Hoseya 11 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 11:1-12

Chikondi cha Mulungu pa Israeli

1“Israeli ali mwana, ndinamukonda,

ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.

2Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana

iwo amandithawa kupita kutali.

Ankapereka nsembe kwa Abaala

ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.

3Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda,

ndipo ndinawagwira pa mkono;

koma iwo sanazindikire

kuti ndine amene ndinawachiritsa.

4Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu

ndi zomangira za chikondi;

ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo

ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.

5“Sadzabwerera ku Igupto,

koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo

pakuti akana kutembenuka.

6Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo,

ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo

nadzathetseratu malingaliro awo.

7Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine.

Ngakhale atayitana Wammwambamwamba,

sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.

8“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu?

Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli?

Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima?

Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu?

Mtima wanga wakana kutero;

chifundo changa chonse chikusefukira.

9Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa,

kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu.

Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu,

Woyerayo pakati panu.

Sindidzabwera mwaukali.

10Iwo adzatsatira Yehova;

Iye adzabangula ngati mkango.

Akadzabangula,

ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.

11Adzabwera akunjenjemera

ngati mbalame kuchokera ku Igupto,

ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya.

Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,”

akutero Yehova.

Tchimo la Israeli

12Efereimu wandizungulira ndi mabodza,

nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo.

Ndipo Yuda wawukira Mulungu,

wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Oseas 11:1-12

El amor de Dios por Israel

1«Desde que Israel era niño, yo lo amé;

de Egipto llamé a mi hijo.

2Pero cuanto más lo llamaba,

más se alejaba de mí.11:2 llamaba … de mí (LXX); llamaban … de ellos (TM).

Ofrecía sacrificios a los falsos dioses11:2 falsos dioses. Lit. baales.

y quemaba incienso a las imágenes.

3Yo fui quien enseñó a caminar a Efraín;

yo fui quien lo tomó de la mano.

Pero él no quiso reconocer

que era yo quien lo sanaba.

4Lo atraje con cuerdas de ternura,11:4 de ternura. Lit. humanas.

lo atraje con lazos de amor.

Le quité de la cerviz el yugo,

y con ternura me acerqué para alimentarlo.

5»No volverán a Egipto,

sino que Asiria reinará sobre ellos,

porque no quisieron volverse a mí.

6En sus ciudades se blandirán espadas,

que destrozarán los barrotes de sus puertas

y acabarán con sus planes.

7Mi pueblo está resuelto a renegar de mi nombre;

por eso, aunque me invoquen, no los exaltaré.

8»¿Cómo podría yo entregarte, Efraín?

¿Cómo podría abandonarte, Israel?

¡Yo no podría entregarte como entregué a Admá!

¡Yo no podría abandonarte como a Zeboyín!

Dentro de mí, el corazón me da vuelcos,

y se me conmueven las entrañas.

9Pero no daré rienda suelta a mi ira,

ni volveré a destruir a Efraín.

Porque en medio de ti no está un hombre,

sino que estoy yo, el Dios santo,

y no atacaré la ciudad».

10El Señor rugirá como león,

y ellos lo seguirán.

Cuando el Señor lance su rugido,

sus hijos vendrán temblando de occidente.

11«Vendrán desde Egipto, temblando como aves;

vendrán desde Asiria, temblando como palomas,

y yo los estableceré en sus casas

—afirma el Señor—.

El pecado de Israel

12»Efraín me ha rodeado con mentiras,

y el reino de Israel, con engaños;

Judá anda errante, lejos de Dios;

¡lejos del Dios santísimo y fiel!