Levitiko 3 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 3:1-17

Nsembe Yachiyanjano

1“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, ndipo choperekacho nʼkukhala ngʼombe yayimuna kapena yayikazi, ikhale yopanda chilema. 2Munthuyo asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo, ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ansembe, ana a Aaroni, awaze magazi mbali zonse za guwalo. 3Pa nsembe yachiyanjanopo, ayenera kupatula zamʼkati mwa nyamayo ndi mafuta onse amene amakuta zamʼkati kupereka nsembe ya chakudya kwa Yehova. 4Apatulenso impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta ake omwe ndiponso mafuta okuta chiwindi amene achotsedwa pamodzi ndi impsyo zija. 5Ndipo ana a Aaroni atenthe zimenezi pa guwa, pamwamba pa chopereka chopsereza chimene chili pa nkhuni zoyakazo. Imeneyi ndi nsembe yotentha pa moto, ya fungo lokomera Yehova.

6“ ‘Ngati munthu apereka nsembe ya chiyanjano kwa Yehova, choperekacho chikhale nkhosa yayimuna kapena yayikazi yopanda chilema. 7Ngati apereka nsembe ya mwana wankhosa, abwere naye pamaso pa Yehova. 8Asanjike dzanja lake pamutu pa nkhosayo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magaziwo mbali zonse za guwalo. 9Pa nsembe yachiyanjanopo ayenera kuchotsa ndi kubweretsa: mafuta a nkhosayo, mchira wake wonse wonona atawudulira mʼtsinde pafupi ndi fupa la msana, zamʼkati zonse ndi mafuta onse amene akuta ziwalo zamʼkatimo, 10impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta amene akuta impsyozo, msonga ya chiwindi imene idzachotsedwere limodzi ndi impsyozo. 11Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya chotentha pa moto choperekedwa kwa Yehova.

12“ ‘Ngati munthuyo apereka mbuzi ngati nsembe, abwere nayo kwa Yehova. 13Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphere pa khomo la tenti ya msonkhano. Ndipo ana a Aaroni awaze magazi ake mbali zonse za guwa. 14Tsono pa nsembe yoti iwotchedwe kukhala nsembe chakudya ya Yehova, achotse ndi kubweretsa: mafuta onse amene amaphimba zamʼkati kapena mafuta onse a mʼkatimo, 15impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse omwe akuta impsyozo ndi msonga ya chiwindi imene adzachotsera pamodzi ndi impsyo zija. 16Wansembe awotche zonsezi pa guwa. Ichi ndi chakudya cha Yehova, chowotcha pa moto ndiponso cha fungo lokomera Yehova. Mafuta onse ndi a Yehova.

17“ ‘Limeneli likhale lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse kuti musadzadye mafuta kapena magazi kulikonse kumene mudzakhale.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

利未記 3:1-17

獻平安祭的條例

1「如果有人用牛獻作平安祭,必須在耶和華面前獻上毫無殘疾的公牛或母牛。 2獻祭者要把手放在牛頭上,在會幕門口宰牛。祭司——亞倫的子孫要把牛血灑在祭壇四周。 3獻祭者要從平安祭中獻上火祭給耶和華。他要取出遮蓋內臟的脂肪和內臟上的脂肪、 4兩個腎臟和腎臟上靠近腰部的脂肪以及肝葉。 5祭司要把這一切放在祭壇燃燒的木柴上和燔祭一起焚燒,作為蒙耶和華悅納的馨香火祭。

6「如果用羊作祭物向耶和華獻平安祭,必須獻毫無殘疾的公羊或母羊。 7如果獻的是綿羊羔,獻祭者要把羊羔帶到耶和華面前, 8將手放在羊頭上,在會幕前宰殺。亞倫的子孫要把羊羔的血灑在祭壇四周。 9獻祭者要從平安祭中取出脂肪作為火祭獻給耶和華。他要從靠近脊椎骨處取下整條肥尾巴、遮蓋內臟的脂肪、 10兩個腎臟和腎臟上靠近腰部的脂肪以及肝葉。 11祭司要把這一切放在祭壇上焚燒,作為獻給耶和華的火祭。

12「如果獻的是山羊,獻祭者要把山羊帶到耶和華面前, 13將手放在羊頭上,在會幕門口宰殺。祭司要把羊血灑在祭壇四周。 14-15獻祭者要取出遮蓋內臟的脂肪和內臟上的脂肪、兩個腎臟和腎臟上面靠近腰部的脂肪以及肝葉,作為火祭獻給耶和華。 16祭司要把這一切放在祭壇上焚燒,作為蒙耶和華悅納的馨香火祭。所有的脂肪都屬於耶和華。 17你們無論住在哪裡,都不可吃脂肪和血,這是你們世代永遠要遵守的條例。」