Hoseya 10 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 10:1-15

1Israeli anali mpesa wotambalala;

anabereka zipatso zambiri.

Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,

anawonjezera kumanga maguwa ansembe.

Pamene dziko lake linkatukuka,

anakongoletsa miyala yake yopatulika.

2Mtima wawo ndi wonyenga

ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.

Yehova adzagumula maguwa awo ansembe

ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.

3Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu

chifukwa sitinaope Yehova.

Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,

kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”

4Mafumu amalonjeza zambiri,

amalumbira zabodza

pochita mapangano.

Kotero maweruzo amaphuka

ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.

5Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha

chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.

Anthu ake adzalirira fanolo,

chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,

amene anakondwera ndi kukongola kwake,

chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.

6Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya

ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.

Efereimu adzachititsidwa manyazi

chifukwa cha mafano ake amitengo.

7Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali

ngati kanthambi koyenda pa madzi.

8Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.

Ili ndiye tchimo la Israeli.

Minga ndi mitungwi zidzamera

ndi kuphimba maguwa awo ansembe.

Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”

ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”

9“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,

ndipo wakhala uli pomwepo.

Kodi nkhondo sinagonjetse anthu

ochita zoyipa ku Gibeya?

10Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;

mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,

kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.

11Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa

amene amakonda kupuntha tirigu,

choncho Ine ndidzayika goli

mʼkhosi lake lokongolalo.

Ndidzasenzetsa Efereimu goli,

Yuda ayenera kulima,

ndipo Yakobo ayenera kutipula.

12Mufese nokha chilungamo

ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.

Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;

pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,

mpaka Iye atabwera

kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.

13Koma inu munadzala zolakwa,

mwakolola zoyipa;

mwadya chipatso cha chinyengo.

Chifukwa mumadalira mphamvu zanu

ndiponso ankhondo anu ochulukawo,

14phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga

kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,

monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;

pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.

15Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli

chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.

Tsiku limeneli likadzafika,

mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

何西阿书 10:1-15

1以色列是茂盛的葡萄树,硕果累累。

可是,他结果越多,

建造的祭坛就越多;

土地出产越丰富,

他就把神柱装饰得越美丽。

2他们心怀诡诈,必受惩罚。

耶和华要拆毁他们的祭坛,

打碎他们的神柱。

3那时他们会说:

“我们没有君王,

因为我们不敬畏耶和华。

君王能为我们做什么呢?”

4他们说虚话,起假誓,立空盟,

因此不法之事滋长,

犹如田间犁沟中蔓延的毒草。

5撒玛利亚的居民要因伯·亚文的牛犊偶像而恐惧颤抖;

祭拜它的人要哀伤,

供奉它的祭司要痛哭,

因为它的荣耀将离开他们。

6它要被带到亚述去,

作为贡物献给强大的亚述王。

以法莲因此而受人嘲笑,

以色列因自己的偶像而蒙羞。

7撒玛利亚和它的君王要被毁灭,

像漂浮在水面上的枯枝一样消逝。

8亚文10:8 亚文”指伯·亚文,伯·亚文的意思见本卷书4:15节脚注。的丘坛——以色列犯罪之地要被拆毁。

他们的祭坛上要长满荆棘和蒺藜。

他们要向高山说:“遮盖我们吧!”

对小丘说:“倒在我们身上吧!”

9耶和华说:

以色列人啊,从基比亚的日子以来,

你们一直不断地犯罪,从未改变。

难道战祸没有临到基比亚的邪恶之辈吗?

10我要按自己的心意惩罚你们。

列国要联合攻击你们,

惩罚你们的重重罪恶。

11以法莲本是驯服的母牛犊,喜欢打谷,

现在我要把轭套在它肥美的颈项上。

我要使犹大耕田,使雅各10:11 雅各”在旧约中常与“以色列”互换使用,有时指以色列人的先祖雅各,有时指以色列民族。本节的以法莲和雅各都代指北国以色列。耙地。”

12你们要为自己种植公义,

就能收获慈爱。

现在是寻求耶和华的时候,

你们要犁开刚硬的心田,

等祂来使公义如雨浇灌你们。

13可是,你们种的是邪恶,

收的是不义,

吃的是谎言的果实。

因为你们倚靠自己的力量,

仰仗众多的勇士。

14因此,战争的喧嚣将从你们中间传出,

你们的一切堡垒将被摧毁,

恰如沙勒幔摧毁伯·亚比勒

将城中的母子一同摔死。

15伯特利10:15 伯特利”此处代指以色列人。啊,你罪大恶极,

必将遭遇同样的下场。

那日来临时,以色列的王将被彻底消灭。