Yehova Ayimba Mlandu Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,
chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu
amene mumakhala mʼdzikoli:
“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi
mulibe kulabadira za Mulungu.
2Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.
Kuba ndi kuchita chigololo;
machimo achita kunyanya
ndipo akungokhalira kuphana.
3Chifukwa chake dziko likulira
ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;
zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,
wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,
pakuti anthu ako ali ngati anthu
amene amayimba mlandu wansembe.
5Mumapunthwa usana ndi usiku
ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.
Choncho ndidzawononga amayi anu.
6Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.
“Pakuti mwakana kudziwa,
Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;
chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,
Inenso ndidzayiwala ana anu.
7Ansembe ankati akachuluka
iwo ankandichimwiranso kwambiri;
iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8Amalemererapo pa machimo a anthu anga
ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.
Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,
ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10“Iwo azidzadya koma sadzakhuta;
azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,
chifukwa anasiya Yehova
kuti adzipereke 11ku zachiwerewere,
ku vinyo wakale ndi watsopano,
zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12za anthu anga.
Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo
ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.
Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;
iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri
ndi kufukiza lubani pa zitunda,
pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,
pamene pali mthunzi wabwino.
Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere
ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14“Ine sindidzalanga ana anu aakazi
pamene iwo adzachita zachiwerewere,
kapena akazi a ana anu
pamene adzachita zigololo.
Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,
ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.
Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,
Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.
“Usapite ku Giligala.
Usapite ku Beti-Aveni.
Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16Aisraeli ndi nkhutukumve,
ngosamva ngati ana angʼombe.
Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji
ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17Efereimu waphathana ndi mafano;
mulekeni!
18Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,
amapitiriza kuchita zachiwerewere;
atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu
ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Pleito contra Israel
1Escuchad, israelitas,
la palabra del Señor,
porque el Señor va a entrar en juicio
contra los habitantes del país:
«Ya no hay entre mi pueblo fidelidad ni amor,
ni conocimiento de Dios.
2Cunden, más bien, el perjurio y la mentira.
Abundan el robo, el adulterio y el asesinato.
¡Un homicidio sigue a otro!
3Por tanto, se resecará la tierra,
y desfallecerán todos sus habitantes.
¡Morirán las bestias del campo,
las aves del cielo y los peces del mar!
4»¡Que nadie acuse ni reprenda a nadie!
¡Tu pueblo parece acusar al sacerdote!
5Tropiezas de día y de noche,
y los profetas tropiezan contigo;
tu madre dejará de existir,
6pues por falta de conocimiento
mi pueblo ha sido destruido.
»Puesto que rechazaste el conocimiento,
yo también te rechazo como mi sacerdote.
Ya que te olvidaste de la ley de tu Dios,
yo también me olvidaré de tus hijos.
7Mientras más aumentaban los sacerdotes,
más pecaban contra mí;
cambiaron a quien es su gloria
en algo deshonroso.
8El pecado de mi pueblo es su comida;
se regodean en su perversidad.
9¡De tal pueblo, tal sacerdote!4:9 ¡De tal … sacerdote! Alt. Al pueblo le irá como al sacerdote.
¡Por eso les pediré cuentas de su conducta
y les daré la paga de sus acciones!
10»Comerán, pero no quedarán satisfechos;
se prostituirán, pero no se saciarán;4:10 no se saciarán. Alt. no tendrán hijos.
porque han abandonado al Señor
para entregarse 11a la prostitución y al vino,
¡al mosto que hace perder la razón!
12Mi pueblo consulta a su ídolo de madera,
y ese pedazo de palo le responde;
su tendencia a prostituirse los descarría;
se prostituyen en abierto desafío a su Dios.
13En la cumbre de montes y colinas
queman ofrendas y ofrecen sacrificios,
bajo la agradable sombra
de robles, álamos y encinas.
Por eso se prostituyen sus hijas
y cometen adulterio sus nueras.
14Pero no las castigaré
por sus prostituciones y adulterios,
porque sus propios maridos
se juntan con prostitutas
y celebran banquetes paganos
con las sacerdotisas del templo.
¡Es así como acaba por hundirse
un pueblo falto de entendimiento!
15»Si tú, Israel, te prostituyes,
¡que no resulte culpable Judá!
»No vayáis a Guilgal ni subáis a Bet Avén,4:15 Bet Avén, nombre que significa casa de iniquidad, se aplica aquí a la ciudad de Betel, que significa casa de Dios (véase también 5:8).
ni juréis: “¡Por la vida del Señor!”
16Israel es tan indómito como una novilla.
¿Cómo podrá el Señor pastorearlos
en campo abierto, como a corderos?
17Efraín se ha aliado con las imágenes;
¡pues que se quede con ellas!
18Cuando ya no tienen licor,
se entregan de lleno a la prostitución,
¡y hasta sus gobernantes aman la deshonra!
19¡Por eso un torbellino los arrastrará,
y quedarán avergonzados por sus sacrificios!