Hoseya 2 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 2:1-23

1“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’ ”

Kulangidwa ndi Kubwezeretsedwa kwa Israeli

2“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo,

pakuti si mkazi wanga,

ndipo ine sindine mwamuna wake.

Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake,

ndi kusakhulupirika pa mawere ake.

3Akapanda kutero ndidzamuvula,

ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa;

ndidzamuwumitsa ngati chipululu,

adzakhala ngati dziko lopanda madzi,

ndi kumupha ndi ludzu.

4Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake,

chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.

5Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere

ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi.

Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga,

zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi,

ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’

6Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga;

ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.

7Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza;

adzazifunafuna koma sadzazipeza.

Pamenepo iye adzati,

‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja,

pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’

8Iye sanazindikire kuti ndine amene

ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta.

Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide,

zimene ankapangira mafano a Baala.

9“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola,

ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa.

Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa,

zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.

10Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake

pamaso pa zibwenzi zake;

palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.

11Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse:

zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano,

za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.

12Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu,

imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake.

Ndidzayisandutsa chithukuluzi,

ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.

13Ndidzamulanga chifukwa cha masiku

amene anafukiza lubani kwa Abaala;

anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali

ndipo anathamangira zibwenzi zake,

koma Ine anandiyiwala,”

akutero Yehova.

14“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;

ndidzapita naye ku chipululu

ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.

15Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,

ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.

Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,

monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16“Tsiku limeneli,” Yehova akuti,

“udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’

sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’

17Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;

sadzatchulanso mayina awo popemphera.

18Tsiku limenelo ndidzachita pangano

ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga

ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.

Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,

lupanga ndi zida zonse zankhondo,

kuti onse apumule mwamtendere.

19Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;

ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,

mwachikondi ndi mwachifundo.

20Ndidzakutomera mokhulupirika

ndipo udzadziwa Yehova.

21“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”

akutero Yehova.

“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo

ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;

22ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,

vinyo ndi mafuta,

ndipo zidzamvera Yezireeli.

23Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:

ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’

Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’

ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

Luganda Contemporary Bible

Koseya 2:1-23

12:1 nny 23“Mwogere ku baganda bammwe nti, ‘bantu bange,’ mwogere ne ku bannyinammwe nti, ‘baagalwa bange.’ ”

Okubonerezebwa kwa Isirayiri, n’Okuzzibwa Obuggya kwabwe

22:2 a nny 5; Is 50:1; Kos 1:2 b Ez 23:45Munenye nnyammwe,

mumunenye,

kubanga si mukazi wange, so nange siri bba.

Aggyewo obukaba obuli mu maaso ge,

n’obwenzi obuva wakati w’amabeere ge;

32:3 a Ez 16:4, 22 b Is 32:13-14nneme okumwambulira ddala

ne mmulekeraawo nga bwe yali ku lunaku kwe yazaalibwa;

ne mmufuula ng’eddungu,

ne mmulekawo ng’ensi enkalu eteriiko ky’egasa,

ne mmussa ennyonta.

42:4 Ez 8:18Sirilaga kwagala kwange eri abaana be,

kubanga baana ba bwenzi.

52:5 a Yer 3:6 b Yer 44:17-18Nnyabwe yakola obwenzi,

n’abazaalira mu buwemu.

Yayogera nti, “Ndigenda eri baganzi bange abampa emmere n’amazzi,

n’ebimbugumya n’ebyokwambala,

n’amafuta n’ekyokunywa.”

62:6 Yob 3:23; 19:8; Kgb 3:9Kyendiva nziba ekkubo lye n’amaggwa,

ne mmuzimbako bbugwe okumwetooloola, aleme okulaba ekkubo wayitira.

72:7 a Kos 5:13 b Yer 2:2; 3:1 c Ez 16:8Aligezaako okugoberera baganzi be abakwate,

naye talibatuukako, alibanoonya naye talibalaba.

Oluvannyuma alyogera nti, “Naagenda eri bba wange eyasooka,

kubanga mu biro ebyo nabanga bulungi

okusinga bwe ndi kaakano.”

82:8 a Is 1:3 b Ez 16:15-19; Kos 8:4Tajjukira nga nze namuwanga eŋŋaano,

ne wayini n’amafuta,

era eyamuwa effeeza ne zaabu

bye baakozesanga okuweerezanga Baali.

92:9 a Kos 8:7 b Kos 9:2“Kyendiva neddiza emmere yange ey’empeke ng’eyengedde,

ne wayini wange ng’atuuse;

era nzija kumuggyako ebyambalo byange eby’ebbugumu n’ebyambalo byange ebya bulijjo,

bye yayambalanga.

102:10 Ez 16:37Era kyenaava nyanika obukaba bwe

mu maaso ga baganzi be,

so tewaliba amuwonya mu mukono gwange.

112:11 a Yer 7:34 b Is 1:14; Yer 16:9; Kos 3:4; Am 8:10Ndikomya ebinyumu bye byonna, n’embaga ze eza buli mwaka,

n’embaga ze ez’emyezi egyakaboneka, ne ssabbiiti ze,

n’enkuŋŋaana ze zonna entukuvu.

122:12 a Is 7:23; Yer 8:13 b Is 5:6 c Kos 13:8Ndizikiriza emizabbibu gye n’emitiini gye,

gye yayogerako nti, ‘Guno gwe musaala baganzi bange gwe bansasula.’

Ndibizisa,

era n’ensolo ez’omu nsiko ziribyonoona.

132:13 a Kos 11:2 b Ez 16:17 c Kos 4:13 d Kos 4:6; 8:14; 13:6Ndimubonereza olw’ennaku

ze yayotereza obubaane eri Babaali,

ne yeeyambaza empeta n’ebintu eby’omuwendo ennyo,

n’agenda eri baganzi be,

naye nze n’aneerabira,”

bw’ayogera Mukama.

14Kale kyendiva musendasenda,

ne mmutwala mu ddungu,

ne njogera naye n’eggonjebwa.

152:15 a Yos 7:24, 26 b Kuv 15:1-18 c Yer 2:2 d Kos 12:9Era eyo ndimuddiza ennimiro ze ez’emizabbibu,

ne nfuula Ekiwonvu kya Akoli2:15 Akoli kitegeeza emitawaana oluggi olw’essuubi.

Alimpuliriza nga bwe yampulirizanga mu nnaku ez’obuvubuka bwe,

era nga mu biro bye yaviira mu nsi ya Misiri.

16“Ku lunaku olwo,” bw’ayogera Mukama,

“olimpita nti, ‘mwami wange;’

toliddayo nate kumpita, ‘Mukama wange.’ ”

172:17 a Kuv 23:13; Zab 16:4 b Yos 23:7Ndiggya amannya ga Babaali mu kamwa ke,

so taliddayo nate okwasanguza amannya gaabwe.

182:18 a Yob 5:22 b Is 2:4 c Yer 23:6; Ez 34:25Ku lunaku olwo ndibakolera endagaano

n’ensolo ez’omu nsiko n’ennyonyi ez’omu bbanga,

n’ebyewalula ku ttaka,

era ndiggyawo obusaale, n’ekitala, n’entalo mu nsi,

bonna ne batuula mirembe.

192:19 a Is 62:4 b Is 1:27Era ndikwogereza ennaku zonna,

ndikwogereza mu butuukirivu, ne mu mazima,

ne mu kwagala ne mu kusaasira.

202:20 Yer 31:34; Kos 6:6; 13:4Ndikwogereza mu bwesigwa,

era olimanya Mukama.

212:21 Is 55:10; Zek 8:12“Ku lunaku olwo,

ndyanukula eggulu,

nalyo ne lyanukula ensi;

222:22 Yer 31:12; Yo 2:19ensi erimeramu emmere ey’empeke,

ne wayini n’amafuta,

nabyo ne bifunibwa Yezuleeri,2:22 Yezuleeri kitegeeza Katonda asimba

bw’ayogera Mukama.

232:23 a Yer 31:27 b Kos 1:6 c Kos 1:10 d Bar 9:25*; 1Pe 2:10“Ndimwesimbira mu nsi,

ndisaasira oyo eyayitibwanga nti, atasaasirwa,

era ndigamba abataali bantu bange nti, ‘Bantu bange,’

era nabo balyogera nti, ‘Ggwe Katonda wange.’ ”