Hoseya 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 9:1-17

Chilango cha Israeli

1Iwe Israeli, usakondwere;

monga imachitira mitundu ina.

Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako;

umakonda malipiro a chiwerewere

pa malo aliwonse opunthira tirigu.

2Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu;

adzasowa vinyo watsopano.

3Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova.

Efereimu adzabwerera ku Igupto

ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.

4Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova,

kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo.

Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa;

onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa.

Chakudya ichi chidzakhala chodya okha,

sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.

5Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika;

pa masiku a zikondwerero za Yehova?

6Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko,

Igupto adzawasonkhanitsa,

ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda.

Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva,

ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.

7Masiku achilango akubwera,

masiku obwezera ali pafupi.

Israeli adziwe zimenezi.

Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri

ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri.

Mneneri amamuyesa chitsiru,

munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.

8Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga

ndiwo alonda a Efereimu,

koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse,

ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.

9Iwo azama mu zachinyengo

monga masiku a Gibeya.

Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo

ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.

10“Pamene ndinamupeza Israeli

zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu.

Nditaona makolo anu,

zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa.

Koma atafika ku Baala Peori,

anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi

ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.

11Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame.

Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.

12Ngakhale atalera ana

ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire.

Tsoka kwa anthuwo

pamene Ine ndidzawafulatira!

13Ndaona Efereimu ngati Turo,

atadzalidwa pa nthaka ya chonde.

Koma Efereimu adzatsogolera

ana ake kuti akaphedwe.”

14Inu Yehova, muwapatse.

Kodi mudzawapatsa chiyani?

Apatseni mimba yomangopita padera

ndi mawere owuma.

15“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala,

Ine ndinawada kumeneko.

Chifukwa cha machitidwe awo auchimo,

ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga.

Sindidzawakondanso;

atsogoleri awo onse ndi owukira.

16Efereimu wathedwa,

mizu yake yauma

sakubalanso zipatso.

Ngakhale atabereka ana,

Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”

17Mulungu wanga adzawakana

chifukwa sanamumvere Iye;

adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

何西阿書 9:1-17

何西阿宣佈對以色列的懲罰

1以色列啊,

不要歡喜快樂,

不要像外族人那樣歡喜快樂!

因為你對你的上帝不忠不貞,

在各麥場上喜愛賣淫得資財。

2但麥場上的穀物將不夠養活你們,

榨酒池裡也將缺乏新酒。

3你們將不能再住在耶和華的土地上。

以法蓮要返回埃及

亞述吃不潔之物。

4你們將不能再獻奠祭給耶和華,

你們的祭牲也不蒙悅納。

這些祭物如居喪之人的食物,

吃的人都被玷污。

你們的食物只能供自己吃,

不能帶進耶和華的殿。

5在耶和華所定的節期裡,

你們要做什麼呢?

6即使你們逃脫毀滅之災,

埃及人也要把你們聚集起來,

摩弗埋葬你們。

你們的珍貴銀器要散落在荊棘中,

你們的帳篷中要長滿蒺藜。

7以色列人受懲罰的日子近了,

遭報應的時候到了!

這點你們要知道。

你們罪惡深重,充滿憎恨,

以致你們說:

「先知是傻瓜,

被靈感動的人是瘋子。」

8先知為了上帝做以法蓮的守望者,

可是他走的路上佈滿網羅,

在他上帝的家裡遭人憎恨。

9你們敗壞至極,

恰如從前在基比亞的日子。

耶和華必記住你們的罪惡,

追討你們的罪債。

10耶和華說:

「昔日我看見以色列時,

像在荒野看見葡萄;

看見你們的祖先時,

像在無花果樹上看見初熟的果子。

但他們卻祭拜巴力·毗珥

把自己獻給可恥的偶像,

變得像他們所愛的偶像一樣可憎。

11以法蓮人的榮耀要如鳥飛逝,

你們將不能受孕,

不能懷胎,

也不能生育。

12你們縱然把孩子養大,

我也要奪去他們的性命,一個也不留。

我撇棄你們的時候,

你們就有禍了!

13我看見以法蓮栽種在草原上,美如泰爾

以法蓮卻要把孩子交給屠殺者。」

14耶和華啊,求你給他們——

你要給他們什麼呢?

求你使他們子宮流產,乳房乾癟。

15耶和華說:

「因他們在吉甲的一切惡行,

我已憎惡他們。

因他們的惡行,

我要將他們逐出我的家,

不再愛他們,

他們的首領都是悖逆之人。

16以法蓮要被擊打,

他們的根將枯乾,

再也不能結果。

就算他們能生兒育女,

我也要殺死他們心愛的孩子。」

17我的上帝必棄絕他們,

因為他們不聽從祂。

他們必在列國中流離飄泊。