Levitiko 26 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 26:1-46

Mphotho ya Kumvera

1“ ‘Musadzipangire mafano ndipo musayimike chifanizo chosema kapena mwala woti mudzipembedza. Musayike mwala wosema mʼdziko mwanu kuti muziwugwadira. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

2“ ‘Muzisunga Masabata anga ndipo muzilemekeza malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova.

3“ ‘Mukamayenda motsata malangizo anga ndi kumvera mosamalitsa malamulo anga, 4ndidzakupatsani mvula pa nyengo yake. Nthaka yanu idzabala zokolola zake, ndipo mitengo ya mʼmunda idzabala zipatso zake. 5Mudzakhala mukupuntha tirigu mpaka nthawi yothyola mphesa, ndipo mudzakhala mukuthyola mphesa mpaka nthawi yodzala. Mudzadya chakudya chanu mpaka kukhuta ndipo mudzakhala mʼdziko lanu mwamtendere.

6“ ‘Ndidzabweretsa mtendere mʼdziko lanu, ndipo muzidzagona popanda wokuopsezani. Ndidzachotsa nyama zakuthengo zoopsa mʼdziko mwanu, ndipo mʼdzikomo simudzakhala nkhondo. 7Mudzapirikitsa adani anu, ndipo mudzawagonjetsa ndi lupanga pamaso panu. 8Anthu asanu mwa inu adzapirikitsa anthu 100, ndipo anthu 100 mwa inu adzathamangitsa anthu 10,000, ndipo adani anuwo mudzawagonjetsa ndi lupanga.

9“ ‘Ndidzakukumbukirani ndi kukupatsani ana ambiri ndi kukuchulukitsani. Ndidzasunga pangano langa ndi inu. 10Mudzakhala mukudyabe chakudya chogonera ndipo mudzachotse chakudyacho mʼnkhokwe kuti mupezemo malo woyika chakudya china chatsopano. 11Ndidzakhala pakati panu, ndipo sindidzayipidwa nanu. 12Ine ndidzayendayenda pakati panu ndipo ndidzakhala Mulungu wanu. Inu mudzakhala anthu anga. 13Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti musakhalenso akapolo a Aigupto. Ndinadula mipiringidzo ya goli lanu ndi kukuthandizani kuti muziyenda momasuka.

Chilango Chakusamvera

14“ ‘Koma mukadzapanda kundimvera ndi kuphwanya malamulo anga onsewa, 15ndipo ngati mudzanyoza malangizo anga ndi kunyansidwa ndi malamulo anga, ndi kulephera kumvera zonse zimene ndakulamulani, ndi kuswa pangano langa, 16Ine ndidzakuchitirani izi: ndidzabweretsa zoopsa zadzidzidzi monga chifuwa chachikulu chowondetsa ndiponso malungo amene adzawononga maso ndi kufowoketsa moyo wanu. Mudzangovutika kudzala mbewu zanu chifukwa adani anu adzazidya. 17Ndidzakufulatirani, kotero kuti adani anu adzakugonjetsani. Odana nanu adzakulamulirani ndipo inu muzidzagothawa popanda wokupirikitsani.

18“ ‘Ngati simudzandimvera mutaona zonsezi, ndidzakulanganinso mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 19Ndidzathyola mphamvu zanu zimene mukunyadirazo, ndipo ndidzasandutsa mitambo kuti ikhale yowuma ngati chitsulo, ndiponso nthaka yanu kuti ikhale ngati mkuwa. 20Mphamvu zanu zidzapita pachabe chifukwa nthaka yanu sidzabala kanthu, ngakhale mitengo yake sidzabala zipatso zake.

21“ ‘Ngati mudzapitirira kutsutsana nane ndi kukana kundimvera, ndidzachulukitsa masautso anu kasanu ndi kawiri molingana ndi machimo anu. 22Ndidzabweretsa zirombo zolusa pakati panu, ndipo zidzakulandani ana anu ndi kuwononga ngʼombe zanu. Choncho zidzachepetsa chiwerengero chanu kotero kuti mʼnjira mwanu simudzapita anthu.

23“ ‘Mukadzapanda kutembenukira kwa Ine ngakhale nditakulangani motere, ndi kumachitabe zotsutsana ndi Ine, 24Ine mwini ndidzalimbana nanu, ndipo ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha machimo anu. 25Ndipo ndidzabweretsa lupanga pa inu ndi kukulangani chifukwa chophwanya pangano langa. Mukadzasonkhana mʼmizinda yanu, ndidzatumiza miliri pakati panu ndipo ndidzakuperekani mʼmanja mwa adani anu. 26Ndikadzachepetsa buledi wanu, akazi khumi adzaphika buledi wawo mu uvuni umodzi, ndipo adzakugawirani bulediyo pangʼonopangʼono. Choncho mudzadya koma wosakhuta.

27“ ‘Mukadzapanda kundimvera ngakhale nditakulangani motere, ndi kumatsutsanabe ndi Ine, 28pamenepo ndidzalimbana nanu mwaukali, ndipo Ine mwini ndidzakulangani mochulukitsa kasanu ndi kawiri chifukwa cha kuchimwa kwanu. 29Mudzadya ana anu aamuna ndiponso mudzadya ana anu aakazi. 30Ine ndidzawononga malo anu opembedzera mafano a ku mapiri. Ndidzagwetsa maguwa anu ofukizira lubani, ndipo ndidzawunjika pamodzi mitembo ya mafano anu wopanda moyowo, ndipo ndidzanyansidwa nanu. 31Ndidzasandutsa mizinda yanu kukhala mabwinja ndi kuwononga malo anu wopatulika. Sindidzakondweranso ndi fungo lokoma la zopereka zanu. 32Ndidzawononga dziko kotero kuti adani anu mʼmenemo adzadabwa. 33Ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina ya anthu ndipo ndidzasolola lupanga langa ndi kukupirikitsani. Dziko lanu lidzawonongedwa, ndipo mizinda yanu idzasanduka mabwinja. 34Nthawi imeneyo nthaka idzasangalalira kuyipumitsa kwake nthawi yonse imene idzakhala yosalimidwa, pamene inu mudzakhala muli mʼdziko la adani anu. Pa nthawi imeneyo dziko lidzapumula ndi kukondwerera kulipumuza kwake. 35Nthawi zonse pamene dzikolo lidzakhala lopanda anthu, nthaka idzapumula. Mpumulo umenewu udzakhala umene nthakayo sinapumulepo pa nthawi zimene inu munkapumula muli mʼdzikomo.

36“ ‘Kunena za amene adzatsale, ndidzayika mantha mʼmitima mwawo mʼdziko la adani awo kotero kuti adzathawa ngakhale mtswatswa wa tsamba lowuluka ndi mphepo. Adzathawa ngati akuthawa lupanga, ndipo adzagwa pansi ngakhale padzakhale wopanda kuwapirikitsa. 37Iwo adzaphunthwitsana ngati akuthawa nkhondo, ngakhale padzakhale popanda wowapirikitsa. Choncho simudzatha kuyima pamaso pa adani anu. 38Mudzatheratu pakati pa mitundu ya anthu. Dziko la adani anu lidzakudyani. 39Ngakhale iwo amene adzatsale adzatheratu mʼdziko la adani awo chifukwa cha machimo awo ndi machimo a makolo awo.

40“ ‘Tsono adzawulula machimo awo ndi machimo a makolo awo, kusakhulupirika kwawo ndi mayendedwe awo otsutsana nane, 41zomwe zinandipangitsa kuwafulatira ndi kuwapereka mʼmanja mwa adani awo. Ndipo mitima yawo yowumayo ikadzadzichepetsa ndi kuvomera kulangidwa chifukwa cha machimo awo, 42Ine ndidzakumbukira pangano langa ndi Yakobo, pangano langa ndi Isake, pangano langa ndi Abrahamu. Ndidzakumbukiranso dzikolo. 43Pakuti adzasiya dziko lawo lopanda anthu, nthaka idzakondwerera zaka zake zoyipumuza pamene iwo kudzakhala kulibe. Koma adzalangidwa chifukwa cha machimo awo popeza anakana malamulo anga ndipo mitima yawo inkayipidwa nawo malangizo anga. 44Komabe ngakhale adzachite zonsezi ali mʼdziko la adani awo, Ine sindidzawakana kapena kuyipidwa nawo kwakuti nʼkuwawononga kwathunthu ndi kuthetsa pangano langa ndi iwo. Ine ndine Yehova Mulungu wawo. 45Koma powachitira chifundo, ndidzakumbukira pangano langa ndi makolo awo amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto mitundu ina ikuona kuti Ine ndikhale Mulungu wawo. Ine ndine Yehova.’ ”

46Amenewa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anawayika pakati pa Iye mwini ndi Aisraeli pa Phiri la Sinai kudzera mwa Mose.

New International Reader’s Version

Leviticus 26:1-46

Rewards for Obeying the Lord

1“ ‘Do not make statues of gods for yourselves. Do not set up a likeness of a god or a sacred stone for yourselves. Do not place a carved stone in your land and bow down in front of it. I am the Lord your God.

2“ ‘You must always keep my Sabbath days. Have respect for my sacred tent. I am the Lord.

3“ ‘Follow my rules. Be careful to obey my commands. 4Then I will send you rain at the right time. The ground will produce its crops. The trees will bear their fruit. 5You will continue to harvest your grain until you gather your grapes. You will continue to gather your grapes until you plant your crops. You will have all you want to eat. And you will live in safety in your land.

6“ ‘I will give you peace in the land. You will be able to sleep because no one will make you afraid. I will remove wild animals from the land. There will not be any war in your country. 7You will hunt down your enemies. You will kill them with your swords. 8Five of you will chase 100. And 100 of you will chase 10,000. You will kill your enemies with your swords.

9“ ‘I will bless you. I will give you many children so that there will be many of you. And I will be faithful to the covenant I made with you. 10You will still be eating last year’s crops when you will have to make room for new crops. 11I will live among you. I will not turn away from you. 12I will walk among you. I will be your God. And you will be my people. 13I am the Lord your God. I brought you out of Egypt. I did not want you to be slaves in Egypt anymore. I threw off your heavy load. I helped you walk with your heads held high.

Punishment for Not Obeying the Lord

14“ ‘On the other hand, suppose you do not listen to me. Suppose you do not carry out all my commands. 15Suppose you say no to my rules and turn away from my laws. And suppose you break my covenant by failing to carry out all my commands. 16Then here is what I will do to you. All at once I will bring terror on you. I will send sicknesses that will make you weak. I will send fever that will destroy your sight. It will slowly take your strength away. When you plant seeds, it will not do you any good. Instead, your enemies will eat what you have planted. 17I will turn against you. Then your enemies will win the battle over you. Those who hate you will rule over you. You will run away even when no one is chasing you.

18“ ‘After all that, suppose you still will not listen to me. Then I will punish you for your sins seven times. 19I will break down your stubborn pride. I will make the sky above you like iron, and it will not rain. I will make the ground under you like bronze, and you will not be able to farm it. 20You will work with all your strength, but it will not do you any good. That is because your soil will not produce any crops. The trees of your land will not bear any fruit.

21“ ‘Suppose you continue to be my enemy. And suppose you still refuse to listen to me. Then I will multiply your troubles many times because of your sins. 22I will send wild animals against you. They will kill your children. They will destroy your cattle. There will be so few of you left that your roads will be deserted.

23“ ‘After all those things, suppose you still do not accept my warnings. And suppose you continue to be my enemy. 24Then I myself will be your enemy. I will make you suffer again and again for your sins. 25I will send war against you to punish you for breaking my covenant. When you go back into your cities, I will send a plague among you. You will be handed over to your enemies. 26I will cut off your supply of bread. Ten women will need only one oven to bake your bread. They will weigh out the bread piece by piece. Even when you eat all of it, it will not be enough to satisfy you.

27“ ‘After all that, suppose you still do not listen to me. And suppose you continue to be my enemy. 28Then I will be angry with you. I will be your enemy. I myself will again punish you for your sins over and over. 29You will eat the dead bodies of your sons. You will also eat the dead bodies of your daughters. 30I will destroy the high places where you worship other gods. I will pull down your incense altars. I will pile up your dead bodies on the lifeless statues of your gods. And I will turn away from you. 31I will completely destroy your cities. I will destroy your places of worship. The pleasant smell of your offerings will not give me any delight. 32I myself will destroy your land so completely that your enemies who live there will be shocked. 33I will scatter you among the nations. I will pull out my sword and hunt you down. Your land and your cities will be completely destroyed. 34Then the deserted land will enjoy its sabbath years. It will rest. It will not be farmed. It will enjoy its sabbaths. But you will become prisoners in the country of your enemies. 35The land will rest the whole time it is deserted. It was not able to rest during the sabbaths you lived in it.

36“ ‘Some of you will be left in the lands of your enemies. I will fill your hearts with fear. The sound of a leaf blown by the wind will scare you away. You will run as if you were escaping from swords. You will fall down, even though no one is chasing you. 37You will trip over one another as if you were running away from the battle. You will run away, even though no one is chasing you. You will not be able to stand and fight against your enemies. 38While you are still scattered among the nations, you will die. The lands of your enemies will destroy you. 39You who are left in those lands will become weaker and weaker. You will die because of your sins and the sins of your people who lived before you.

40“ ‘But suppose you admit that both you and your people who lived before you have sinned. You admit the evil and dishonest things you have done against me. And you admit you have become my enemy. 41What you did made me become your enemy. I let your enemies take you into their land. But suppose you stop being stubborn. You stop being proud. And you pay for your sin. 42Then I will remember my covenant with Jacob. I will remember my covenant with Isaac. I will remember my covenant with Abraham. I will remember what I said to them about the land. 43You will leave the land. It will enjoy its sabbaths while it lies deserted because you are not there. You will pay for your sins because you said no to my laws. You turned away from my rules. 44But even after all that, I will not say no to you or turn away from you. I will not destroy you completely in the land of your enemies. I will not break my covenant with you. I am the Lord your God. 45Because of you, I will remember the covenant I made with the people of Israel who lived before you. I brought them out of Egypt to be their God. The nations saw me do it. I am the Lord.’ ”

46These are the orders, the laws and the rules of the covenant the Lord made on Mount Sinai. He made it between himself and the Israelites through Moses.