Hoseya 12 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 12:1-14

1Efereimu amadya mpweya;

tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa

ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.

Amachita mgwirizano ndi Asiriya

ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.

2Yehova akuyimba mlandu Yuda;

Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,

adzamulanga molingana ndi ntchito zake.

3Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;

iye atakula analimbana ndi Mulungu.

4Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;

analira napempha kuti amukomere mtima.

Mulungu anakumana naye ku Beteli

ndipo anayankhula naye kumeneko,

5Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

Yehova ndiye dzina lake lotchuka!

6Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;

pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,

ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

7Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;

iyeyo amakonda kubera anthu.

8Efereimu amadzitama ponena kuti,

“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.

Palibe amene angandiloze chala

chifukwa cha kulemera kwanga.”

9“Ine ndine Yehova Mulungu wako

amene ndinakutulutsa mu Igupto.

Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,

monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.

10Ndinayankhula ndi aneneri,

ndinawaonetsa masomphenya ambiri,

ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11Kodi Giliyadi ndi woyipa?

Anthu ake ndi achabechabe!

Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?

Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala

mʼmunda molimidwa.

12Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,

Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,

ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.

13Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;

kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.

14Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.

Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.

Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.

New International Reader’s Version

Hosea 12:1-14

1The people of Ephraim look to others for help.

It’s like chasing the wind.

The wind they keep chasing

is hot and dry.

They tell more and more lies.

They are always hurting others.

They make a peace treaty with Assyria.

They send olive oil to Egypt to get help.

2The Lord is bringing charges against Judah.

He will punish Jacob’s people

because of how they act.

He’ll pay them back

for the evil things they’ve done.

3Even before Jacob was born,

he was holding on to his brother’s heel.

When he became a man,

he struggled with God.

4At Peniel he struggled with the angel and won.

Jacob wept and begged for his blessing.

God also met with him at Bethel.

He talked with him there.

5He is the Lord God who rules over all.

His name is the Lord.

6People of Jacob, you must return to your God.

You must hold on to love and do what is fair.

You must trust in your God always.

7You are like a trader who uses dishonest scales.

You love to cheat others.

8People of Ephraim, you brag,

“We are very rich.

We’ve become wealthy.

And no one can prove we sinned

to gain all this wealth.”

9The Lord says,

“I have been the Lord your God

ever since you came out of Egypt.

But I will make you live in tents again.

That is what you did when you celebrated

the Feast of Booths in the desert.

10I spoke to the prophets.

They saw many visions.

I gave you warnings through them.”

11The people of Gilead are evil!

They aren’t worth anything!

Gilgal’s people sacrifice bulls to other gods.

Their altars will become like piles of stones

on a plowed field.

12Jacob ran away to the country of Aram.

There Israel served Laban to get a wife.

He took care of sheep to pay for her.

13The prophet Moses brought Israel up from Egypt.

The Lord used him to take care of them.

14But Ephraim’s people have made the Lord very angry.

Their Lord will hold them accountable for the blood they’ve spilled.

He’ll pay them back for the shameful things they’ve done.