Levitiko 23 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 23:1-44

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.

Za Sabata

3“ ‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.

Za Paska ndi za Buledi Wopanda Yisiti

4“ ‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake: 5Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba. 6Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 7Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse. 8Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’ ”

Za Zipatso Zoyambirira Kucha

9Yehova anawuza Mose kuti, 10“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu. 11Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata. 12Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova. 13Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka. 14Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

Chikondwerero cha Masabata

15“ ‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu. 16Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova. 17Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha. 18Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova. 19Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano. 20Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe. 21Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.

22“ ‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

Chikondwerero cha Malipenga

23Yehova anawuza Mose kuti, 24“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga. 25Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’ ”

Tsiku Lopepesera Machimo

26Yehova anawuza Mose kuti, 27“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova. 28Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 29Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake. 30Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake. 31Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale. 32Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”

Chikondwerero cha Misasa

33Yehova anawuza Mose kuti, 34“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova. 35Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa. 36Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.

37(“ ‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku. 38Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)

39“ ‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso. 40Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri. 41Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri. 42Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa 43kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’ ”

44Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Levítico 23:1-44

Calendario de fiestas solemnes

1El Señor le ordenó a Moisés 2que les dijera a los israelitas: «Estas son las fiestas que yo he establecido, y a las que habéis de convocar como fiestas solemnes en mi honor. Yo, el Señor, las establecí.

Celebración del sábado

3»Trabajaréis durante seis días, pero el séptimo día es de reposo, es un día de fiesta solemne en mi honor, en el que no haréis ningún trabajo. Dondequiera que viváis, será sábado consagrado al Señor.

Fiesta de la Pascua

23:4-8Éx 12:14-20; Nm 28:16-25; Dt 16:1-8

4»Estas son las fiestas que el Señor ha establecido, las fiestas solemnes en su honor que deberéis convocar en las fechas señaladas para ellas:

5»La Pascua del Señor comienza el día catorce del mes primero, a la hora del crepúsculo. 6El día quince del mismo mes comienza la fiesta de los Panes sin levadura en honor al Señor. Durante siete días comeréis pan sin levadura. 7El primer día celebraréis una fiesta solemne en su honor; ese día no haréis ningún trabajo. 8Durante siete días presentaréis al Señor ofrendas por fuego, y el séptimo día celebraréis una fiesta solemne en su honor; ese día no haréis ningún trabajo».

Fiesta de las Primicias

9El Señor le ordenó a Moisés 10que les dijera a los israelitas: «Cuando hayáis entrado en la tierra que os voy a dar, y seguéis la mies, deberéis llevar al sacerdote una gavilla de las primeras espigas que cosechéis. 11El sacerdote mecerá la gavilla ante el Señor para que os sea aceptada. La mecerá a la mañana siguiente del sábado. 12Ese mismo día sacrificaréis vosotros un cordero de un año, sin defecto, como holocausto al Señor. 13También presentaréis cuatro kilos23:13 cuatro kilos. Lit. dos décimas (de efa); también en v. 17. de harina fina mezclada con aceite, como ofrenda de cereal, ofrenda por fuego, de aroma grato al Señor, y un litro23:13 un litro. Lit. un cuarto de hin. de vino como ofrenda de libación. 14No comeréis pan, ni grano tostado o nuevo, hasta el día en que traigáis esta ofrenda a vuestro Dios. Este será un estatuto perpetuo para todos vuestros descendientes, dondequiera que habitéis.

Fiesta de las Semanas

23:15-22Nm 28:26-31; Dt 16:9-12

15»A partir del día siguiente al sábado, es decir, a partir del día en que traigáis la gavilla de la ofrenda mecida, contaréis siete semanas completas. 16En otras palabras, contaréis cincuenta días incluyendo la mañana siguiente al séptimo sábado; entonces presentaréis al Señor una ofrenda de grano nuevo. 17Desde vuestro lugar de residencia le llevaréis al Señor, como ofrenda mecida de las primicias, dos panes hechos con cuatro kilos de flor de harina, cocidos con levadura. 18Junto con el pan deberéis presentar siete corderos de un año, sin defecto, un novillo y dos carneros. Seréis, junto con vuestras ofrendas de cereal y vuestras ofrendas de libación, un holocausto al Señor, una ofrenda presentada por fuego, de aroma grato al Señor. 19Luego sacrificaréis un macho cabrío como ofrenda por el pecado, y dos corderos de un año como sacrificio de comunión. 20El sacerdote mecerá los dos corderos, junto con el pan de las primicias. Son una ofrenda mecida ante el Señor, una ofrenda consagrada al Señor y reservada para el sacerdote. 21Ese mismo día convocaréis a una fiesta solemne en honor al Señor, y en ese día no haréis ningún trabajo. Este será un estatuto perpetuo para todos vuestros descendientes, dondequiera que habitéis.

22»Cuando llegue el tiempo de la cosecha, no seguéis hasta el último rincón del campo ni recojáis todas las espigas que queden de la mies. Dejadlas para los pobres y los extranjeros. Yo soy el Señor vuestro Dios».

Fiesta de las Trompetas

23:23-25Nm 29:1-6

23El Señor le ordenó a Moisés 24que les dijera a los israelitas: «El primer día del séptimo mes será para vosotros un día de reposo, una conmemoración con toques de trompeta, una fiesta solemne en honor al Señor. 25Ese día no haréis ningún trabajo, sino que presentaréis al Señor ofrendas por fuego».

El día del Perdón

23:26-32Lv 16:2-34; Nm 29:7-11

26El Señor le dijo a Moisés: 27«El día diez del mes séptimo es el día del Perdón. Celebraréis una fiesta solemne en honor al Señor, y ayunaréis y le presentaréis ofrendas por fuego. 28En ese día no haréis ningún tipo de trabajo, porque es el día del Perdón, cuando se hace expiación por vosotros ante el Señor vuestro Dios. 29Cualquiera que no observe el ayuno será eliminado de su pueblo. 30Si alguien hace algún trabajo en ese día, yo mismo lo eliminaré de su pueblo. 31Por tanto, no haréis ningún trabajo. Este será un estatuto perpetuo para todos vuestros descendientes, dondequiera que habiten. 32Será para vosotros un sábado de solemne reposo, y deberéis observar el ayuno. Este sábado lo observaréis desde la tarde del día nueve del mes hasta la tarde siguiente».

Fiesta de las Enramadas

23:33-43Nm 29:12-39; Dt 16:13-17

33El Señor le ordenó a Moisés 34que les dijera a los israelitas: «El día quince del mes séptimo comienza la fiesta de las Enramadas en honor al Señor, la cual durará siete días. 35El primer día se celebrará una fiesta solemne en honor al Señor. Ese día no haréis ningún trabajo. 36Durante siete días le presentaréis al Señor ofrendas por fuego. Al octavo día celebraréis una fiesta solemne en honor al Señor y volveréis a presentarle ofrendas por fuego. Es una fiesta solemne; ese día no haréis ningún trabajo.

37»Estas son las fiestas que el Señor ha establecido, y a las que vosotros habréis de convocar como fiestas solemnes en su honor, para presentarle ofrendas por fuego, holocaustos, ofrendas de cereal, y sacrificios y ofrendas de libación, tal como está prescrito para cada día. 38Todas estas fiestas son adicionales a los sábados del Señor y a los tributos y ofrendas votivas o voluntarias que vosotros le presentéis.

39»A partir del día quince del mes séptimo, después de que hayáis recogido los frutos de la tierra, celebraréis durante siete días la fiesta del Señor. El primer día y el octavo serán de descanso especial. 40El primer día tomaréis frutos de los mejores árboles, ramas de palmera, de árboles frondosos y de sauces de los arroyos, y durante siete días os regocijaréis en presencia del Señor vuestro Dios. 41Cada año, durante siete días, celebraréis esta fiesta en honor al Señor. La celebraréis en el mes séptimo. Este será un estatuto perpetuo para las generaciones venideras. 42Durante siete días viviréis bajo enramadas. Todos los israelitas nativos vivirán bajo enramadas, 43para que vuestros descendientes sepan que yo hice vivir así a los israelitas cuando los saqué de Egipto. Yo soy el Señor vuestro Dios».

44Así anunció Moisés a los israelitas las fiestas establecidas por el Señor.