Hoseya 12 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 12:1-14

1Efereimu amadya mpweya;

tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa

ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.

Amachita mgwirizano ndi Asiriya

ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.

2Yehova akuyimba mlandu Yuda;

Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,

adzamulanga molingana ndi ntchito zake.

3Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;

iye atakula analimbana ndi Mulungu.

4Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;

analira napempha kuti amukomere mtima.

Mulungu anakumana naye ku Beteli

ndipo anayankhula naye kumeneko,

5Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

Yehova ndiye dzina lake lotchuka!

6Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;

pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,

ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

7Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;

iyeyo amakonda kubera anthu.

8Efereimu amadzitama ponena kuti,

“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.

Palibe amene angandiloze chala

chifukwa cha kulemera kwanga.”

9“Ine ndine Yehova Mulungu wako

amene ndinakutulutsa mu Igupto.

Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,

monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.

10Ndinayankhula ndi aneneri,

ndinawaonetsa masomphenya ambiri,

ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11Kodi Giliyadi ndi woyipa?

Anthu ake ndi achabechabe!

Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?

Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala

mʼmunda molimidwa.

12Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,

Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,

ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.

13Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;

kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.

14Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.

Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.

Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

New International Version – UK

Hosea 12:1-14

In Hebrew texts 12:1-14 is numbered 12:2-15. 1Ephraim feeds on the wind;

he pursues the east wind all day

and multiplies lies and violence.

He makes a treaty with Assyria

and sends olive oil to Egypt.

2The Lord has a charge to bring against Judah;

he will punish Jacob12:2 Jacob means he grasps the heel, a Hebrew idiom for he takes advantage of or he deceives. according to his ways

and repay him according to his deeds.

3In the womb he grasped his brother’s heel;

as a man he struggled with God.

4He struggled with the angel and overcame him;

he wept and begged for his favour.

He found him at Bethel

and talked with him there –

5the Lord God Almighty,

the Lord is his name!

6But you must return to your God;

maintain love and justice,

and wait for your God always.

7The merchant uses dishonest scales

and loves to defraud.

8Ephraim boasts,

‘I am very rich; I have become wealthy.

With all my wealth they will not find in me

any iniquity or sin.’

9‘I have been the Lord your God

ever since you came out of Egypt;

I will make you live in tents again,

as in the days of your appointed festivals.

10I spoke to the prophets,

gave them many visions

and told parables through them.’

11Is Gilead wicked?

Its people are worthless!

Do they sacrifice bulls in Gilgal?

Their altars will be like piles of stones

on a ploughed field.

12Jacob fled to the country of Aram12:12 That is, North-west Mesopotamia;

Israel served to get a wife,

and to pay for her he tended sheep.

13The Lord used a prophet to bring Israel up from Egypt,

by a prophet he cared for him.

14But Ephraim has aroused his bitter anger;

his Lord will leave on him the guilt of his bloodshed

and will repay him for his contempt.