Hoseya 10 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 10:1-15

1Israeli anali mpesa wotambalala;

anabereka zipatso zambiri.

Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,

anawonjezera kumanga maguwa ansembe.

Pamene dziko lake linkatukuka,

anakongoletsa miyala yake yopatulika.

2Mtima wawo ndi wonyenga

ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.

Yehova adzagumula maguwa awo ansembe

ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.

3Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu

chifukwa sitinaope Yehova.

Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,

kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”

4Mafumu amalonjeza zambiri,

amalumbira zabodza

pochita mapangano.

Kotero maweruzo amaphuka

ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.

5Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha

chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.

Anthu ake adzalirira fanolo,

chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,

amene anakondwera ndi kukongola kwake,

chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.

6Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya

ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.

Efereimu adzachititsidwa manyazi

chifukwa cha mafano ake amitengo.

7Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali

ngati kanthambi koyenda pa madzi.

8Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.

Ili ndiye tchimo la Israeli.

Minga ndi mitungwi zidzamera

ndi kuphimba maguwa awo ansembe.

Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”

ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”

9“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,

ndipo wakhala uli pomwepo.

Kodi nkhondo sinagonjetse anthu

ochita zoyipa ku Gibeya?

10Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;

mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,

kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.

11Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa

amene amakonda kupuntha tirigu,

choncho Ine ndidzayika goli

mʼkhosi lake lokongolalo.

Ndidzasenzetsa Efereimu goli,

Yuda ayenera kulima,

ndipo Yakobo ayenera kutipula.

12Mufese nokha chilungamo

ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.

Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;

pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,

mpaka Iye atabwera

kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.

13Koma inu munadzala zolakwa,

mwakolola zoyipa;

mwadya chipatso cha chinyengo.

Chifukwa mumadalira mphamvu zanu

ndiponso ankhondo anu ochulukawo,

14phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga

kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,

monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;

pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.

15Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli

chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.

Tsiku limeneli likadzafika,

mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

Het Boek

Hosea 10:1-15

Het lot van Israël

1Wat is Israël welvarend, als een wijnstok vol druiventrossen. Maar hoe meer rijkdom God haar schonk, hoe meer altaren zij bouwde voor heidense goden. Hoe rijker de oogst, hoe mooier haar gewijde stenen. 2Het hart van deze mensen neemt een huichelachtige houding aan tegenover God. Zij zijn schuldig en zullen moeten boeten. God zal hun heidense altaren verwoesten en hun gewijde stenen vernielen. 3Dan zullen zij zeggen: ‘Wij hebben de Here verlaten en nu heeft Hij ons onze koning ontnomen. Maar wat maakt het uit? We hebben hem toch niet nodig!’ 4Zij beloven dingen die zij toch niet van plan zijn te doen. Hun rechtspraak is als giftig onkruid in de voren van een akker. 5De bevolking van Samaria maakt zich bezorgd over het afgodsbeeld van een kalf in Bet-Aven. Het volk en de afgodspriesters rouwen en treuren om de vergane glorie van het beeld. 6Maar het ding zal met hen in ballingschap meegaan naar Assyrië en als geschenk worden gegeven aan de grote koning daar. Israël zal worden uitgelachen, omdat zij op dit beeld vertrouwde en zal te schande worden gemaakt. 7Samaria wordt verwoest en haar koning zal verdwijnen als een stuk hout in de golven. 8De afgodenaltaars van Aven, waar Israël zondigde, zullen verbrokkelen. Dorens en distels zullen de restanten overwoekeren. En de mensen zullen tegen bergen roepen: ‘Val op ons neer,’ en tegen de heuvels: ‘Bedek ons!’

9‘In Gibea is het begonnen, toen hebt u voor het eerst gezondigd en bent er sindsdien niet mee opgehouden. U hebt daarna nooit meer enige vooruitgang geboekt. Was het niet terecht dat de mannen van Gibea werden weggevaagd? 10Ik zal u straffen voor uw zonden. Ik ga de legers van verschillende volken verzamelen om u daarmee de les te lezen over uw zonden. 11Israël was als een goed getrainde jonge koe die gewillig graan dorste. Ik heb haar nooit een zwaar juk opgelegd, want Ik spaarde liever haar mooie nek. Maar nu heb Ik haar ingespannen, Juda zal ploegen en Jakob zal eggen. 12Zaai gerechtigheid uit en u zult mijn liefde oogsten. Ontgin nieuw land, want het is nu de tijd om de Here te zoeken. Dan zal Hij komen en gerechtigheid over u laten regenen. 13U hebt goddeloosheid verbouwd en misdaad geoogst. U hebt uw verdiende loon gekregen door te vertrouwen op leugens: u geloofde dat militair overwicht en een grote troepenmacht uw land konden beschermen! 14Daarom zal uw volk worden getroffen door de verschrikkingen van de oorlog en al uw vestingen zullen ten val komen, net als Bet-Arbel, dat werd verwoest door Salman. Zelfs moeders en hun kinderen werden toen verpletterd. 15Dit zal ook uw lot zijn, Israël, vanwege uw grote zonden. Op een morgen zal de koning van Israël voorgoed worden uitgeschakeld.’