Levitiko 16 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 16:1-34

Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo

1Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose. 2Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.

3“Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. 4Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi. 5Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.

6“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake. 7Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano. 8Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele. 9Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo. 10Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.

11“Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja. 12Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani. 13Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe. 14Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.

15“Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho. 16Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo. 17Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.

18“Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe. 19Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.

20“Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe. 21Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu. 22Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.

23“Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko. 24Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu. 25Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.

26“Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa. 27Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe. 28Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.

29“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu, 30chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova. 31Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya. 32Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika. 33Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.

34“Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.”

Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.

Thai New Contemporary Bible

เลวีนิติ 16:1-34

วันลบบาป

(ลนต.23:26-32; กดว.29:7-11)

1องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสหลังจากที่บุตรชายสองคนของอาโรนสิ้นชีวิตเมื่อพวกเขาเข้ามาหาองค์พระผู้เป็นเจ้า 2องค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสกับโมเสสว่า “จงเตือนอาโรนพี่ชายของเจ้าไม่ให้เข้าไปในอภิสุทธิสถานหลังม่านซึ่งอยู่เบื้องหน้าพระที่นั่งกรุณาที่อยู่บนหีบพันธสัญญาตามอำเภอใจ มิฉะนั้นเขาจะต้องตาย เพราะเราจะปรากฏในกลุ่มเมฆเหนือพระที่นั่งกรุณา

3“ต่อไปนี้เป็นข้อปฏิบัติในการที่อาโรนจะเข้าไปยังบริเวณสถานนมัสการ เขาจะต้องนำวัวหนุ่มสำหรับเป็นเครื่องบูชาไถ่บาปและแกะผู้สำหรับเป็นเครื่องเผาบูชาไป 4เขาต้องสวมเสื้อตัวในอันบริสุทธิ์ที่ทำด้วยผ้าลินินกับเครื่องแต่งกายชั้นในผ้าลินินที่ติดกับร่างกายของเขา คาดสายคาดเอวลินิน และโพกศีรษะด้วยผ้าลินิน นี่เป็นเครื่องแต่งกายอันบริสุทธิ์ ดังนั้นเขาต้องอาบน้ำก่อนที่จะสวมใส่ 5ให้เขารับแพะผู้สองตัวสำหรับเป็นเครื่องบูชาไถ่บาป และแกะผู้หนึ่งตัวสำหรับเป็นเครื่องเผาบูชาจากชุมชนอิสราเอล

6“ให้อาโรนถวายวัวหนุ่มหนึ่งตัวเป็นเครื่องบูชาไถ่บาป เพื่อลบบาปให้ตนเองและครอบครัว 7จากนั้นจะนำแพะสองตัวมาต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้าที่ทางเข้าเต็นท์นัดพบ 8เขาจะต้องจับฉลากสำหรับแพะทั้งสองนั้น ฉลากอันหนึ่งสำหรับองค์พระผู้เป็นเจ้า และอีกอันหนึ่งสำหรับแพะรับบาป16:8 คือแพะแห่งการขจัดออกภาษาฮีบรูว่าอาซาเซลเช่นเดียวกับข้อ 10 และ 26 9อาโรนจะถวายแพะตัวที่ใช้ถวายองค์พระผู้เป็นเจ้าเป็นเครื่องบูชาไถ่บาป 10แต่แพะที่ได้รับเลือกโดยฉลากให้เป็นแพะรับบาปจะถูกนำมาถวายทั้งที่ยังมีชีวิตต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้า เพื่อเป็นการลบบาป โดยส่งมันเข้าไปในถิ่นกันดารเป็นแพะรับบาป

11“อาโรนจะนำวัวหนุ่มมาฆ่าเป็นเครื่องบูชาไถ่บาปเพื่อลบบาปให้ตนเองและครอบครัว 12เขาจะเอากระถางไฟบรรจุถ่านคุโชนจากแท่นบูชาต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้าและกอบผงเครื่องหอมซึ่งบดละเอียดสองกำมือนำเข้าไปหลังม่าน 13เขาจะโรยเครื่องหอมบนไฟต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้าให้ควันเครื่องหอมปกคลุมทั่วพระที่นั่งกรุณาเหนือหีบพันธสัญญา เพื่อว่าเขาจะไม่ตาย 14เขาจะนำเลือดบางส่วนของวัวหนุ่มเข้าไปและใช้นิ้วพรมบนด้านหน้าของพระที่นั่งกรุณาเจ็ดครั้ง

15“แล้วอาโรนจะฆ่าแพะเป็นเครื่องบูชาไถ่บาปสำหรับประชากร และนำเลือดของมันเข้าไปหลังม่าน แล้วทำเช่นเดียวกับที่ทำกับเลือดวัวผู้คือ เขาจะพรมเลือดนั้นที่ข้างบนและข้างหน้าของพระที่นั่งกรุณา 16เขาจะลบบาปสำหรับอภิสุทธิสถานด้วยวิธีนี้เพราะมลทินและการกบฏของชาวอิสราเอล ไม่ว่าบาปของเขาจะเป็นอะไร เขาจะต้องทำอย่างเดียวกันนี้สำหรับเต็นท์นัดพบซึ่งอยู่ท่ามกลางพวกเขา ซึ่งแวดล้อมด้วยมลทินของพวกเขา 17ห้ามผู้ใดอยู่ในเต็นท์นัดพบขณะที่อาโรนเข้าไปทำการลบบาปในอภิสุทธิสถาน จนกว่าเขาจะออกมาอีกครั้งหลังจากลบบาปให้ตนเอง ให้ครอบครัวและชุมชนอิสราเอลทั้งหมดแล้ว

18“จากนั้นอาโรนจะไปยังแท่นบูชา คือต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้าและทำการลบบาปสำหรับแท่นนั้น เขาจะเอาเลือดวัวผู้และเลือดแพะบางส่วนทาที่เชิงงอนของแท่น 19แล้วเอานิ้วจุ่มเลือดพรมบนแท่นบูชาเจ็ดครั้ง เป็นการชำระแท่นนั้นให้บริสุทธิ์พ้นจากมลทินของชนอิสราเอล

20“เมื่ออาโรนลบบาปสำหรับอภิสุทธิสถาน เต็นท์นัดพบ และแท่นบูชาเสร็จแล้ว เขาจะนำแพะที่มีชีวิตตัวนั้นมา 21วางมือทั้งสองบนหัวแพะ สารภาพความชั่วร้ายและการละเมิดฝ่าฝืนของชนอิสราเอล ปลดเปลื้องบาปทั้งหมดลงบนแพะ แล้วมอบหมายให้ชายคนหนึ่งจูงแพะเข้าไปในถิ่นกันดาร 22แพะตัวนั้นจะแบกรับบาปทั้งหมดของเหล่าประชากรเข้าสู่ที่เปลี่ยว ชายผู้นั้นจะปล่อยมันไว้ในถิ่นกันดาร

23“จากนั้นให้อาโรนเข้าไปในเต็นท์นัดพบ ถอดชุดผ้าลินินซึ่งใช้สวมเข้าไปในอภิสุทธิสถานนั้นวางไว้ในเต็นท์นัดพบ 24แล้วอาบน้ำชำระกายในที่บริสุทธิ์ สวมเสื้อผ้าชุดปกติ แล้วออกไปถวายเครื่องเผาบูชาสำหรับตนเองและเครื่องเผาบูชาสำหรับประชากร เพื่อลบบาปให้ตนเองและประชากร 25เขาจะเผาไขมันของเครื่องบูชาไถ่บาปบนแท่นบูชาด้วย

26“ชายคนที่จูงแพะเข้าไปปล่อยในถิ่นกันดารเสร็จแล้ว ต้องอาบน้ำ ซักเสื้อผ้า แล้วกลับเข้ามาในค่ายพัก 27วัวหนุ่มและแพะซึ่งใช้เป็นเครื่องบูชาไถ่บาป ซึ่งอาโรนนำเลือดของมันเข้าไปในอภิสุทธิสถานเพื่อทำการลบบาป จะถูกนำไปเผาให้หมดนอกค่ายพัก รวมทั้งหนัง เนื้อ และไส้ 28แล้วผู้ทำหน้าที่เผาต้องซักเสื้อผ้าและอาบน้ำ และค่อยกลับมาที่ค่ายพัก

29“ต่อไปนี้เป็นข้อปฏิบัติถาวรสำหรับเจ้าคือ ห้ามเจ้าทำกิจธุระในวันที่สิบเดือนที่เจ็ด แต่จงบังคับตน16:29 หรือต้องอดอาหารเช่นเดียวกับข้อ 31 ไม่ว่าจะเป็นคนอิสราเอลโดยกำเนิดหรือเป็นคนต่างด้าวซึ่งอาศัยอยู่ในหมู่พวกเจ้า 30เพราะในวันนี้จะมีการลบบาปสำหรับเจ้า เพื่อชำระเจ้าให้สะอาด แล้วเจ้าจะสะอาดพ้นจากบาปทั้งสิ้นต่อหน้าองค์พระผู้เป็นเจ้า 31เป็นสะบาโตแห่งการหยุดพัก เจ้าต้องบังคับตน ถือเป็นข้อปฏิบัติถาวรสืบไปทุกชั่วอายุ 32ปุโรหิตซึ่งได้รับการเจิมและสถาปนาให้เป็นมหาปุโรหิตสืบทอดจากบิดาจะเป็นผู้ลบบาป เขาจะต้องสวมชุดบริสุทธิ์ที่ทำจากผ้าลินิน 33และลบบาปสำหรับอภิสุทธิสถาน เต็นท์นัดพบ และแท่นบูชา สำหรับปุโรหิตและประชากรทั้งปวงในชุมชน

34“นี่เป็นข้อปฏิบัติถาวรสำหรับเจ้าทั้งหลายสืบไปคือ ให้ลบบาปทั้งสิ้นสำหรับประชากรอิสราเอลปีละครั้ง”

และเขาก็ทำตามที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงบัญชาโมเสสไว้