Levitiko 26 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 26:1-46

Mphotho ya Kumvera

1“ ‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

2“ ‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.

3“ ‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga, 4ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake. 5Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.

6“ ‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo. 7Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu. 8Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.

9“ ‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu. 10Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano. 11Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu. 12Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga. 13Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.

Chilango Chakusamvera

14“ ‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa, 15ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa, 16Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya. 17Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.

18“ ‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 19Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa. 20Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.

21“ ‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu. 22Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.

23“ ‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine, 24Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu. 25Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu. 26Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.

27“ ‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine, 28pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 29Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi. 30Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu. 31Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu. 32Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa. 33Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja. 34Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake. 35Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.

36“ ‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa. 37Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu. 38Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani. 39Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.

40“ ‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane, 41zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo, 42Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo. 43Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga. 44Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 45Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’ ”

46Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.

New Russian Translation

Левит 26:1-46

Благословения за послушание

(Втор. 7:12-16; 28:1-14)

1«Не делайте себе идолов, не ставьте себе ни изваяний, ни священных столбов и не кладите в вашей земле резных камней, чтобы поклоняться им. Я – Господь, ваш Бог.

2Храните Мои субботы и чтите Мое святилище. Я – Господь.

3Если вы будете следовать Моим установлениям и прилежно исполнять Мои повеления, 4Я пошлю вам дождь в срок, и земля будет давать урожай, а деревья в поле плодоносить. 5Молотьба зерна у вас будет длиться до сбора винограда, а сбор винограда – до посева. Вы будете досыта есть и безопасно жить в вашей земле.

6Я пошлю вам мир на землю: спите спокойно, и никто вас не потревожит. Я прогоню из этой земли диких зверей, и меч не пройдет по вашей стране. 7Когда вы будете преследовать врагов, они падут от меча перед вами. 8Пятеро из вас прогонят сотню, а сто – десять тысяч. Враги падут от меча перед вами.

9Я посмотрю на вас милостиво, сделаю вас плодовитыми, размножу вас и буду хранить Мой завет с вами. 10Вы еще будете есть прошлогодние запасы, когда вам придется выбрасывать их, чтобы освободить место для новых. 11Я поставлю среди вас Мое жилище и не стану гнушаться вас. 12Я буду ходить среди вас и буду вашим Богом, а вы будете Моим народом. 13Я – Господь, ваш Бог, Который вывел вас из Египта, чтобы вам больше не быть рабами у египтян. Я сокрушил ярмо рабства, бывшее на вас, и позволил вам идти с гордо поднятой головой».

Проклятия за непослушание

(Втор. 28:15-68)

14«Но если вы не будете слушать Меня и не будете исполнять все эти повеления, 15если вы отвергнете Мои установления и будете гнушаться Моими законами, если не исполните все Мои повеления, расторгая завет со Мной, 16то Я сделаю вот что: Я наведу на вас внезапный ужас: чахотку и лихорадку, от которых меркнет в глазах и угасает жизнь. Вы будете сеять напрасно: урожай съедят ваши враги. 17Я обращу Мое лицо против вас, и ваши враги разобьют вас. Ненавидящие вас станут повелевать вами, и вы побежите даже тогда, когда за вами не будет погони.

18Если и после этого вы не послушаете Меня, Я накажу вас за ваши грехи в семь раз сильнее. 19Я сломлю вашу упрямую гордость и сделаю небо над вами железным, а землю под вами бронзовой. 20Вы растратите силы напрасно, потому что ваша земля не принесет урожая, а деревья на ней не будут плодоносить.

21Если вы останетесь Мне врагами и не захотите слушать Меня, то за ваши грехи Я умножу ваши беды семикратно. 22Я нашлю на вас диких зверей, и они лишат вас детей, истребят ваш скот и сделают вас такими малочисленными, что ваши дороги запустеют.

23Если и после этого вы не исправитесь и останетесь Мне врагами, 24то и Я стану вам врагом и покараю вас за ваши грехи в семь раз сильнее. 25Мстя за расторгнутый завет, Я обрушу на вас меч, а когда вы укроетесь в городах, пошлю на вас мор, и вы попадете в руки врагов. 26Я лишу вас хлеба, и десять женщин будут печь хлеб в одной печи. Хлеб вам будут выдавать по весу; вы будете есть, но не наедитесь.

27Если и после этого вы не станете слушать Меня и останетесь Мне врагами, 28то и Я стану вам врагом и в гневе накажу вас за ваши грехи в семь раз сильнее. 29Вы будете есть плоть своих сыновей и дочерей.

30Я разрушу ваши святилища на возвышенностях26:30 Святилища на возвышенностях – евр.: «бамот»; также в других местах Ветхого Завета., сокрушу кадильные жертвенники и повергну ваши трупы на обломки ваших идолов и возгнушаюсь вами. 31Я разорю ваши города, опустошу места поклонения лжебогам и не буду вкушать приятное благоухание ваших жертв. 32Я опустошу землю так, что ваши враги, которые поселятся на ней, ужаснутся. 33Я рассею вас между народами и буду преследовать вас с обнаженным мечом. Ваша земля будет опустошена, а города разорены. 34Тогда земля будет наслаждаться своими субботними годами все время26:34 Или: «возместит себе за свои субботние года во все время»., когда будет лежать в запустении, пока вы будете в краю ваших врагов. Тогда земля будет отдыхать и наслаждаться своими субботами. 35Все время, что она будет оставлена, земля будет отдыхать за те субботы, когда вы на ней жили.

36А сердца уцелевших в землях их врагов Я сделаю такими боязливыми, что звук гонимого ветром листа будет обращать их в бегство. Они побегут, словно от меча, и упадут, хотя за ними не будет погони. 37Они будут спотыкаться друг о друга, словно спасаясь от меча, хотя за ними не будет погони. У вас не будет силы подняться на врагов. 38Вы погибнете между народами; вражеская земля пожрет вас. 39Уцелевшие погибнут во вражеских землях за свои грехи и за грехи своих отцов.

40Но если они признают свои грехи и грехи своих отцов – как они предавали Меня и враждовали со Мной, 41за что и Я ополчился на них и отвел их в землю их врагов, если их необрезанные сердца26:41 Люди с необрезанными сердцами – это метафора, обозначающая людей непокорных Богу. смирятся и они заплатят за свой грех, 42то Я вспомню Свой завет с Иаковом, Свой завет с Исааком и Свой завет с Авраамом и вспомню эту землю. 43Ведь земля будет оставлена ими и будет наслаждаться своими субботними годами, когда будет лежать в запустении, без них, пока они будут платить за свои грехи, за то, что дерзнули отвергнуть Мои установления и презреть Мои установления. 44Но даже так, когда они будут во вражеской земле, Я не отвергну их и не вознегодую на них, чтобы не погубить их до конца и не нарушить Свой завет с ними. Я – Господь, их Бог. 45Ради них Я вспомню завет с их предками, которых Я вывел из Египта на глазах у народов, чтобы быть их Богом: Я – Господь».

46Таковы установления, законы и правила, которые Господь установил через Моисея на горе Синай между Собой и израильтянами.