)». С помощью этих предметов определяли волю Всевышнего, но как именно, сегодня не известно.. 9Он надел ему на голову тюрбан и прикрепил к тюрбану спереди золотое украшение, священный венец, как повелел Мусе Вечный.

10Муса взял масло для помазания и помазал священный шатёр и всё, что в нём. Так он освятил всё это. 11Он семь раз окропил маслом жертвенник, помазав его со всей его утварью и умывальник с его основанием, чтобы освятить их. 12Он возлил масло для помазания на голову Харуна и помазал его, чтобы освятить. 13Затем он вывел вперёд сыновей Харуна, надел на них рубашки, обвязал их поясами и надел на них головные уборы, как повелел Мусе Вечный.

14Он привёл молодого быка для жертвы за грех, а Харун и его сыновья возложили руки ему на голову. 15Муса заколол быка, взял кровь и пальцем нанёс её на рога жертвенника, чтобы очистить его. Остальную кровь он вылил к основанию жертвенника. Так он освятил жертвенник, чтобы сделать его чистым. 16Ещё Муса взял весь жир вокруг внутренностей, сальник с печени и обе почки с их жиром и сжёг на жертвеннике. 17Но самого быка – его шкуру, мясо и кишки – он сжёг за лагерем, как повелел Мусе Вечный.

18Муса привёл барана для всесожжения, а Харун и его сыновья возложили руки ему на голову. 19Муса заколол барана и окропил его кровью жертвенник со всех сторон. 20Он разрезал барана на куски и сжёг их вместе с головой и жиром. 21Он вымыл внутренности и голени жертвы и сжёг всего барана на жертвеннике как всесожжение, приятное благоухание, огненную жертву Вечному, как повелел Мусе Вечный.

22Он привёл другого барана, барана для посвящения, а Харун и его сыновья возложили руки ему на голову. 23Муса заколол барана, взял кровь и помазал ею мочку правого уха Харуна, большой палец его правой руки и большой палец правой ноги. 24Муса вывел вперёд сыновей Харуна и помазал кровью мочки их правых ушей, большие пальцы их правых рук и большие пальцы правых ног. Он окропил кровью жертвенник со всех сторон. 25Он взял жир, курдюк, весь жир вокруг внутренностей, сальник с печени, обе почки с их жиром и правое бедро. 26Из корзины с пресным хлебом, что была перед Вечным, он взял один пресный хлеб, лепёшку, приготовленную на масле, и корж. Он положил их на жир и правое бедро барана. 27Он вложил всё это в руки Харуну и его сыновьям и потряс перед Вечным как приношение потрясания. 28Затем Муса взял это у них из рук и сжёг на жертвеннике, сверху всесожжения, как жертву посвящения, приятное благоухание, огненную жертву Вечному. 29Он взял грудину – свою долю от барана для посвящения – и потряс её перед Вечным как приношение потрясания, как повелел Мусе Вечный.

30Муса взял масло для помазания и кровь с жертвенника и окропил Харуна и его одеяния, а также его сыновей с их одеяниями. Так он освятил Харуна, его сыновей и их одеяния.

31Муса сказал Харуну и его сыновьям:

– Сварите мясо у входа в шатёр встречи и ешьте его там с хлебом из корзины для посвящённых хлебов, как я велел, сказав8:31 Или: «как мне было приказано».: «Пусть Харун и его сыновья едят это». 32Остаток мяса и хлеба сожгите. 33Не уходите от входа в шатёр встречи семь дней, пока не завершатся дни вашего посвящения, потому что ваше посвящение будет длиться семь дней. 34Сделанное сегодня было исполнено по повелению Вечного, чтобы совершить для вас очищение. 35Оставайтесь у входа в шатёр встречи день и ночь в течение семи дней и исполняйте то, что требует Вечный, чтобы вам не умереть, потому что так мне было велено.

36Харун и его сыновья сделали всё, что повелел через Мусу Вечный.