Hoseya 2 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 2:1-23

1“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’ ”

Kulangidwa ndi Kubwezeretsedwa kwa Israeli

2“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo,

pakuti si mkazi wanga,

ndipo ine sindine mwamuna wake.

Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake,

ndi kusakhulupirika pa mawere ake.

3Akapanda kutero ndidzamuvula,

ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa;

ndidzamuwumitsa ngati chipululu,

adzakhala ngati dziko lopanda madzi,

ndi kumupha ndi ludzu.

4Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake,

chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.

5Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere

ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi.

Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga,

zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi,

ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’

6Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga;

ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.

7Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza;

adzazifunafuna koma sadzazipeza.

Pamenepo iye adzati,

‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja,

pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’

8Iye sanazindikire kuti ndine amene

ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta.

Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide,

zimene ankapangira mafano a Baala.

9“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola,

ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa.

Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa,

zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.

10Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake

pamaso pa zibwenzi zake;

palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.

11Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse:

zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano,

za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.

12Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu,

imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake.

Ndidzayisandutsa chithukuluzi,

ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.

13Ndidzamulanga chifukwa cha masiku

amene anafukiza lubani kwa Abaala;

anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali

ndipo anathamangira zibwenzi zake,

koma Ine anandiyiwala,”

akutero Yehova.

14“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo;

ndidzapita naye ku chipululu

ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.

15Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa,

ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo.

Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake,

monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.

16“Tsiku limeneli,” Yehova akuti,

“udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’

sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’

17Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake;

sadzatchulanso mayina awo popemphera.

18Tsiku limenelo ndidzachita pangano

ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga

ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga.

Ndidzachotsa mʼdzikomo uta,

lupanga ndi zida zonse zankhondo,

kuti onse apumule mwamtendere.

19Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya;

ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro,

mwachikondi ndi mwachifundo.

20Ndidzakutomera mokhulupirika

ndipo udzadziwa Yehova.

21“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,”

akutero Yehova.

“Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo

ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;

22ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu,

vinyo ndi mafuta,

ndipo zidzamvera Yezireeli.

23Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga:

ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’

Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’

ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’ ”

Korean Living Bible

호세아 2:1-23

이스라엘의 형벌과 회복

1“너희 형제에게는 2:1 히 ‘암미’‘내 백성’ 이라 하고 너희 자매에게는 2:1 히 ‘루하마’‘나의 사랑하는 자’ 라 고 하라.”

2“내 자녀들아, 너희는 너희 어머니를 책망하고 책망하라. 너희 어머니는 내 아내가 아니며 나는 그녀의 남편이 아니다. 그녀가 자기 얼굴에서 음란한 모습을 지워 버리게 하고 그 유방 사이에서 음란을 제거하게 하라.

3그렇지 않으면 내가 그녀를 벌거벗겨 저가 태어나던 날과 같게 할 것이며 저를 광야같이 되게 하고 마른 땅같이 되게 하여 목말라 죽게 할 것이다.

4내가 그 자녀들에게 사랑을 베풀지 않을 것이다. 그들은 음란한 자식들이기 때문이다.

5그들의 어머니가 창녀짓을 하였고 그들을 배었던 여자가 부끄러운 일을 하였다. 그녀는 ‘내가 사랑하는 자들을 쫓아가겠다. 그들은 나에게 빵과 물과 양털과 모시와 기름과 술을 준다’ 라고 말하였다.

6그러므로 내가 가시덤불로 그 길을 막고 담을 쌓아 저가 그 길을 찾지 못하게 하겠다.

7그녀가 사랑하는 자들을 쫓아갈지라도 따라 잡지 못할 것이며 그들을 찾아도 만나지 못할 것이다. 그제서야 그녀는 ‘내가 본남편에게 돌아가겠다. 내 형편이 그 때가 지금보다 더 나았다’ 하고 말할 것이다.

8저에게 곡식과 새 포도주와 기름도 내가 주고 저가 바알 숭배를 위해 사용한 은과 금도 내가 주었는데 저는 이것을 알지 못하고 있다.

9“그러므로 2:9 또는 ‘그시절에’추수 때에 내가 내 곡식을 찾아가고 그 시기에 나의 새 포도주를 도로 찾으며 저의 벌거벗은 몸을 가리도록 준 내 양털과 모시를 뺏을 것이다.

10이제 내가 그녀의 연인들이 보는 데서 저의 수치를 드러내겠다. 저를 내 손에서 건져낼 자가 없을 것이다.

11내가 저의 모든 즐거움과 연례 축제와 매월 있는 2:11 또는 ‘월삭과’초하룻날 행사와 안식일과 모든 명절을 폐지할 것이며

12저가 그 연인들에게 화대로 받았다고 하는 포도나무와 무화과나무를 내가 못 쓰도록 하여 잡목 숲이 되게 하고 들짐승이 그것을 먹게 하겠다.

13저가 귀고리와 패물로 단장하고 연인들을 따라가서 나를 잊어버리고 바알에게 분향한 그 날수만큼 내가 그녀를 벌할 것이다. 이것은 나 주 여호와의 말이다.

14“그러므로 내가 그녀를 꾀어내어 광야로 데리고 가서 부드러운 말로 잘 타이르고

15거기서 그녀에게 포도원을 되돌려 주고 2:15 히 ‘아골골짜기’고난의 골짜기를 희망의 문이 되게 하겠다. 저가 어렸을 때와 같이, 이집트에서 나오던 날과 같이 거기서 노래할 것이다.

16“나 여호와가 말한다. 그 날에 저가 나를 ‘내 남편’ 이라 부르고 다시는 2:16 히 ‘내바알’‘내 주’ 라 부르지 않을 것이다.

17내가 그 입에서 바알들의 이름을 제하여 저가 다시는 그 이름을 부르지 않게 하겠다.

18그 날에 내가 모든 들짐승과 공중의 새들과 땅에 기어다니는 것들과 계약을 맺어 내 백성을 해치지 못하게 할 것이며 또 이 땅에서 활과 칼을 꺾어 전쟁을 없애고 그들이 평안히 살게 할 것이다.

19이스라엘아, 내가 너를 영원히 내 아내로 삼아 너에게 신의와 사랑과 자비를 베풀고

20진실함으로 너를 맞을 것이니 네가 나를 여호와로 인정할 것이다.

21“나 여호와가 말한다. 그 날에 내가 응답하겠다. 나는 하늘에 응답하고 하늘은 땅에 응답하고

22땅은 곡식과 포도주와 기름에 응답하고 또 이것들은 2:22 ‘하나님이씨를뿌리신다’ 는뜻.이스르엘에 응답할 것이다.

23내가 나를 위하여 그를 이 땅에 심고 ‘사랑받지 못하는 자’ 라고 불리던 자에게 내가 사랑을 베풀고 내 백성이 아니라고 하던 자에게 ‘너는 내 백성이다’ 하고 말할 것이며 그들이 ‘주는 나의 하나님이십니다’ 하고 말할 것이다.”