Levitiko 23 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 23:1-44

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.

Za Sabata

3“ ‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.

Za Paska ndi za Buledi Wopanda Yisiti

4“ ‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake: 5Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. 6Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 7Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse. 8Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’ ”

Za Zipatso Zoyambirira Kucha

9Yehova anawuza Mose kuti, 10“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu. 11Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata. 12Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova. 13Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka. 14Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

Chikondwerero cha Masabata

15“ ‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu. 16Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova. 17Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha. 18Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova. 19Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano. 20Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe. 21Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

22“ ‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Chikondwerero cha Malipenga

23Yehova anawuza Mose kuti, 24“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga. 25Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’ ”

Tsiku Lopepesera Machimo

26Yehova anawuza Mose kuti, 27“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova. 28Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 29Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake. 30Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake. 31Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale. 32Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”

Chikondwerero cha Misasa

33Yehova anawuza Mose kuti, 34“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova. 35Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa. 36Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.

37(“ ‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku. 38Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)

39“ ‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso. 40Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri. 41Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri. 42Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa 43kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

44Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

New International Version

Leviticus 23:1-44

The Appointed Festivals

1The Lord said to Moses, 2“Speak to the Israelites and say to them: ‘These are my appointed festivals, the appointed festivals of the Lord, which you are to proclaim as sacred assemblies.

The Sabbath

3“ ‘There are six days when you may work, but the seventh day is a day of sabbath rest, a day of sacred assembly. You are not to do any work; wherever you live, it is a sabbath to the Lord.

The Passover and the Festival of Unleavened Bread

4“ ‘These are the Lord’s appointed festivals, the sacred assemblies you are to proclaim at their appointed times: 5The Lord’s Passover begins at twilight on the fourteenth day of the first month. 6On the fifteenth day of that month the Lord’s Festival of Unleavened Bread begins; for seven days you must eat bread made without yeast. 7On the first day hold a sacred assembly and do no regular work. 8For seven days present a food offering to the Lord. And on the seventh day hold a sacred assembly and do no regular work.’ ”

Offering the Firstfruits

9The Lord said to Moses, 10“Speak to the Israelites and say to them: ‘When you enter the land I am going to give you and you reap its harvest, bring to the priest a sheaf of the first grain you harvest. 11He is to wave the sheaf before the Lord so it will be accepted on your behalf; the priest is to wave it on the day after the Sabbath. 12On the day you wave the sheaf, you must sacrifice as a burnt offering to the Lord a lamb a year old without defect, 13together with its grain offering of two-tenths of an ephah23:13 That is, probably about 7 pounds or about 3.2 kilograms; also in verse 17 of the finest flour mixed with olive oil—a food offering presented to the Lord, a pleasing aroma—and its drink offering of a quarter of a hin23:13 That is, about 1 quart or about 1 liter of wine. 14You must not eat any bread, or roasted or new grain, until the very day you bring this offering to your God. This is to be a lasting ordinance for the generations to come, wherever you live.

The Festival of Weeks

15“ ‘From the day after the Sabbath, the day you brought the sheaf of the wave offering, count off seven full weeks. 16Count off fifty days up to the day after the seventh Sabbath, and then present an offering of new grain to the Lord. 17From wherever you live, bring two loaves made of two-tenths of an ephah of the finest flour, baked with yeast, as a wave offering of firstfruits to the Lord. 18Present with this bread seven male lambs, each a year old and without defect, one young bull and two rams. They will be a burnt offering to the Lord, together with their grain offerings and drink offerings—a food offering, an aroma pleasing to the Lord. 19Then sacrifice one male goat for a sin offering23:19 Or purification offering and two lambs, each a year old, for a fellowship offering. 20The priest is to wave the two lambs before the Lord as a wave offering, together with the bread of the firstfruits. They are a sacred offering to the Lord for the priest. 21On that same day you are to proclaim a sacred assembly and do no regular work. This is to be a lasting ordinance for the generations to come, wherever you live.

22“ ‘When you reap the harvest of your land, do not reap to the very edges of your field or gather the gleanings of your harvest. Leave them for the poor and for the foreigner residing among you. I am the Lord your God.’ ”

The Festival of Trumpets

23The Lord said to Moses, 24“Say to the Israelites: ‘On the first day of the seventh month you are to have a day of sabbath rest, a sacred assembly commemorated with trumpet blasts. 25Do no regular work, but present a food offering to the Lord.’ ”

The Day of Atonement

26The Lord said to Moses, 27“The tenth day of this seventh month is the Day of Atonement. Hold a sacred assembly and deny yourselves,23:27 Or and fast; similarly in verses 29 and 32 and present a food offering to the Lord. 28Do not do any work on that day, because it is the Day of Atonement, when atonement is made for you before the Lord your God. 29Those who do not deny themselves on that day must be cut off from their people. 30I will destroy from among their people anyone who does any work on that day. 31You shall do no work at all. This is to be a lasting ordinance for the generations to come, wherever you live. 32It is a day of sabbath rest for you, and you must deny yourselves. From the evening of the ninth day of the month until the following evening you are to observe your sabbath.”

The Festival of Tabernacles

33The Lord said to Moses, 34“Say to the Israelites: ‘On the fifteenth day of the seventh month the Lord’s Festival of Tabernacles begins, and it lasts for seven days. 35The first day is a sacred assembly; do no regular work. 36For seven days present food offerings to the Lord, and on the eighth day hold a sacred assembly and present a food offering to the Lord. It is the closing special assembly; do no regular work.

37(“ ‘These are the Lord’s appointed festivals, which you are to proclaim as sacred assemblies for bringing food offerings to the Lord—the burnt offerings and grain offerings, sacrifices and drink offerings required for each day. 38These offerings are in addition to those for the Lord’s Sabbaths and23:38 Or These festivals are in addition to the Lord’s Sabbaths, and these offerings are in addition to your gifts and whatever you have vowed and all the freewill offerings you give to the Lord.)

39“ ‘So beginning with the fifteenth day of the seventh month, after you have gathered the crops of the land, celebrate the festival to the Lord for seven days; the first day is a day of sabbath rest, and the eighth day also is a day of sabbath rest. 40On the first day you are to take branches from luxuriant trees—from palms, willows and other leafy trees—and rejoice before the Lord your God for seven days. 41Celebrate this as a festival to the Lord for seven days each year. This is to be a lasting ordinance for the generations to come; celebrate it in the seventh month. 42Live in temporary shelters for seven days: All native-born Israelites are to live in such shelters 43so your descendants will know that I had the Israelites live in temporary shelters when I brought them out of Egypt. I am the Lord your God.’ ”

44So Moses announced to the Israelites the appointed festivals of the Lord.