Yehova Ayimba Mlandu Israeli
1Inu Aisraeli, imvani mawu a Yehova,
chifukwa Yehova ali ndi mlandu ndi inu
amene mumakhala mʼdzikoli:
“Mʼdziko mwanu mulibe kukhulupirika, mulibe chikondi
mulibe kulabadira za Mulungu.
2Muli kutemberera kokha, kunama ndi kupha.
Kuba ndi kuchita chigololo;
machimo achita kunyanya
ndipo akungokhalira kuphana.
3Chifukwa chake dziko likulira
ndipo onse amene amakhalamo akuvutika;
zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga
ndiponso nsomba zamʼnyanja zikufa.
4“Koma wina asapeze mnzake chifukwa,
wina aliyense asayimbe mlandu mnzake,
pakuti anthu ako ali ngati anthu
amene amayimba mlandu wansembe.
5Mumapunthwa usana ndi usiku
ndipo aneneri amapunthwa nanu pamodzi.
Choncho ndidzawononga amayi anu.
6Anthu anga akuwonongeka chifukwa chosadziwa.
“Pakuti mwakana kudziwa,
Inenso ndidzakukanani monga ansembe anga;
chifukwa mwayiwala lamulo la Mulungu wanu,
Inenso ndidzayiwala ana anu.
7Ansembe ankati akachuluka
iwo ankandichimwiranso kwambiri;
iwo anasinthanitsa ulemerero wawo ndi chinthu china chonyansa.
8Amalemererapo pa machimo a anthu anga
ndipo amafunitsitsa kuti anthuwo azipitiriza kuchimwa.
9Ndipo zidzakhala motere: zochitikira anthu ena, zidzachitikiranso ansembe.
Ndidzawalanga onsewo chifukwa cha njira zawo,
ndidzawabwezera chifukwa cha machitidwe awo.
10“Iwo azidzadya koma sadzakhuta;
azidzachita zachiwerewere koma sadzachulukana,
chifukwa anasiya Yehova
kuti adzipereke 11ku zachiwerewere,
ku vinyo wakale ndi watsopano,
zimene zimachotsa nzeru zomvetsa zinthu
12za anthu anga.
Anthu anga amapempha nzeru ku fano lamtengo
ndipo ndodo yawo yamtengo imawayankha.
Mzimu wachiwerewere umawasocheretsa;
iwo sakukhulupirika kwa Mulungu wawo.
13Amapereka nsembe pamwamba pa mapiri
ndi kufukiza lubani pa zitunda,
pa tsinde pa mtengo wa thundu, mnjale ndi mkundi,
pamene pali mthunzi wabwino.
Nʼchifukwa chake ana anu aakazi akuchita zachiwerewere
ndipo akazi a ana anu akuchita zigololo.
14“Ine sindidzalanga ana anu aakazi
pamene iwo adzachita zachiwerewere,
kapena akazi a ana anu
pamene adzachita zigololo.
Paja inu nomwe amunanu mumayenda ndi akazi achiwerewere,
ndipo mumapereka nsembe pamodzi ndi akazi achiwerewere a ku malo opembedzerako.
Anthu amene alibe nzeru adzawonongeka ndithu!
15“Ngakhale umachita chigololo, iwe Israeli,
Yuda asapezeke ndi mlandu wotere.
“Usapite ku Giligala.
Usapite ku Beti-Aveni.
Ndipo usalumbire kuti, ‘Pali Yehova wamoyo!’
16Aisraeli ndi nkhutukumve,
ngosamva ngati ana angʼombe.
Kodi Yehova angathe kuwaweta bwanji
ngati ana ankhosa pa msipu wabwino?
17Efereimu waphathana ndi mafano;
mulekeni!
18Ngakhale pamene zakumwa zawo zatha,
amapitiriza kuchita zachiwerewere;
atsogoleri awo amakonda kwambiri njira zawo zochititsa manyazi.
19Adzachotsedwa ndi kamvuluvulu
ndipo adzachita manyazi chifukwa cha nsembe zawo.
Обвинение против Исроила
1Народ Исроила, слушайте слово Вечного,
потому что у Вечного тяжба с вами,
жители этой земли:
– В этой стране нет ни верности, ни любви,
ни познания Всевышнего.
2Есть лишь проклятие, ложь и убийство,
воровство и разврат.
Они переходят все границы,
кровопролитие следует за кровопролитием.
3Поэтому земля высыхает,
и все, кто живёт в ней, изнемогают.
Гибнут дикие звери, птицы небесные
и рыбы морские.
4Но пусть никто не судится,
пусть один не обвиняет другого;
Я вас обвиняю, священнослужители!4:4 Или: «ваш народ подобен тем, кто спорит со священнослужителями».
5Вы спотыкаетесь днём и ночью,
и пророки спотыкаются вместе с вами.
Итак, Я истреблю вашу мать4:5 То есть Исроил. –
6Мой народ будет истреблён из-за недостатка знания.
Как вы отвергли знание,
так и Я отвергну вас, Мои священнослужители.
Как вы забыли Закон вашего Бога,
так и Я забуду ваших детей.
7Чем больше становилось священнослужителей,
тем больше они грешили против Меня.
Я поменяю их славу4:7 Или: «Они сменили свою славу»; или: «Они сменили свою Славу (Вечного)». на нечто постыдное.
8Они питаются жертвами за грехи Моего народа,
потому и желают их беззаконий4:8 См. Лев. 6:26..
9Что будет с народом, то и со священнослужителями.
Я накажу их за грехи их
и воздам им по делам их.
10Они будут есть, но не насытятся,
будут блудить, но останутся бездетными,
потому что они оставили Вечного
и предали себя 11разврату,
вину старому и вину молодому,
которые отнимают понимание 12у Моего народа.
Они просят совета у деревяшки,
и палка даёт им ответ.
Они сбились с пути, следуя за ложными богами,
и, развратившись, отдалились от своего Бога.
13Они приносят жертвы на вершинах гор
и сжигают приношения на холмах,
под дубом, тополем и теревинфом4:13 Теревинф – невысокое дерево (до пяти метров) с широкой кроной. Распространено в тёплых сухих местах в самом Исроиле и в соседних районах.,
потому что их тень приятна.
Поэтому ваши дочери блудят,
а ваши невестки нарушают супружескую верность.
14Я не накажу ваших дочерей,
когда они будут блудить,
и не накажу ваших невесток,
когда они будут нарушать супружескую верность,
потому что мужчины сами уединяются с блудницами
и приносят жертвы с блудницами храмовыми4:14 Храмовые блудницы – имеются в виду «жрицы любви», которые были неотъемлемой частью весьма распространённых в те дни языческих культов плодородия..
Невежественный народ погибнет!
15Хотя ты и блудишь, Исроил,
пусть хоть Иудея не грешит.
Не ходите в Гилгал,
не поднимайтесь в Бет-Авен («дом зла»)4:15 Бет-Авен («дом зла») – прозвище, данное Вефилю, чьё название значит «дом Всевышнего». См. также 5:8 и 10:5..
Не клянитесь там: «Верно, как и то, что жив Вечный!»
16Исроильтяне упираются,
как упрямая телица.
Как же тогда Вечный сможет пасти их,
словно овец на просторном пастбище?
17Ефраим4:17 Ефраим – так часто называли Северное царство, Исроил, где наиболее влиятельным был род Ефраима. привязался к идолам –
оставь его!
18Даже когда у них кончается вино,
они продолжают блудить.
Их правители любят постыдные пути.
19Сильный ветер сметёт их,
и им будет стыдно за свои жертвы.