Levitiko 3 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 3:1-17

Nsembe Yachiyanjano

1“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, ndipo choperekacho nʼkukhala ngʼombe yayimuna kapena yayikazi, ikhale yopanda chilema. 2Munthuyo asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo, ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ansembe, ana a Aaroni, awaze magazi mbali zonse za guwalo. 3Pa nsembe yachiyanjanopo, ayenera kupatula zamʼkati mwa nyamayo ndi mafuta onse amene amakuta zamʼkati kupereka nsembe ya chakudya kwa Yehova. 4Apatulenso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake omwe ndiponso mafuta okuta chiwindi amene achotsedwa pamodzi ndi impsyo zija. 5Ndipo ana a Aaroni atenthe zimenezi pa guwa, pamwamba pa chopereka chopsereza chimene chili pa nkhuni zoyakazo. Imeneyi ndi nsembe yotentha pa moto, ya fungo lokomera Yehova.

6“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, choperekacho chikhale nkhosa yayimuna kapena yayikazi yopanda chilema. 7Ngati apereka nsembe ya mwana wankhosa, abwere naye pamaso pa Yehova. 8Asanjike dzanja lake pamutu pa nkhosayo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magaziwo mbali zonse za guwalo. 9Pa nsembe yachiyanjanopo ayenera kuchotsa ndi kubweretsa: mafuta a nkhosayo, mchira wake wonse wonona atawudulira mʼtsinde pafupi ndi fupa la msana, zamʼkati zonse ndi mafuta onse amene akuta ziwalo zamʼkatimo, 10impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta amene akuta impsyozo, msonga ya chiwindi imene idzachotsedwere limodzi ndi impsyozo. 11Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya chotentha pa moto choperekedwa kwa Yehova.

12“ ‘Ngati munthuyo apereka mbuzi ngati nsembe, abwere nayo kwa Yehova. 13Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magazi ake mbali zonse za guwa. 14Tsono pa nsembe yoti iwotchedwe kukhala nsembe chakudya ya Yehova, achotse ndi kubweretsa: mafuta onse amene amaphimba zamʼkati kapena mafuta onse a mʼkatimo, 15impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse omwe akuta impsyozo ndi msonga ya chiwindi imene adzachotsera pamodzi ndi impsyo zija. 16Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya cha Yehova, chowotcha pa moto ndiponso cha fungo lokomera Yehova. Mafuta onse ndi a Yehova.

17“ ‘Limeneli likhale lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse kuti musadzadye mafuta kapena magazi kulikonse kumene mudzakhale.’ ”

New Russian Translation

Левит 3:1-17

Жертва примирения

1«Когда кто-то приносит в жертву примирения животное из крупного скота, все равно, самца или самку, – он должен поставить перед Господом животное без изъяна. 2Пусть он положит руку на голову жертвы и заколет ее у входа в шатер собрания. Затем священники, сыновья Аарона, окропят кровью жертвенник со всех сторон. 3Пусть он принесет из жертвы примирения в огненную жертву Господу весь жир, покрывающий внутренности или прилегающий к ним, 4обе почки с жиром, который на них и который возле бедер, и сальник с печени; все это он вынет вместе с почками. 5Пусть сыновья Аарона сожгут это на жертвеннике на горящих дровах вместе с жертвой всесожжения. Это будет огненная жертва, благоухание, приятное Господу.

6Если он приносит Господу в жертву примирения животное из мелкого скота, пусть принесет самца или самку без изъяна. 7Если он приносит ягненка, пусть поставит его перед Господом. 8Пусть положит руку на голову жертвы, заколет ее перед шатром собрания, и сыновья Аарона окропят кровью жертвенник со всех сторон. 9Пусть он принесет из жертвы примирения в огненную жертву Господу ее жир: весь курдюк, срезанный у нижнего позвонка, весь жир, покрывающий внутренности или прилегающий к ним, 10обе почки с жиром, который на них и который возле бедер, и сальник с печени; все это он вынет вместе с почками. 11Священник сожжет это на жертвеннике как пищу – огненную жертву Господу.

12Если жертвующий приносит в жертву козу, пусть поставит ее перед Господом. 13Пусть он положит руку ей на голову, заколет ее перед шатром собрания, и сыновья Аарона окропят кровью жертвенник со всех сторон. 14Пусть из своего приношения он принесет в огненную жертву Господу весь жир, покрывающий внутренности или прилегающий к ним, 15обе почки с жиром, который на них и который возле бедер, и сальник с печени; все это он вынет вместе с почками. 16Священник сожжет это на жертвеннике как пищу – приношение огнем, приятное благоухание. Весь жир принадлежит Господу.

17Это – вечное установление для грядущих поколений; где бы вы ни жили, не ешьте ни жира, ни крови».