Levitiko 10 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Levitiko 10:1-20

Imfa ya Nadabu ndi Abihu

1Ana a Aaroni, Nadabu ndi Abihu, aliyense anatenga chofukizira lubani chake nayikamo makala a moto ndi kuthiramo lubani. Iwo anapereka pamaso pa Yehova moto wachilendo, moto umene Yehova sanawalamule. 2Choncho moto unatuluka pamaso pa Yehova ndi kuwapsereza, ndipo anafa pamaso pa Yehova. 3Pamenepo Mose anawuza Aaroni kuti, “Pajatu Yehova ananena kuti,

“ ‘Kwa iwo amene amandiyandikira

ndidzaonetsa ulemerero wanga;

pamaso pa anthu onse

ndidzalemekezedwa.’ ”

Aaroni anakhala chete wosayankhula.

4Mose anayitana Misaeli ndi Elizafani, ana a Uzieli, abambo angʼono a Aaroni, ndipo anawawuza kuti, “Bwerani kuno mudzachotse abale anuwa pa malo wopatulika ndi kuwatulutsira kunja kwa msasa.” 5Choncho anabwera atavala minjiro yawo ndipo anawatenga ndi kuwatulutsa kunja kwa msasawo monga momwe Mose analamulira.

6Ndipo Mose anawuza Aaroni ndi ana ake Eliezara ndi Itamara kuti, “Musalileke tsitsi lanu nyankhalala ndipo musangʼambe zovala zanu kuti mungafe, ndi mkwiyo wa Yehova ungagwere anthu onsewa. Koma abale anu okha, kutanthauza fuko lonse la Israeli ndiwo ayenera kulira omwalira aja amene Yehova wawapsereza ndi moto. 7Musatuluke kunja kwa tenti ya msonkhano, mungafe, chifukwa munadzozedwa ndi mafuta a Yehova kukhala ansembe.” Choncho iwo anachita monga Mose ananenera.

8Pambuyo pake Yehova anayankhula ndi Aaroni nati, 9“Iwe ndi ana ako musamamwe vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa pamene mukulowa mu tenti ya msonkhano kuti mungafe. Ili ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. 10Muzisiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, pakati pa zinthu zodetsedwa ndi zinthu zoyeretsedwa, 11ndipo muyenera kuphunzitsa Aisraeli onse malamulo amene Yehova wakupatsani kudzera mwa Mose.”

12Mose anawuza Aaroni ndi ana ake otsalawo, Eliezara ndi Itamara kuti, “Tengani zopereka zachakudya zopanda yisiti zimene zatsala pa nsembe zopsereza za kwa Yehova ndipo muzidye pafupi ndi guwa pakuti ndi zopatulika kwambiri. 13Muzidye pa malo wopatulika chifukwa zimenezi ndi gawo lako ndi la ana ako pa zopereka zopsereza kwa Yehova. Izitu ndi zimene Yehova anandilamulira. 14Koma iwe pamodzi ndi ana ako aamuna ndi aakazi muzidya chidale chimene chinaweyulidwa ndi ntchafu zimene zinaperekedwa nsembe. Muzidye pamalo woyeretsedwa. Zimenezi zaperekedwa kwa iwe ndi ana ako monga gawo lanu pa zopereka zachiyanjano zimene apereka Aisraeli. 15Ntchafu imene inaperekedwayo ndi chidale chomwe chinaweyulidwacho abwere nazo pamodzi ndi nsembe ya mafuta ya Yehova yotentha pa moto, ndipo uziweyule kuti zikhale zopereka zoweyula pamaso pa Yehova. Zimenezi zizikhala zako ndi ana ako nthawi zonse monga walamulira Yehova.”

16Pambuyo pake Mose anafunafuna mbuzi ya nsembe yopepesera machimo koma anapeza kuti anayitentha kale. Apa Mose anakalipira Eliezara ndi Itamara, ana a Aaroni otsala aja nati, 17“Chifukwa chiyani simunadyere pamalo wopatulika nsembe yopepesera machimo ija? Kodi imene ija siyopatulika? Kodi Yehova sanapereke nyamayo kwa inu kuti muchotse machimo a mpingo wonse powachitira mwambo wa nsembe yopepesera machimo pamaso pa Yehova? 18Pakuti magazi ake sanalowe nawo ku Malo Wopatulika, mukanadya nyama ya mbuziyo pa malo wopatulikawo monga Yehova analamulira.”

19Aaroni anamuyankha Mose kuti, “Lero anthu apereka nsembe yawo yopepesera machimo ndiponso nsembe yawo yopsereza pamaso pa Yehova komabe zinthu zoterezi zandichitikira. Kodi Yehova akanakondwa ndikanadya nsembe yopepesera machimo lero?” 20Pamene Mose anamva zimenezi, anakhutira.

New Serbian Translation

3. Мојсијева 10:1-20

Ватра спаљује Надава и Авијуда

1Аронови синови, Надав и Авијуд, сваки узме своју кадионицу, у њих ставе ватру а на њу кад, па су принели пред Господом туђи огањ, супротно ономе што им је заповедио. 2Тада сиђе огањ од Господа и прогута их, те погину пред Господом. 3Тада Мојсије рече Арону: „То је оно што је Господ рекао: ’Показаћу своју светост преко оних који су ми близу, и прославићу се пред свим народом.’“ Арон је ћутао.

4Мојсије је позвао Мисаила и Елисафана, синове Озила, стрица Ароновог, па им је рекао: „Приступите и изнесите своју браћу испред Светиње на место изван табора.“ 5Они приступе и изнесу их у њиховим одорама изван табора, као што је Мојсије рекао.

6Потом Мојсије рече Арону и његовим синовима, Елеазару и Итамару: „Не рашчупавајте своју косу, и не раздирите своју одећу, да не погинете и да он не плане гневом на сву заједницу. А ваша браћа, сав дом Израиљев, могу да оплакују оне које је Господ спалио. 7Не напуштајте улаз Шатора од састанка да не погинете, јер је уље помазања Господњег на вама.“ Они су учинили како је Мојсије рекао.

8Господ рече Арону: 9„Немој пити вина и жестока пића, ни ти ни твоји синови, када улазите у Шатор од састанка, да не погинете. То је вечна уредба за ваше нараштаје, 10да бисте могли правити разлику између светог и несветог, и између нечистог и чистог, 11и да бисте учили Израиљце свим уредбама које им је Господ рекао преко Мојсија.“

12Мојсије рече Арону и његовим преосталим синовима, Елеазару и Итамару: „Узмите житну жртву што је остала од паљене жртве Господње, и једите је бесквасну поред жртвеника, јер је пресвета. 13Једите је на светом месту; то је део од паљене жртве Господње, који следује теби и твојим синовима, јер ми је тако заповеђено. 14А груди жртве дизанице и плећку жртвеног дара једите на чистом месту, ти, твоји синови и твоје ћерке; то је део од жртава мира израиљског народа, који следује теби и твојим синовима. 15Плећка жртвеног дара и груди жртве дизанице, заједно са деловима сала паљене жртве, нека се донесу ради приношења жртве дизанице пред Господом. То ће бити део који следује твојим синовима и теби довека, као што је Господ заповедио.“

16Онда се Мојсије распитао о јарцу – жртви за грех, а он већ спаљен! Разгневивши се на Елеазара и Итамара, Аронове преостале синове, рекао је: 17„Зашто нисте јели жртву за грех на светом месту, јер је пресвета?! Она вам је дана да уклони кривицу заједнице и да изврши за њих обред откупљења пред Господом. 18Пошто њена крв није била унесена у Светињу, требало је да је једете у Светињи, као што сам заповедио.“

19Арон одговори Мојсију: „Види, данас су принели своју жртву за грех и своју жртву свеспалницу пред Господом, а ево шта ме је задесило. Да сам данас јео жртву за грех, да ли би то угодило Господу?“ 20Кад је Мојсије то чуо, одобрио је то.