Hoseya 13 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 13:1-16

Mkwiyo wa Yehova pa Israeli

1Kale Efereimu ankati akayankhula, anthu ankanjenjemera;

anali wolemekezeka mu Israeli.

Koma analakwa popembedza Baala, motero anafa.

2Tsopano akunka nachimwirachimwirabe;

akudzipangira mafano pogwiritsa ntchito siliva wawo,

zifanizo zopangidwa mwaluso,

zonsezo zopangidwa ndi amisiri.

Amanena za anthu awa kuti,

“Amatenga munthu ndi kumupereka nsembe

ndipo amapsompsona fano la mwana wangʼombe.”

3Choncho adzakhala ngati nkhungu yammawa,

ngati mame amene amakamuka msanga,

ngati mungu wowuluka kuchokera pa malo opunthira tirigu,

ngati utsi umene ukutulukira pa zenera.

4Koma Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mu Igupto.

Simuyenera kudziwa Mulungu wina, koma Ine ndekha,

palibe Mpulumutsi wina kupatula Ine.

5Ndinakusamalira mʼchipululu,

mʼdziko lotentha kwambiri.

6Pamene ndinawadyetsa, iwo anakhuta;

iwo atakhuta anayamba kunyada;

ndipo anandiyiwala Ine.

7Motero ndidzawalumphira ngati mkango,

ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku.

8Ngati chimbalangondo cholandidwa ana ake,

ndidzawambwandira ndi kuwathyolathyola.

Ndidzawapwepweta ngati mkango;

chirombo chakuthengo chidzawakhadzula.

9“Iwe Israeli, wawonongedwa,

chifukwa ukutsutsana ndi Ine, ukutsutsana ndi mthandizi wako.

10Kodi mfumu yako ili kuti, kuti ikupulumutse?

Olamulira ako a mʼmizinda yonse ali kuti,

amene iwe unanena za iwo kuti,

‘Patseni mfumu ndi akalonga?’

11Choncho Ine ndinakupatsani mfumu mwachipseramtima,

ndipo ndinayichotsa mwaukali.

12Kulakwa kwa Efereimu kwasungidwa,

machimo ake alembedwa mʼbuku.

13Zowawa zonga za mayi pa nthawi yobala mwana zamugwera,

koma iye ndi mwana wopanda nzeru,

pamene nthawi yake yobadwa yafika

iyeyo safuna kutuluka mʼmimba mwa amayi ake.

14“Ndidzawapulumutsa ku mphamvu ya manda;

ndidzawawombola ku imfa.

Kodi iwe imfa, miliri yako ili kuti?

Kodi iwe manda, kuwononga kwako kuli kuti?

“Sindidzachitanso chifundo,

15ngakhale Efereimu akondwe pakati pa abale ake,

mphepo ya kummawa yochokera kwa Yehova idzabwera,

ikuwomba kuchokera ku chipululu.

Kasupe wake adzaphwa

ndipo chitsime chake chidzawuma.

Chuma chake chonse chamtengowapatali

chidzafunkhidwa ndipo chidzatengedwa.

16Anthu a ku Samariya adzalangidwa chifukwa cha zolakwa zawo,

chifukwa anawukira Mulungu wawo.

Adzaphedwa ndi lupanga;

ana awo adzaphedwa mowamenyetsa pansi,

akazi awo oyembekezera adzatumbulidwa pa mimba.”

Hoffnung für Alle

Hosea 13:1-15

Gottes Gericht ist nicht mehr aufzuhalten

1Der Herr sagt: »Es gab eine Zeit, da waren die Bewohner von Ephraim mächtig und stark. Wenn sie redeten, packte alle die Angst. Doch dann ließen sie sich mit dem Götzen Baal ein und gingen zugrunde. 2Trotzdem haben sie noch nicht genug, sondern treiben es nur noch schlimmer: Aus Silber gießen sie Götterfiguren, wie es ihnen gefällt. Sie sagen: ›Wer Gott opfern will, muss die Stierfiguren küssen!‹13,2 Oder: Von ihnen sagt man: ›Sie opfern Menschen und küssen Stierfiguren!‹ Ihre Götter sind Menschenwerk, von Handwerkern hergestellt. 3Darum werden sie so schnell verschwinden wie eine Wolke am Morgen, wie der Tau unter der Sonne, wie Spreu, die der Wind vom Dreschplatz weht, und wie Rauch, der aus der Dachluke aufsteigt.

4Ich bin der Herr, euer Gott, ich habe euch aus Ägypten befreit. Mich allein habt ihr als euren Gott kennen gelernt, es gibt keinen anderen Retter! 5In der glühenden Hitze der Wüste habe ich euch begleitet und bewahrt. 6Ich habe euch gutes Land gegeben, und ihr seid stets satt geworden. Doch je besser es euch ging, desto überheblicher wurdet ihr. Mich, den Herrn, habt ihr vergessen! 7Darum falle ich euch an wie ein Löwe. Wie ein Leopard liege ich am Weg auf der Lauer. 8Ich greife euch an wie eine Bärin, der man die Jungen geraubt hat. Ich reiße euch in Stücke, ja, ich verschlinge euch wie eine Löwin! Was übrig bleibt, werden die wilden Tiere zerfleischen.

9Ihr Leute von Israel, ihr stellt euch gegen mich, obwohl ich allein euch helfen kann. Weil ihr dies tut, geht ihr zugrunde! 10Wo ist nun euer König, der euch schützt und eure Städte vor dem Untergang bewahrt? Wo sind die führenden Männer eures Volkes? Ihr wolltet doch einen König haben und Männer, die euch regieren! 11Voller Zorn habe ich euch einen König gegeben, und voller Zorn habe ich ihn wieder weggenommen. 12Ephraim hat gegen mich gesündigt. Die Erinnerung daran bewahre ich sorgfältig auf! 13Israel ist wie ein Kind im Mutterleib, das sich vor der Geburt so dreht, dass es nicht zur Welt kommen kann.

14Soll ich sie vor dem Tod retten? Soll ich sie aus der Gewalt des Totenreichs erlösen? Nein! Der Tod soll sie dahinraffen, das Totenreich sie gefangen nehmen!13,14 Wörtlich: Wo ist deine Pest, Tod? Wo sind deine Seuchen, Totenreich? – Nach einer anderen Deutung sind diese Worte als Ankündigung von Israels Rettung und Gottes Sieg über den Tod zu verstehen. Ich werde kein Mitleid mehr mit ihnen haben. 15Noch ist Ephraim wie ein fruchtbarer Garten unter seinen Bruderstämmen, doch der Feind wird kommen und ihn vernichten. Wie ein starker Ostwind, der aus der glühend heißen Wüste weht, die Brunnen austrocknet und die Quellen versiegen lässt, so wird der Feind über Ephraim herfallen. Er plündert die Schätze und raubt die kostbarsten Gegenstände. Dafür sorge ich, der Herr!