Hoseya 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 1:1-11

1Awa ndi mawu amene Yehova anayankhula kwa Hoseya mwana wa Beeri pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda ndiponso pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu mwana wa Yowasi mfumu ya ku Israeli.

Mkazi wa Hoseya ndi Ana Ake

2Yehova atayamba kuyankhula kudzera mwa Hoseya, Yehova anati kwa Hoseyayo, “Pita kakwatire mkazi wachiwerewere ndipo ubereke naye ana mʼchiwerewere chake pakuti anthu a mʼdziko muno achimwa pochita chigololo choyipitsitsa, posiya Yehova.” 3Motero Hoseya anakwatira Gomeri mwana wamkazi wa Dibulaimu, ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna.

4Tsono Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti Yezireeli, pakuti ndili pafupi kulanga banja la Yehu chifukwa cha anthu amene anawapha ku Yezireeli ndipo ndidzathetsa ufumu wa Israeli. 5Tsiku limenelo ndidzathyola uta wa Israeli mʼchigwa cha Yezireeli.”

6Gomeri anakhala woyembekezeranso ndipo anabereka mwana wamkazi. Ndipo Yehova anati kwa Hoseya, “Umutche dzina loti ‘Sakondedwa’ pakuti sindidzaonetsanso chikondi changa pa nyumba ya Israeli, kuti ndingawakhululukire konse. 7Komatu ndidzaonetsa chikondi pa nyumba ya Yuda; ndipo ndidzawapulumutsa, osati ndi uta, lupanga kapena nkhondo, kapena akavalo ndi okwerapo ake, koma ine Yehova Mulungu wawo ndidzawapulumutsa.”

8Sakondedwa ataleka kuyamwa, Gomeri anabereka mwana wina wamwamuna. 9Pamenepo Yehova anati, “Umutche dzina loti Sianthuanga,” pakuti inu si ndinu anthu anga ndipo Ine si ndine Mulungu wanu.

10“Komabe Aisraeli adzachuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja umene sangathe kuwuyeza kapena kuwuwerenga. Pamalo omwe ananena kuti, ‘Sindinu anthu anga,’ pomweponso adzawatchula kuti ‘Ana a Mulungu wamoyo.’ 11Anthu a ku Yuda ndi anthu a ku Israeli adzasonkhananso pamodzi ndipo adzasankha mtsogoleri mmodzi ndi kutuluka mʼdzikomo, pakuti tsiku la Yezireeli lidzakhala lalikulu kwambiri.”

New Serbian Translation

Књига пророка Осије 1:1-11

1Ово је Господња реч која је дошла Осији, Веировом сину, у време Јудиних царева Озије, Јотама, Ахаза и Језекије, и у време израиљског цара Јеровоама, Јоасовог сина.

Осијина жена и деца

2Господ је почео да говори преко Осије. Рекао је Осији: „Иди и ожени блудницу с децом блуда, јер је земља огрезла у блудништву, одметнула се од Господа.“ 3И он је отишао и оженио Гомеру, ћерку Дивлаимову, а она је затруднела и родила му сина.

4Господ му је рекао: „Назови га Језраел1,4 Језраел значи Бог сеје., јер ћу убрзо да казним Јујев дом због покоља Језраела. Окончаћу царство дома Израиљевог! 5Тога дана сломићу лук Израиљев у долини језраелској.“

6Она је поново затруднела и родила ћерку. И он му рече: „Назови је Ло-Рухама1,6 Ло-Рухама значи непомилована., јер се више нећу смиловати дому Израиљевом и сигурно им нећу опростити. 7А на дом Јудин ћу се смиловати, спашћу их ја – Господ, њихов Бог – нећу да их спасем луком и мачем, битком, коњима и коњаницима.“

8А када је одојила Ло-Рухаму затруднела је и родила сина. 9Бог је рекао: „Назови га Ло-Ами1,9 Ло-Ами значи није мој народ., јер ви нисте мој народ и ја нисам ваш Бог.

10Израиљци ће бити бројни као морски песак без мере и броја; а на месту где им се рекло: ’Ви нисте народ мој’, назваће се ’синовима живога Бога.’ 11Сабраће се народ Јуде и народ Израиља заједно, па ће себи поставити једног главара. И отићи ће из земље јер ће онај дан бити велики за Језраел.