Levitiko 17 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 17:1-16

Za Kusadya Magazi

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uza Aaroni ndi ana ake, pamodzi ndi Aisraeli onse kuti, ‘Chimene Yehova walamula ndi ichi: 3Mwisraeli aliyense amene apha ngʼombe, mwana wankhosa kapena mbuzi mu msasa kapena kunja kwa msasa, 4mʼmalo mobwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova ndi kuyipereka kuti ikhale nsembe ya Yehova, ameneyo wapalamula mlandu wa magazi, wakhetsa magazi ndipo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake. 5Izi zili choncho kuti Aisraeli azibwera ndi nyama zawo za nsembe zimene akanaphera ku malo kwina kulikonse. Aisraeli azibwera nazo nyamazo kwa Yehova, kwa wansembe wokhala pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo aziphere pomwepo kuti zikhale nsembe za chiyanjano. 6Wansembe awaze magazi ake pa guwa la Yehova limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano ndipo atenthe mafuta ake kuti atulutse fungo lokomera Yehova. 7Motero asadzapherenso nsembe fano la mbuzi limene amachita nalo zadama. Limeneli ndi lamulo la muyaya kwa iwo ndi mibado ya mʼtsogolo.’ ”

8“Uwawuze kuti, ‘Mwisraeli aliyense kapena mlendo amene amakhala pakati pawo akapereka nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse 9popanda kubwera nayo pa khomo la tenti ya msonkhano kudzayipereka pamaso pa Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati pa anthu anzake.’ ”

10“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene adya magazi, ndidzamufulatira ndipo ndidzamuchotsa pakati pa anthu anzake. 11Pakuti moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi, ndipo ndawupereka kwa inu kuti muzichitira mwambo wopepesera machimo a moyo wanu pa guwa. Pajatu magazi ndiwo amachotsa machimo chifukwa moyo uli mʼmenemo. 12Choncho ndikuwawuza Aisraeli kuti, ‘Pasapezeke aliyense wa inu wodya magazi, ngakhale mlendo wokhala pakati panu.’ ”

13“Mwisraeli aliyense kapena mlendo aliyense wokhala pakati panu amene amasaka ndi kupha nyama zakuthengo kapena mbalame zimene amadya, ataye magazi ake pansi ndi kuwakwirira ndi dothi, 14chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi ake. Nʼchifukwa chake ndinawawuza Aisraeli kuti, ‘Musamadye magazi a cholengedwa chilichonse, chifukwa moyo wa cholengedwa chilichonse uli mʼmagazi. Aliyense wodya magaziwo ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu anzake.

15“ ‘Munthu aliyense, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, amene amadya chilichonse chofa chokha, kapena chojiwa ndi zirombo, achape zovala zake ndi kusamba, komabe adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Kenaka adzakhala woyeretsedwa. 16Koma ngati sachapa zovala zake ndi kusamba, adzasenzabe machimo ake.’ ”

New International Version

Leviticus 17:1-16

Eating Blood Forbidden

1The Lord said to Moses, 2“Speak to Aaron and his sons and to all the Israelites and say to them: ‘This is what the Lord has commanded: 3Any Israelite who sacrifices an ox,17:3 The Hebrew word can refer to either male or female. a lamb or a goat in the camp or outside of it 4instead of bringing it to the entrance to the tent of meeting to present it as an offering to the Lord in front of the tabernacle of the Lord—that person shall be considered guilty of bloodshed; they have shed blood and must be cut off from their people. 5This is so the Israelites will bring to the Lord the sacrifices they are now making in the open fields. They must bring them to the priest, that is, to the Lord, at the entrance to the tent of meeting and sacrifice them as fellowship offerings. 6The priest is to splash the blood against the altar of the Lord at the entrance to the tent of meeting and burn the fat as an aroma pleasing to the Lord. 7They must no longer offer any of their sacrifices to the goat idols17:7 Or the demons to whom they prostitute themselves. This is to be a lasting ordinance for them and for the generations to come.’

8“Say to them: ‘Any Israelite or any foreigner residing among them who offers a burnt offering or sacrifice 9and does not bring it to the entrance to the tent of meeting to sacrifice it to the Lord must be cut off from the people of Israel.

10“ ‘I will set my face against any Israelite or any foreigner residing among them who eats blood, and I will cut them off from the people. 11For the life of a creature is in the blood, and I have given it to you to make atonement for yourselves on the altar; it is the blood that makes atonement for one’s life.17:11 Or atonement by the life in the blood 12Therefore I say to the Israelites, “None of you may eat blood, nor may any foreigner residing among you eat blood.”

13“ ‘Any Israelite or any foreigner residing among you who hunts any animal or bird that may be eaten must drain out the blood and cover it with earth, 14because the life of every creature is its blood. That is why I have said to the Israelites, “You must not eat the blood of any creature, because the life of every creature is its blood; anyone who eats it must be cut off.”

15“ ‘Anyone, whether native-born or foreigner, who eats anything found dead or torn by wild animals must wash their clothes and bathe with water, and they will be ceremonially unclean till evening; then they will be clean. 16But if they do not wash their clothes and bathe themselves, they will be held responsible.’ ”