Hoseya 10 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 10:1-15

1Israeli anali mpesa wotambalala;

anabereka zipatso zambiri.

Pamene zipatso zawo zinanka zichuluka,

anawonjezera kumanga maguwa ansembe.

Pamene dziko lake linkatukuka,

anakongoletsa miyala yake yopatulika.

2Mtima wawo ndi wonyenga

ndipo tsopano ayenera kulangidwa chifukwa cha kulakwa kwawo.

Yehova adzagumula maguwa awo ansembe

ndi kuwononga miyala yawo yopatulika.

3Pamenepo anthuwo adzanena kuti, “Ife tilibe mfumu

chifukwa sitinaope Yehova.

Koma ngakhale tikanakhala ndi mfumu,

kodi mfumuyo ikanatichitira chiyani?”

4Mafumu amalonjeza zambiri,

amalumbira zabodza

pochita mapangano.

Kotero maweruzo amaphuka

ngati zitsamba zakupha mʼmunda umene walimidwa.

5Anthu amene amakhala mu Samariya akuchita mantha

chifukwa cha fano la mwana wangʼombe ku Beti-Aveni.

Anthu ake adzalirira fanolo,

chimodzimodzinso ansembe ake adamawo,

amene anakondwera ndi kukongola kwake,

chifukwa lachotsedwa pakati pawo ndi kupita ku ukapolo.

6Fanolo lidzatengedwa kupita ku Asiriya

ngati mphatso kwa mfumu yayikulu.

Efereimu adzachititsidwa manyazi

chifukwa cha mafano ake amitengo.

7Samariya ndi mfumu yake adzatengedwa kupita kutali

ngati kanthambi koyenda pa madzi.

8Malo opembedzerako mafano a ku Aveni adzawonongedwa.

Ili ndiye tchimo la Israeli.

Minga ndi mitungwi zidzamera

ndi kuphimba maguwa awo ansembe.

Kenaka anthu adzawuza mapiri kuti, “Tiphimbeni!”

ndipo adzawuza zitunda kuti, “Tigwereni!”

9“Iwe Israeli, wachimwa kuyambira mʼmasiku a Gibeya,

ndipo wakhala uli pomwepo.

Kodi nkhondo sinagonjetse anthu

ochita zoyipa ku Gibeya?

10Pamene ndifunire, ndidzalanga anthuwo;

mitundu ya anthu idzasonkhanitsidwa kudzalimbana nawo,

kuwayika mʼndende chifukwa cha uchimo wawo waukulu.

11Efereimu ndi mwana wangʼombe wamkazi wophunzitsidwa

amene amakonda kupuntha tirigu,

choncho Ine ndidzayika goli

mʼkhosi lake lokongolalo.

Ndidzasenzetsa Efereimu goli,

Yuda ayenera kulima,

ndipo Yakobo ayenera kutipula.

12Mufese nokha chilungamo

ndipo mudzakolola chipatso cha chikondi changa chosasinthika.

Ndipo tipulani munda wanu wosalimidwawo;

pakuti ino ndi nthawi yofunafuna Yehova,

mpaka Iye atabwera

kudzakugwetserani mivumbi ya chilungamo.

13Koma inu munadzala zolakwa,

mwakolola zoyipa;

mwadya chipatso cha chinyengo.

Chifukwa mumadalira mphamvu zanu

ndiponso ankhondo anu ochulukawo,

14phokoso lankhondo lidzamveka pakati pa anthu anga

kotero kuti malinga anu onse adzawonongeka,

monga momwe Salimani anawonongera Beti-Aribeli pa nthawi ya nkhondo;

pamene anapha amayi pamodzi ndi ana awo omwe.

15Momwemonso zidzakuchitikira, iwe Beteli

chifukwa kuyipa kwako ndi kwakukulu.

Tsiku limeneli likadzafika,

mfumu ya Israeli idzawonongedwa kwathunthu.

Священное Писание

Осия 10:1-15

1Исраил – ветвистый виноград;

он производил плод для себя.

Чем больше было у него плодов,

тем больше он возводил жертвенников;

чем плодороднее была его земля,

тем лучше он украшал свои священные камни.

2Их сердце обманчиво,

и теперь они должны понести наказание.

Вечный разрушит их жертвенники

и уничтожит их священные камни.

3Тогда они скажут: «У нас нет царя,

потому что мы не почитали Вечного.

Но даже если бы и был у нас царь,

то что бы он мог сделать для нас?»

4Они говорят пустые слова,

дают ложные клятвы

и заключают бесполезные соглашения,

поэтому несправедливый суд процветает у них,

как ядовитые сорняки на вспаханном поле.

5Жители Самарии будут бояться

за идола-тельца Бет-Авена («дома зла»)10:5 См. сноску на 4:15..

Его народ и его жрецы,

что радовались славе идола,

будут скорбеть по нему,

потому что слава отойдёт от него.

6Он будет унесён в Ассирию

в дар великому царю10:6 Или: «царю Иареву»..

Ефраим будет опозорен,

Исраил будет постыжен за свой совет10:6 Или: «за своих деревянных идолов»..

7Самария и её царь уплывут,

как ветка по течению.

8Капища зла10:8 Букв.: «Авен». Имеется в виду Бет-Авен; см. сноску на 4:15., грех Исраила, будут уничтожены,

колючки и сорняки вырастут на их жертвенниках.

Тогда люди скажут горам: «Покройте нас!» –

и холмам: «Падите на нас!»

9– Ты грешил со времён Гивы10:9 См. Суд. 19–20., Исраил,

и таким ты и остался.

Разве война не настигла

беззаконников в Гиве?

10По Моему желанию Я накажу их:

народы соберутся против них,

чтобы надеть на них оковы за их двойной грех.

11Ефраим – приученная телица,

привыкшая молотить зерно.

Итак, Я Сам надену ярмо

на её тучную шею.

Я запрягу Ефраима;

на Иудее буду пахать,

а на Якубе боронить.

12Сейте для себя праведность,

и пожнёте плоды верной любви;

распашите свою целину,

потому что настало время искать Вечного,

пока Он не придёт

и не изольёт на вас праведность, как дождь.

13Но вы сеяли беззаконие,

пожинали зло

и съели плод лжи.

Так как вы полагались на свою силу

и на множество своих воинов,

14рёв войны поднимется против вашего народа,

и все ваши крепости будут разрушены.

Как Салман разрушил Бет-Арбел в день битвы,

когда матери вместе со своими детьми были забиты до смерти,

15так будет и с тобою, Вефиль,

потому что велики твои злодеяния.