Hoseya 6 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 6:1-11

Kusalapa kwa Israeli

1“Bwerani, tiyeni tibwerere kwa Yehova.

Iye watikhadzula,

koma adzatichiritsa.

Iye wativulaza,

koma adzamanga mabala athu.

2Pakapita masiku awiri adzatitsitsimutsa;

pa tsiku lachitatu Iye adzatiukitsa

kuti tikhale ndi moyo pamaso pake.

3Tiyeni timudziwe Yehova,

tiyeni tilimbike kumudziwa Iye.

Adzabwera kwa ife mosakayikira konse

ngati kutuluka kwa dzuwa;

adzabwera kwa ife ngati mvula ya mʼchilimwe,

ngati mvula ya nthawi yamphukira imene imakhathamiritsa nthaka.”

4Iwe Efereimu, kodi ndichite nawe chiyani?

Kodi ndichite nawe chiyani, iwe Yuda?

Chikondi chanu chili ngati nkhungu yammawa,

ngati mame a mmamawa amene amakamuka msanga.

5Choncho ndakuwazani ngati nkhuni kudzera mwa aneneri anga,

ndakuphani ndi mawu a pakamwa panga;

chigamulo changa chinangʼanima ngati mphenzi pa inu.

6Pakuti Ine ndimafuna chifundo osati nsembe,

ndi kudziwa Mulungu kulekana ndi nsembe zopsereza.

7Monga Adamu, anthuwa aphwanya pangano langa,

iwo sanakhulupirike kwa Ine.

8Giliyadi ndi mzinda wa anthu ochita zoyipa,

okhala ndi zizindikiro za kuphana.

9Monga momwe mbala zimadikirira anthu,

magulu a ansembe amachitanso motero;

iwo amapha anthu pa njira yopita ku Sekemu,

kupalamula milandu yochititsa manyazi.

10Ndaona chinthu choopsa kwambiri

mʼnyumba ya Israeli.

Kumeneko Efereimu akuchita zachiwerewere,

ndipo Israeli wadzidetsa.

11“Kunenanso za iwe Yuda,

udzakolola chilango.

“Pamene ndiwabwezere anthu anga zinthu zabwino.”

New International Version – UK

Hosea 6:1-11

Israel unrepentant

1‘Come, let us return to the Lord.

He has torn us to pieces

but he will heal us;

he has injured us

but he will bind up our wounds.

2After two days he will revive us;

on the third day he will restore us,

that we may live in his presence.

3Let us acknowledge the Lord;

let us press on to acknowledge him.

As surely as the sun rises,

he will appear;

he will come to us like the winter rains,

like the spring rains that water the earth.’

4‘What can I do with you, Ephraim?

What can I do with you, Judah?

Your love is like the morning mist,

like the early dew that disappears.

5Therefore I cut you in pieces with my prophets,

I killed you with the words of my mouth –

then my judgments go forth like the sun.6:5 The meaning of the Hebrew for this line is uncertain.

6For I desire mercy, not sacrifice,

and acknowledgment of God rather than burnt offerings.

7As at Adam,6:7 Or Like Adam; or Like human beings they have broken the covenant;

they were unfaithful to me there.

8Gilead is a city of evildoers,

stained with footprints of blood.

9As marauders lie in ambush for a victim,

so do bands of priests;

they murder on the road to Shechem,

carrying out their wicked schemes.

10I have seen a horrible thing in Israel:

there Ephraim is given to prostitution,

Israel is defiled.

11‘Also for you, Judah,

a harvest is appointed.

‘Whenever I would restore the fortunes of my people,