Hoseya 14 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 14:1-9

Kulapa Kubweretsa Madalitso

1Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.

Machimo anu ndi amene akugwetsani!

2Bweretsani zopempha zanu

ndipo bwererani kwa Yehova.

Munene kwa Iye kuti,

“Tikhululukireni machimo athu onse

ndi kutilandira mokoma mtima,

kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.

3Asiriya sangatipulumutse;

ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,

sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’

kwa zimene manja athu omwe anazipanga,

pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”

4Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo

ndipo ndidzawakonda mwaufulu

pakuti ndaleka kuwakwiyira.

5Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli

Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.

Adzazika mizu yake pansi

ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

6mphukira zake zidzakula.

Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,

kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.

7Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.

Iye adzakula bwino ngati tirigu.

Adzachita maluwa ngati mphesa

ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.

8Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?

Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.

Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;

zipatso zako zimachokera kwa Ine.”

9Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.

Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.

Njira za Yehova ndi zolungama;

anthu olungama amayenda mʼmenemo,

koma anthu owukira amapunthwamo.

La Bible du Semeur

Osée 14:1-10

1Samarie paiera pour ses fautes

parce qu’elle s’est révoltée ╵contre son Dieu,

ses habitants mourront ╵sous les coups de l’épée,

ses bébés seront écrasés,

et l’on fendra le ventre ╵de ses femmes enceintes. »

Appel et promesse

2Reviens donc, Israël, ╵à l’Eternel, ton Dieu,

car ce sont tes péchés ╵qui ont causé ta chute.

3Préparez vos paroles

et revenez à l’Eternel,

et dites-lui : ╵« Pardonne toute faute,

et prends en bonne part ╵que nous t’offrions en retour, ╵en sacrifice, l’hommage de nos lèvres, ╵en guise de taureaux.

4Ce n’est pas l’Assyrie, ╵qui pourra nous sauver,

nous ne monterons pas ╵sur des chevaux de guerre

et nous ne dirons plus ╵à l’œuvre de nos mains : ╵“Toi, tu es notre Dieu”,

car c’est toi qui as compassion ╵de l’orphelin. »

5« Moi, je les guérirai ╵de leur apostasie,

je leur témoignerai ╵librement mon amour

parce que ma colère ╵se détournera d’eux.

6Oui, je serai pour Israël ╵semblable à la rosée,

il fleurira comme le lis,

et s’enracinera ╵comme les cèdres du Liban.

7Ses rameaux s’étendront au loin

et il aura la majesté ╵de l’olivier,

et son parfum sera semblable ╵à celui du Liban.

8Ils reviendront

habiter à son ombre,

ils revivront comme le blé

et fleuriront comme la vigne,

et ils auront la renommée ╵des grands vins du Liban.

9O Ephraïm… ╵qu’as-tu à faire14.9 qu’as-tu à faire: d’après l’ancienne version grecque. Le texte hébreu traditionnel a : qu’ai-je à faire. ╵encore des idoles ?

Moi, je l’exaucerai, ╵je veillerai14.9 Le verbe exaucer fait assonance, en hébreu, avec le nom de la déesse Anat, et le verbe veiller avec celui de la déesse Ashéra. sur lui.

Je suis comme un cyprès ╵qui reste toujours vert,

tu porteras du fruit ╵et c’est moi qui l’aurai produit. »

10Qui donc est assez sage

pour comprendre ces choses,

assez intelligent ╵pour les connaître ?

Les voies que l’Eternel prescrit sont droites,

les justes les suivront,

tandis que les rebelles ╵trébucheront sur elles.