Levitiko 5 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 5:1-19

1“ ‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.

2“ ‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.

3“ ‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.

4“ ‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.

5“ ‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo. 6Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.

7“ ‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza. 8Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu, 9kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo. 10Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.

11“ ‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo. 12Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo. 13Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’ ”

Chopereka Chopepesera Kupalamula

14Yehova anawuza Mose kuti, 15“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula. 16Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.

17“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa. 18Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. 19Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

New Russian Translation

Левит 5:1-19

1Если человек согрешит, промолчав, когда его приведут к присяге, чтобы свидетельствовать о том, что он видел или знал, – он подлежит наказанию.

2Или если человек прикоснется к нечистому: к трупам нечистых диких зверей, или нечистого скота, или нечистых пресмыкающихся – даже если не заметит этого, – он станет нечистым и будет виновен.

3Или если он прикоснется к человеческой нечистоте – любой нечистоте, которая его осквернит – даже если не заметит этого, то когда поймет, он будет виновен.

4Или если человек произносит опрометчивую клятву сделать что-либо хорошее или злое, о чем только можно безрассудно поклясться – то даже если он не осознает этого, когда поймет, он будет виновен.

5Если кто-то виновен в этом, пусть открыто признает, в чем согрешил, 6и в расплату за свой грех приведет к Господу для жертвы за грех самку из отары – овцу или козу. Тогда священник совершит для него отпущение за грех.

7Если ему не по средствам принести овцу, пусть принесет Господу двух горлиц или двух молодых голубей как расплату за свой грех: одного в жертву за грех, а другого в жертву всесожжения. 8Пусть он отдаст их священнику, который сначала принесет жертву за грех. Он свернет птице голову, не отрывая ее до конца, 9и окропит кровью жертвы за грех сторону жертвенника. Остальную кровь нужно выцедить к основанию жертвенника. Это – жертва за грех. 10Потом священник принесет другую птицу в жертву всесожжения, как велит обычай, и совершит для него отпущение за грех, который он совершил, и будет прощен.

11Если ему не по средствам принести двух горлиц или двух молодых голубей, он должен принести за свой проступок десятую часть ефы5:11 Вероятно, около 2 л. лучшей муки в жертву за грех. Пусть он не льет на муку масло и не кладет сверху ладана, ведь это – жертва за грех. 12Пусть он принесет ее к священнику, который возьмет из нее пригоршню как памятную часть и сожжет на жертвеннике вместе с огненными жертвами Господу. Это – жертва за грех. 13Так священник совершит для него отпущение за любой из грехов, которыми он согрешил, и он будет прощен. Остаток жертвы принадлежит священнику, как в случае с хлебным приношением».

Жертва повинности

14Господь сказал Моисею:

15– Если человек совершит проступок, согрешив по неведению против какой-либо из Господних святынь, он должен привести к Господу в расплату барана из отары без изъяна, имеющего соответствующую стоимость в серебре, по установленной мере святилища5:15 Букв.: «в серебряных шекелях, шекелях святилища». Шекель святилища – стандартная мера, которой пользовались священники шатра и храма, то есть около 11,5 г.. Это жертва повинности. 16Он должен возместить за святыню, против которой согрешил, добавить к этому пятую часть ее стоимости и отдать священнику, который совершит для него отпущение бараном жертвы повинности, и он будет прощен.

17Если человек согрешит и сделает то, что запрещено в какой-либо из Господних заповедей, даже если он не знает этого, он виновен и подлежит наказанию. 18Он должен привести к священнику барана из отары, должной стоимости и без изъяна для жертвы повинности. Тогда священник совершит для него отпущение за проступок, который он совершил по неведению, и он будет прощен. 19Это жертва повинности – человек провинился перед Господом.