Levitiko 7 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 7:1-38

Nsembe Yopepesera Kupalamula

1“ ‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa: 2Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa. 3Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo. 4Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi. 5Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula. 6Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.

7“ ‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake. 8Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake. 9Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo. 10Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.

Nsembe Yachiyanjano

11“ ‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:

12“ ‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta. 13Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake. 14Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano. 15Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.

16“ ‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake. 17Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto. 18Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.

19“ ‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo. 20Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake. 21Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’ ”

Za Kuletsa Kudya Mafuta ndi Magazi

22Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 23“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi. 24Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo. 25Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake. 26Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse. 27Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’ ”

Gawo la Ansembe

28Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 29“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova. 30Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova. 31Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake. 32Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye. 33Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake. 34Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”

35Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova. 36Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.

37Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano. 38Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.

Thai New Contemporary Bible

เลวีนิติ 7:1-38

เครื่องบูชาลบความผิด

1“ ‘ต่อไปนี้เป็นกฎระเบียบเกี่ยวกับเครื่องบูชาลบความผิดซึ่งบริสุทธิ์ที่สุดคือ 2สัตว์ที่นำมาถวายเป็นเครื่องบูชาลบความผิดจะฆ่าในที่สำหรับฆ่าสัตว์เป็นเครื่องเผาบูชา แล้วพรมเลือดของมันรอบแท่น 3ปุโรหิตจะถวายไขมันทั้งหมด คือไขมันส่วนหางและไขมันหุ้มเครื่องใน 4ไตสองลูก ไขมันหุ้มไตใกล้ส่วนเอว และพังผืดหุ้มตับซึ่งเอาออกมาพร้อมไต 5ปุโรหิตจะเผาสิ่งเหล่านี้บนแท่นบูชาเป็นเครื่องบูชาด้วยไฟถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้านี่คือเครื่องบูชาลบความผิด 6ผู้ชายในครอบครัวของปุโรหิตเท่านั้นจึงจะกินเนื้อนั้นได้ และต้องกินในที่บริสุทธิ์เพราะเป็นของบริสุทธิ์ที่สุด

7“ ‘กฎเดียวกันนี้ใช้ได้ทั้งเครื่องบูชาไถ่บาปและเครื่องบูชาลบความผิดคือ เนื้อส่วนที่เหลือมอบให้เป็นอาหารของปุโรหิตผู้ทำการลบบาป 8ปุโรหิตผู้ถวายเครื่องเผาบูชาจะได้รับหนังของมันด้วย 9ปุโรหิตซึ่งถวายเครื่องธัญบูชาจะได้รับส่วนที่เหลือเมื่อเสร็จพิธีแล้ว ไม่ว่าจะเป็นธัญบูชาที่อบ ปิ้ง หรือทอด 10ธัญบูชาทุกอย่างไม่ว่าจะแห้งหรือเคล้าน้ำมัน เป็นของบรรดาบุตรของอาโรนทุกคนอย่างเท่าเทียมกัน

เครื่องสันติบูชา

11“ ‘ต่อไปนี้เป็นกฎระเบียบเกี่ยวกับเครื่องสันติบูชาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า

12“ ‘หากเป็นเครื่องบูชาขอบพระคุณ ให้ผู้ถวายนำขนมปังไม่ใส่เชื้อคลุกน้ำมันควบคู่มากับเครื่องบูชา พร้อมด้วยขนมปังแผ่นบางไม่ใส่เชื้อทาน้ำมัน และขนมปังแป้งละเอียดเคล้าน้ำมัน 13ให้นำขนมปังใส่เชื้อมาถวายควบคู่กับเครื่องสันติบูชา เป็นเครื่องบูชาขอบพระคุณ 14เขาจะต้องนำส่วนหนึ่งจากเครื่องบูชาแต่ละชนิดมาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า แล้วมอบให้ปุโรหิตผู้พรมเลือดของเครื่องสันติบูชา 15เนื้อของเครื่องสันติบูชาเพื่อขอบพระคุณจะต้องกินในวันที่ถวาย อย่าเหลือค้างจนถึงวันรุ่งขึ้น

16“ ‘หากเป็นเครื่องบูชาตามที่ถวายปฏิญาณไว้หรือเครื่องบูชาตามความสมัครใจ ส่วนที่ปุโรหิตยังไม่ได้กินในวันที่ถวายอาจจะกินในวันรุ่งขึ้นได้ 17แต่เนื้อของเครื่องบูชาที่เหลือค้างจนถึงวันที่สามต้องเผาทิ้ง 18เพราะหากกินส่วนใดของเครื่องสันติบูชาในวันที่สามจะไม่เป็นที่ยอมรับ ไม่เป็นผลดีแก่ผู้ที่นำมาถวายเพราะเป็นเครื่องบูชาที่ไม่บริสุทธิ์ ผู้ที่กินจะต้องรับผิดชอบ

19“ ‘อย่ากินเนื้อที่สัมผัสสิ่งที่เป็นมลทินตามระเบียบพิธี จงเผาทิ้ง แต่เนื้อส่วนอื่นให้ผู้ที่ไม่มีมลทินตามระเบียบพิธีกินได้ 20แต่ถ้าผู้ใดเป็นมลทินแล้วยังขืนกินเนื้อของเครื่องสันติบูชาซึ่งเป็นขององค์พระผู้เป็นเจ้า ผู้นั้นจะถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา 21ผู้ใดแตะต้องสิ่งที่เป็นมลทิน ไม่ว่าจะเป็นสิ่งที่เป็นมลทินของมนุษย์ หรือสัตว์ที่เป็นมลทิน หรือสิ่งใดๆ อันน่ารังเกียจที่เป็นมลทิน แล้วมากินเนื้อของเครื่องสันติบูชาที่เป็นขององค์พระผู้เป็นเจ้า ผู้นั้นจะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา’ ”

ห้ามกินไขมันและเลือด

22องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 23“จงสั่งประชากรอิสราเอลว่า ‘อย่ากินไขมัน ไม่ว่าไขมันจากวัว แกะ หรือแพะ 24ไขมันจากสัตว์ที่พบเมื่อตายแล้ว หรือถูกสัตว์ป่าทำร้าย อาจจะใช้ทำอย่างอื่นได้ แต่อย่ากิน 25ผู้ใดกินไขมันจากสัตว์ซึ่งถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าด้วยไฟจะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา 26และไม่ว่าเจ้าอาศัยที่ไหนก็ตาม ห้ามกินเลือด ไม่ว่าเลือดนกหรือเลือดสัตว์ใดๆ 27ถ้าผู้ใดกินเลือดผู้นั้นจะต้องถูกตัดออกจากหมู่ประชากรของเขา’ ”

ส่วนแบ่งของปุโรหิต

28องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า 29“จงกล่าวแก่ประชากรอิสราเอลว่า ‘ผู้ใดนำเครื่องสันติบูชามาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า จะต้องนำส่วนหนึ่งของเครื่องบูชานั้นมาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า 30เขาต้องนำเครื่องบูชานี้มาเผาถวายด้วยไฟแด่ องค์พระผู้เป็นเจ้ากับมือของเขาเอง เขาจะนำไขมันและอกมายื่นถวายต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้าเป็นเครื่องบูชายื่นถวาย 31ปุโรหิตจะเผาไขมันบนแท่นบูชา แต่เนื้ออกเป็นของอาโรนและบรรดาบุตรชาย 32โคนขาขวาของสัตว์ที่นำมาถวายเป็นเครื่องสันติบูชาจะยกให้แก่ปุโรหิตผู้ประกอบพิธี 33บุตรชายของอาโรนผู้ถวายเลือดและไขมันของเครื่องสันติบูชาจะได้รับโคนขาขวาเป็นส่วนแบ่งของเขา 34เราได้กำหนดให้ยกเนื้ออกและโคนขาที่ยื่นถวายเป็นสิ่งที่ชาวอิสราเอลมอบให้แก่อาโรนและบรรดาบุตรชายของเขา เป็นส่วนแบ่งประจำจากเครื่องสันติบูชาของพวกเขา’ ”

35นี่เป็นส่วนของอาโรนกับบรรดาบุตรชายจากเครื่องบูชาด้วยไฟถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้า ซึ่งยกให้แก่พวกเขาในวันที่ได้รับการแต่งตั้งให้ปฏิบัติหน้าที่ปุโรหิตรับใช้องค์พระผู้เป็นเจ้า 36ในวันที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงเจิมตั้งพวกเขา พระองค์ทรงบัญชาชาวอิสราเอลให้มอบสิ่งเหล่านี้แก่พวกเขาเป็นส่วนแบ่งประจำตลอดทุกชั่วอายุ

37ทั้งหมดนี้คือกฎระเบียบเกี่ยวกับเครื่องเผาบูชา เครื่องธัญบูชา เครื่องบูชาไถ่บาป เครื่องบูชาลบความผิด เครื่องบูชาในพิธีสถาปนา และเครื่องสันติบูชา 38ซึ่งองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงบัญชาโมเสสบนภูเขาซีนายในวันที่ทรงบัญชาชาวอิสราเอลให้นำเครื่องบูชามาถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าในถิ่นกันดารซีนาย