Levitiko 20 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 20:1-27

Zilango za Tchimo

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aisraeli kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala mu Israeli wopereka mwana wake kwa Moleki ayenera kuphedwa. Anthu a mʼdera lakelo amuphe ndi miyala. 3Munthu ameneyo ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anzake.’ Popereka mwana wake kwa Moleki, wadetsa malo anga wopatulika ndi kuyipitsa dzina langa loyera. 4Ngati anthu a mʼderalo achita ngati sakumuona munthuyo pamene akupereka mwana wake kwa Moleki ndi kusamupha, 5Ineyo ndidzamufulatira pamodzi ndi banja lake. Ndidzawachotsa pakati pa anthu anzawo onse amene anamutsatira, nadziyipitsa okha popembedza Moleki.”

6“ ‘Ngati munthu adzapita kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena kwa owombeza, nadziyipitsa powatsatira iwowo, Ine ndidzamufulatira ndi kumuchotsa pakati pa anthu anzake.

7“ ‘Chifukwa chake dzipatuleni ndi kukhala woyera popeza Ine ndine Yehova Mulungu wanu. 8Ndipo sungani malangizo anga ndi kuwatsata. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani.

9“ ‘Munthu aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa. Magazi ake adzakhala pamutu pake chifukwa iye watemberera abambo kapena amayi ake.

10“ ‘Ngati munthu wachita chigololo ndi mkazi wa mnzake, mwamunayo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa.

11“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa abambo ake, wachititsa manyazi abambo ake. Munthuyo pamodzi ndi mkaziyo ayenera kuphedwa. Magazi awo adzakhala pa mitu pake.

12“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

13“ ‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

14“ ‘Ngati munthu akwatira mkazi, nakwatiranso amayi ake, chimenecho ndi chinthu choyipa kwambiri. Mwamunayo pamodzi ndi akaziwo ayenera kutenthedwa pa moto kuti chinthu choyipa chotere chisapezekenso pakati panu.

15“ ‘Ngati mwamuna agonana ndi nyama, iye ayenera kuphedwa, ndipo muyeneranso kupha nyamayo.

16“ ‘Ngati mkazi agonana ndi nyama, aphedwe pamodzi ndi nyamayo. Mkaziyo ndi nyamayo ayenera kuphedwa, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.

17“ ‘Ngati munthu akakwatira mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake, kapena mwana wamkazi wa amayi ake, ndipo iwo nʼkugonana, ndiye kuti achita chinthu chochititsa manyazi. Onse awiri ayenera kuchotsedwa pa gulu la abale awo. Tsono popeza munthuyo wachititsa manyazi mlongo wake, adzayenera kulandira chilango.

18“ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi pa nthawi yake yosamba, ndiye kuti wavula msambo wake, ndipo mkaziyo wadzivulanso. Onse awiri achotsedwe pakati pa anthu anzawo.

19“ ‘Musagonane ndi mchemwali wa amayi anu kapena abambo anu, pakuti kutero ndi kuchititsa manyazi mʼbale wanu. Nonse mudzalipira mlandu wanu.

20“ ‘Ngati munthu agonana ndi azakhali ake, munthuyo wachititsa manyazi a malume ake. Onse adzalipira mlandu wawo. Onsewo adzafa wopanda mwana.

21“ ‘Munthu akakwatira mkazi wa mchimwene wake ndiye kuti wachita chinthu chonyansa. Wachititsa manyazi mʼbale wakeyo. Onse awiriwo adzakhala wopanda mwana.

22“ ‘Nʼchifukwa chake muzisunga malangizo anga onse ndi malamulo anga ndipo muwatsatire kuti ku dziko limene Ine ndikupita nanu kuti mukakhalemo lisakakusanzeni. 23Musatsanzire miyambo ya mitundu ya anthu imene ndi kuyipirikitsa inu mukufika. Chifukwa iwo anachita zinthu zonsezi, ndipo Ine ndinanyansidwa nawo. 24Koma Ine ndinakuwuzani kuti, ‘Mudzatenga dziko lawo. Ine ndidzakupatsani dzikolo kuti likhale cholowa chanu, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’ Ine ndine Yehova Mulungu wanu amene ndakupatulani pakati pa mitundu yonse ya anthu.

25“ ‘Chifukwa chake muzisiyanitsa pakati pa nyama zoyeretsedwa ndi nyama zodetsedwa ndiponso pakati pa mbalame zoyeretsedwa ndi mbalame zodetsedwa. Musadzidetse pakudya nyama iliyonse kapena mbalame, kapena chilichonse chimene chimakwawa pansi, chimene Ine ndachipatula kuti chikhale chodetsedwa kwa inu. 26Muzikhala woyera pamaso panga chifukwa Ine Yehova, ndine woyera ndipo ndakupatulani pakati pa anthu a mitundu yonse kuti mukhale anthu anga.

27“ ‘Mwamuna kapena mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa kapena wanyanga pakati panu ayenera kuphedwa. Muwagende ndi miyala, ndipo magazi awo adzakhala pa mitu pawo.’ ”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Левит 20:1-27

Наказания за грех

1Вечный сказал Мусо:

2– Скажи исроильтянам: «Любого исроильтянина или живущего в Исроиле чужеземца, который отдаёт Молоху своего ребёнка, нужно предать смерти. Народ Исроила должен забить его камнями. 3Я обращу Своё лицо против него и исторгну его из народа; ведь, отдавая своих детей Молоху, он осквернил Моё святилище и обесчестил Моё святое имя. 4Если народ Исроила закроет глаза на то, что кто-то отдал своего ребёнка Молоху, и не предаст его смерти, 5то Я сам обращу Своё лицо против того человека и его семьи и исторгну их из народа – и его самого, и всех, кто следует за ним, блудя с Молохом.

6Я обращу Моё лицо против человека, который обращается к вызывателям умерших и к чародеям, нарушая верность Мне, следуя за ними, и Я исторгну его из народа.

7Освящайтесь и будьте святы, потому что Я – Вечный, ваш Бог. 8Соблюдайте Мои установления и следуйте им. Я – Вечный, Который освящает вас.

9Всякий, кто злословит отца или мать, должен быть предан смерти. Он злословил отца или мать – он сам виновен в своей гибели.

10Если мужчина ляжет с женой другого, то и изменника, и изменницу нужно предать смерти.

11Если мужчина переспит с женой отца20:11 Имеется в виду не мать данного человека, а другая жена его отца. – он опозорил отца. И мужчину, и женщину нужно предать смерти – они сами виновны в своей гибели.

12Если мужчина переспит со своей снохой, их обоих нужно предать смерти. Они сделали мерзость – они сами виновны в своей гибели.

13Если мужчина ляжет с мужчиной, как ложатся с женщиной, они оба сделали мерзость. Их нужно предать смерти – они сами виновны в своей гибели.

14Если мужчина женится и на дочери, и на её матери – это разврат. И его, и их нужно сжечь, чтобы среди вас не было разврата.

15Если мужчина совокупится с животным, его нужно предать смерти. Убейте и животное.

16Если женщина приблизится к животному для совокупления, убейте и женщину, и животное. Их нужно предать смерти – они сами виновны в своей гибели.

17Если мужчина женится на своей родной, единокровной или единоутробной сестре, и они совокупятся – это позор. Их нужно принародно изгнать. Он обесчестил сестру и подлежит наказанию.

18Если человек ляжет с женщиной во время её месячных и переспит с ней, то он обнажил источник её кровотечения, и она также открыла его. Их обоих нужно исторгнуть из народа.

19Не спи с сестрой матери или отца, потому что это бесчестие для близкой родни; вы оба будете виновны.

20Если человек переспит с женой дяди, он опозорил своего дядю. Развратники будут виновны; они умрут бездетными.

21Если человек переспит с женой своего брата – это нечистота; он опозорил брата. Они будут бездетными.

22Исполняйте все Мои установления и законы и соблюдайте их, чтобы земля, куда Я веду вас жить, не отторгла вас. 23Не следуйте обычаям народов, которые Я прогоняю от вас. За то, что они делали всё это, Я вознегодовал на них. 24Но вам Я сказал: „Вы завладеете их землёй. Я дам вам в наследие эту землю, где течёт молоко и мёд“. Я – Вечный, ваш Бог, Который отделил вас от народов.

25Отличайте чистых животных и птиц от нечистых. Не оскверняйте себя ни зверем, ни птицей, ни пресмыкающимся, которых Я велел вам считать нечистыми. 26Будьте святы предо Мной, потому что Я, Вечный, свят. Я отделил вас от народов, чтобы вы были Моими.

27Мужчину или женщину, которые будут вызывать умерших или чародействовать среди вас, нужно предать смерти. Забейте их камнями – они сами виновны в своей гибели».