Levitiko 4 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 4:1-35

Nsembe Yopepesera Tchimo

1Yehova anayankhula ndi Mose kuti, 2“Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:

3“ ‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake. 4Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova. 5Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 6Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika. 7Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 8Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo. 9Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo 10monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza. 11Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo, 12kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.

13“ ‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu. 14Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano. 15Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova. 16Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano. 17Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga. 18Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano. 19Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa, 20ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa. 21Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.

22“ ‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula. 23Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake. 24Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo. 25Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo. 26Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.

27“ ‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula. 28Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo. 29Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 30Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo. 31Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.

32“ ‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema. 33Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza. 34Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo. 35Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.

Священное Писание

Левит 4:1-35

Жертва за грех

1Вечный сказал Мусе:

2– Скажи исраильтянам: «Если кто-то согрешит по неведению, сделав то, что запрещено в каком-либо из повелений Вечного; 3если согрешит помазанный4:3 Посредством обряда помазания человек посвящался на определённое служение. Такого помазания удостаивались пророки, цари и священнослужители (см. гл. 8). священнослужитель, наводя вину на народ, – то пусть согрешивший приведёт к Вечному молодого быка без изъяна в жертву за свой грех. 4Пусть он поставит быка у входа в шатёр встречи, положит руку ему на голову и заколет его перед Вечным. 5Пусть помазанный священнослужитель возьмёт кровь быка и внесёт в шатёр встречи. 6Пусть он обмакнёт палец в кровь и покропит ею семь раз перед Вечным, перед завесой Святая Святых. 7Пусть священнослужитель помажет кровью рога жертвенника для возжигания благовоний перед Вечным в шатре встречи. Остальную кровь быка пусть выльет к основанию жертвенника для всесожжений у входа в шатёр встречи. 8Пусть он вынет из молодого быка, принесённого в жертву за грех, весь жир – тот, что покрывает внутренности или прилегает к ним, 9обе почки с жиром, который на них и который возле бёдер, и сальник с печени, всё это он вынет вместе с почками – 10как удаляют жир из вола4:10 Или: «из коровы»., которого приносят в жертву примирения. Пусть священнослужитель сожжёт это на жертвеннике для всесожжений. 11Но шкуру и мясо быка, а также голову и ноги, требуху и нечистоты в кишках – 12всё, что остаётся от быка, – пусть он вынесет за лагерь, на чистое место, куда высыпают пепел, и сожжёт в пламени дров.

13Если весь народ Исраила согрешит по неведению, сделав то, что запрещено в каком-либо из повелений Вечного, – даже если народ сам того не знает, – то он виновен. 14Когда грех, который он совершил, станет известен, общество должно привести молодого быка для жертвы за грех и поставить его перед шатром встречи. 15Пусть старейшины общества возложат руки на голову быка и заколют его перед Вечным. 16Пусть помазанный священнослужитель внесёт кровь быка в шатёр встречи. 17Он обмакнёт палец в кровь и семь раз покропит ею перед Вечным, перед завесой. 18Пусть он помажет кровью рога жертвенника, который перед Вечным в шатре встречи. Остальную кровь пусть он выльет к основанию жертвенника для всесожжений у входа в шатёр встречи. 19Он вынет из него весь жир и сожжёт его на жертвеннике, 20и сделает с этим быком то же, что и с быком жертвы за грех. Так священнослужитель очистит народ, и народ будет прощён. 21Затем он вынесет молодого быка за лагерь и сожжёт его так же, как и первого. Это жертва за грех народа.

22Если вождь согрешит по неведению, сделав то, что запрещено в каком-либо из повелений Вечного, его Бога, то он виновен. 23Когда откроется ему грех, который он совершил, он должен принести в жертву козла без изъяна. 24Пусть он положит руку на голову козла и заколет его там, где закалывают перед Вечным жертвы всесожжения. Это жертва за грех. 25Пусть священнослужитель возьмёт пальцем кровь жертвы за грех и помажет ею рога жертвенника для всесожжений, а остальную кровь выльет к основанию жертвенника. 26Он сожжёт на жертвеннике весь жир, подобно жиру жертвы примирения. Так священнослужитель очистит вождя от греха его, и вождь будет прощён.

27Если кто-нибудь из народа согрешит по неведению, сделав то, что запрещено в каком-либо из повелений Вечного, то он виновен. 28Когда откроется ему грех, который он совершил, он должен принести за него в жертву козу без изъяна. 29Пусть он положит руку на голову жертвы за грех и заколет её на месте, где закалывают жертвы для всесожжений. 30Пусть священнослужитель возьмёт пальцем кровь и помажет ею рога жертвенника для всесожжений, а остальную кровь выльет к основанию жертвенника. 31Он вынет весь жир так же, как удаляют жир из жертвы примирения, и сожжёт его на жертвеннике в благоухание, приятное Вечному. Так священнослужитель очистит любого человека из народа, и тот будет прощён.

32Если он приносит в жертву за грех ягнёнка, то пусть принесёт самку без изъяна. 33Пусть он положит руку ей на голову и принесёт её в жертву за грех на том месте, где закалывают жертву для всесожжения. 34Пусть священнослужитель возьмёт пальцем кровь жертвы за грех и помажет ею рога жертвенника для всесожжений, а остальную кровь выльет к основанию жертвенника. 35Он вынет весь жир так же, как удаляют жир из ягнёнка жертвы примирения, и сожжёт его на жертвеннике вместе с огненными жертвами Вечному. Так священнослужитель очистит его от греха, который он совершил, и он будет прощён.