Levitiko 4 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 4:1-35

Nsembe Yopepesera Tchimo

1Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 2“Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:

3“ ‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake. 4Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova. 5Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 6Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika. 7Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 8Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo. 9Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo 10monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza. 11Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo, 12kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.

13“ ‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu. 14Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 15Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova. 16Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 17Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga. 18Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 19Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa, 20ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa. 21Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.

22“ ‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula. 23Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake. 24Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo. 25Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo. 26Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.

27“ ‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula. 28Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo. 29Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 30Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo. 31Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.

32“ ‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema. 33Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 34Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo. 35Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.

New International Reader’s Version

Leviticus 4:1-35

Rules for Sin Offerings

1The Lord spoke to Moses. He said, 2“Speak to the Israelites. Tell them, ‘Suppose someone sins without meaning to. And that person does something the Lord commands us not to do.

3“ ‘Suppose it is the anointed priest who sins. And suppose he brings guilt on the people. Then he must bring a young bull to the Lord. It must not have any flaws. He must bring it as a sin offering for the sin he has committed. 4He must bring the bull to the entrance to the tent of meeting in the sight of the Lord. He must place his hand on its head. He must kill it there in the sight of the Lord. 5Then the anointed priest must take some of the bull’s blood. He must carry it into the tent of meeting. 6He must dip his finger into the blood. He must sprinkle some of it seven times in the sight of the Lord. He must do it in front of the curtain of the Most Holy Room. 7Then the priest must put some of the blood on the horns of the altar for burning incense. The horns stick out from the upper four corners of the altar. The incense burned on that altar has a sweet smell. The altar stands in front of the Lord in the tent of meeting. The priest must pour out the rest of the bull’s blood at the bottom of the altar for burnt offerings. That altar stands at the entrance to the tent. 8He must remove all the fat from the bull for the sin offering. It includes the fat that is connected to the inside parts. 9It includes both kidneys with the fat on them next to the lower back muscles. It also includes the long part of the liver. He must remove all of it together with the kidneys. 10He must remove it in the same way the fat is removed from an ox sacrificed as a friendship offering. Then the priest must burn all of it on the altar for burnt offerings. 11But the bull’s hide must be taken away. So must all its meat. So must its head and legs. And so must its inside parts and guts. 12In other words, all the rest of the bull must be taken away. The priest must take it outside the camp. He must take it to a “clean” place. He must take it to the place where the ashes are thrown. Then he must burn it there in a wood fire on a pile of ashes.

13“ ‘Or suppose the whole community of Israel sins without meaning to. They do something the Lord commands us not to do. Suppose they realize their guilt. 14And suppose their sin becomes known. Then they must bring a young bull as a sin offering. They must offer it in front of the tent of meeting. 15The elders of the community must place their hands on the bull’s head in the sight of the Lord. The bull must be killed in the sight of the Lord. 16Then the anointed priest must take some of the bull’s blood into the tent of meeting. 17He must dip his finger into the blood. He must sprinkle it seven times in the sight of the Lord. He must do it in front of the curtain. 18He must put some of the blood on the horns that stick out from the upper four corners of the altar. The altar stands in front of the Lord in the tent of meeting. The priest must pour out the rest of the blood at the bottom of the altar for burnt offerings. That altar stands at the entrance to the tent. 19He must remove all the fat from the bull. He must burn it on the altar. 20He must do the same thing with that bull as he did with the bull for the sin offering. When he does, he will pay for the sin of the community. And they will be forgiven. 21Then he must take the bull outside the camp. He must burn it just as he burned the first bull. It is the sin offering for the whole community.

22“ ‘Or suppose a leader sins without meaning to. He disobeys any of the commands of the Lord his God. 23And suppose he realizes his guilt and his sin becomes known. Then he must bring an offering. It must be a male goat. It must not have any flaws. 24He must place his hand on the goat’s head. He must kill it. He must do it at the place where the animals for burnt offerings are killed in the sight of the Lord. His offering is a sin offering. 25Then the priest must dip his finger into some of the blood of the sin offering. He must put it on the horns that stick out from the upper four corners of the altar for burnt offerings. He must pour out the rest of the blood at the bottom of the altar. 26He must burn all the fat on the altar. He must burn it in the same way he burned the fat of the friendship offering. When he does, he will pay for the sin of the leader. And the leader will be forgiven.

27“ ‘Or suppose someone in the community sins without meaning to. They disobey any of the Lord’s commands. 28And suppose they realize their guilt and their sin becomes known. Then they must bring an offering for the sin they have committed. It must be a female goat. It must not have any flaws. 29They must place their hand on the head of the animal for the sin offering. It must be killed at the place where the animals for burnt offerings are killed. 30Then the priest must dip his finger into some of the blood. He must put it on the horns that stick out from the upper four corners of the altar for burnt offerings. He must pour out the rest of the blood at the bottom of the altar. 31They must remove all the fat in the same way the fat is removed from the friendship offering. The priest must burn it on the altar. Its smell pleases the Lord. When the priest burns the offering, he will pay for their sin. And they will be forgiven.

32“ ‘Suppose someone brings a lamb as their sin offering. Then they must bring a female animal. It must not have any flaws. 33They must place their hand on its head. They must kill it as a sin offering. They must do it at the place where the animals for burnt offerings are killed. 34Then the priest must dip his finger into some of the blood of the sin offering. He must put it on the horns that stick out from the upper four corners of the altar for burnt offerings. He must pour out the rest of the blood at the bottom of the altar. 35They must remove all the fat in the same way the fat is removed from the lamb for the friendship offering. The priest must burn it on the altar on top of the food offerings presented to the Lord. When he does, he will pay for the sin they have committed. And they will be forgiven.