Hoseya 10 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 10:1-15

1Israeli anali mpesa wotambalala;

anabereka zipatso zambiri.

Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,

anawonjezera kumanga maguwa ansembe.

Pamene dziko lake linkatukuka,

anakongoletsa miyala yake yopatulika.

2Mtima wawo ndi wonyenga

ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.

Yehova adzagumula maguwa awo ansembe

ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.

3Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu

chifukwa sitinaope Yehova.

Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,

kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”

4Mafumu amalonjeza zambiri,

amalumbira zabodza

pochita mapangano.

Kotero maweruzo amaphuka

ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.

5Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha

chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.

Anthu ake adzalirira fanolo,

chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,

amene anakondwera ndi kukongola kwake,

chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.

6Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya

ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.

Efereimu adzachititsidwa manyazi

chifukwa cha mafano ake amitengo.

7Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali

ngati kanthambi koyenda pa madzi.

8Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.

Ili ndiye tchimo la Israeli.

Minga ndi mitungwi zidzamera

ndi kuphimba maguwa awo ansembe.

Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”

ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”

9“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,

ndipo wakhala uli pomwepo.

Kodi nkhondo sinagonjetse anthu

ochita zoyipa ku Gibeya?

10Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;

mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,

kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.

11Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa

amene amakonda kupuntha tirigu,

choncho Ine ndidzayika goli

mʼkhosi lake lokongolalo.

Ndidzasenzetsa Efereimu goli,

Yuda ayenera kulima,

ndipo Yakobo ayenera kutipula.

12Mufese nokha chilungamo

ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.

Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;

pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,

mpaka Iye atabwera

kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.

13Koma inu munadzala zolakwa,

mwakolola zoyipa;

mwadya chipatso cha chinyengo.

Chifukwa mumadalira mphamvu zanu

ndiponso ankhondo anu ochulukawo,

14phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga

kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,

monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;

pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.

15Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli

chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.

Tsiku limeneli likadzafika,

mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

King James Version

Hosea 10:1-15

1Israel is an empty vine, he bringeth forth fruit unto himself: according to the multitude of his fruit he hath increased the altars; according to the goodness of his land they have made goodly images.10.1 an…: or, a vine emptying the fruit which it giveth10.1 images: Heb. statues, or, standing images 2Their heart is divided; now shall they be found faulty: he shall break down their altars, he shall spoil their images.10.2 Their heart…: or, He hath divided their heart10.2 break…: Heb. behead10.2 images: Heb. statues, or, standing images 3For now they shall say, We have no king, because we feared not the LORD; what then should a king do to us? 4They have spoken words, swearing falsely in making a covenant: thus judgment springeth up as hemlock in the furrows of the field. 5The inhabitants of Samaria shall fear because of the calves of Beth-aven: for the people thereof shall mourn over it, and the priests thereof that rejoiced on it, for the glory thereof, because it is departed from it.10.5 the priests…: or, Chemarim 6It shall be also carried unto Assyria for a present to king Jareb: Ephraim shall receive shame, and Israel shall be ashamed of his own counsel. 7As for Samaria, her king is cut off as the foam upon the water.10.7 the water: Heb. the face of the water 8The high places also of Aven, the sin of Israel, shall be destroyed: the thorn and the thistle shall come up on their altars; and they shall say to the mountains, Cover us; and to the hills, Fall on us.

9O Israel, thou hast sinned from the days of Gibeah: there they stood: the battle in Gibeah against the children of iniquity did not overtake them. 10It is in my desire that I should chastise them; and the people shall be gathered against them, when they shall bind themselves in their two furrows.10.10 when…: or, when I shall bind them for their two transgressions, or, in their two habitations 11And Ephraim is as an heifer that is taught, and loveth to tread out the corn; but I passed over upon her fair neck: I will make Ephraim to ride; Judah shall plow, and Jacob shall break his clods.10.11 her…: Heb. the beauty of her neck 12Sow to yourselves in righteousness, reap in mercy; break up your fallow ground: for it is time to seek the LORD, till he come and rain righteousness upon you. 13Ye have plowed wickedness, ye have reaped iniquity; ye have eaten the fruit of lies: because thou didst trust in thy way, in the multitude of thy mighty men. 14Therefore shall a tumult arise among thy people, and all thy fortresses shall be spoiled, as Shalman spoiled Beth-arbel in the day of battle: the mother was dashed in pieces upon her children. 15So shall Beth-el do unto you because of your great wickedness: in a morning shall the king of Israel utterly be cut off.10.15 your…: Heb. the evil of your evil