Levitiko 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 5:1-19

1“ ‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.

2“ ‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.

3“ ‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.

4“ ‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.

5“ ‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo. 6Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.

7“ ‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza. 8Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu, 9kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo. 10Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.

11“ ‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo. 12Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo. 13Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’ ”

Chopereka Chopepesera Kupalamula

14Yehova anawuza Mose kuti, 15“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula. 16Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.

17“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa. 18Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. 19Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

New International Reader’s Version

Leviticus 5:1-19

1“ ‘Suppose someone has been called as a witness to something they have seen or learned about. Then if they do not tell what they know, they have sinned. And they will be held responsible for it.

2“ ‘Or suppose someone touches something not “clean.” It could be the dead bodies of wild animals or of livestock. Or it could be the dead bodies of creatures that move along the ground. Even though those people are not aware that they touched them, they have become “unclean.” And they are guilty. 3Or suppose they touch something “unclean” that comes from a human being. It could be anything that would make them “unclean.” Suppose they are not aware that they touched it. When they find out about it, they will be guilty. 4Or suppose someone makes a promise to do something without thinking it through. It does not matter what they promised. It does not matter whether they made the promise without thinking about it carefully. And suppose they are not aware that they did not think it through. When they find out about it, they will be guilty. 5When someone is guilty in any of those ways, they must admit they have sinned. 6They must bring a sin offering to pay for the sin they have committed. They must bring to the Lord a female lamb or goat from the flock. The priest will sacrifice the animal. That will pay for the person’s sin.

7“ ‘Suppose they can’t afford a lamb. Then they must get two doves or two young pigeons. They must bring them to the Lord to pay for their sin. One of them is for a sin offering. The other is for a burnt offering. 8They must bring them to the priest. The priest will offer the one for the sin offering first. He must twist its head. But he must not twist it off completely. 9Then he must splash some of the blood of the sin offering against the side of the altar. He must empty out the rest of the blood at the bottom of the altar. It is a sin offering. 10Then the priest will offer the other bird as a burnt offering. He must do it in the way the law requires. That will pay for the sin they have committed. And they will be forgiven.

11“ ‘But suppose they can’t afford two doves or two young pigeons. Then they must bring three and a half pounds of the finest flour as an offering for their sin. It is a sin offering. They must not put olive oil or incense on it. That is because it is a sin offering. 12They must bring it to the priest. The priest must take a handful of it. He must burn that part on the altar. It will be a reminder that all good things come from the Lord. The priest must burn it on top of the food offerings presented to the Lord. It is a sin offering. 13In that way the priest will pay for any of the sins they have committed. And they will be forgiven. The rest of the offering will belong to the priest. It is the same as in the case of the grain offering.’ ”

Rules for Guilt Offerings

14The Lord spoke to Moses. He said, 15“Suppose someone is unfaithful to me and sins. And they do it without meaning to. Here is how they sin against me or my priests. They refuse to give the priests one of the holy things set apart for them. Then they must bring me a ram from the flock. It must not have any flaws. It must be worth the required amount of silver. The silver must be weighed out in keeping with the standard weights that are used in the sacred tent. The ram is a guilt offering. It will pay for their sin. 16They must also pay for the holy thing they refused to give. They must add a fifth of its value to it. They must give all of it to the priest. The priest will pay for their sin with the ram. It is a guilt offering. And they will be forgiven.

17“Suppose someone sins by doing something I command them not to do. Even though they do not know it, they are guilty. They will be held responsible for it. 18They must bring to the priest a ram from the flock as a guilt offering. It must not have any flaws. And it must be worth the required amount of money. The priest will sacrifice the animal. That will pay for what they have done wrong without meaning to. And they will be forgiven. 19It is a guilt offering. They have been guilty of doing wrong against me.”