Hagai 1 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 1:1-15

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

New International Reader’s Version

Haggai 1:1-15

Haggai Tells His People to Rebuild the Lord’s Temple

1A message from the Lord came to Haggai the prophet. Haggai gave it to Zerubbabel and Joshua. Zerubbabel was governor of Judah and the son of Shealtiel. Joshua was high priest and the son of Jozadak. The message came on the first day of the sixth month of the second year that Darius was king of Persia. Here is what Haggai said.

2Here is what the Lord who rules over all says. “The people of Judah say, ‘It’s not yet time to rebuild the Lord’s temple.’ ”

3So the message from the Lord came to me. The Lord said, 4“My temple is still destroyed. But you are living in your houses that have beautiful wooden walls.”

5The Lord who rules over all says, “Think carefully about how you are living. 6You have planted many seeds. But the crops you have gathered are small. So you eat. But you never have enough. You drink. But you are never full. You put on your clothes. But you are not warm. You earn your pay. But it will not buy everything you need.”

7He continues, “Think carefully about how you are living. 8Go up into the mountains. Bring logs down. Use them to rebuild the temple, my house. Then I will enjoy it. And you will honor me,” says the Lord. 9“You expected a lot. But you can see what a small amount it turned out to be. I blew away what you brought home. I’ll tell you why,” announces the Lord who rules over all. “Because my temple is still destroyed. In spite of that, each one of you is busy with your own house. 10So because of what you have done, the heavens have held back the dew. And the earth has not produced its crops. 11I ordered the rain not to fall on the fields and mountains. Then the ground did not produce any grain. There were not enough grapes to make fresh wine. The trees did not bear enough olives to make oil. People and cattle suffered. All your hard work failed.”

12Zerubbabel was the son of Shealtiel. Joshua the high priest was the son of Jozadak. They obeyed the Lord their God. So did all the Lord’s people who were still left alive. The Lord had given his message to them through me. He had sent me to speak to them. And the people had respect for him.

13Haggai was the Lord’s messenger. So Haggai gave the Lord’s message to the people. He told them, “The Lord announces, ‘I am with you.’ ” 14So the Lord stirred up the spirits of Zerubbabel, the governor of Judah, and Joshua the high priest. The Lord also stirred up the rest of the people to help them. Then everyone began to work on the temple of the Lord who rules over all. He is their God. 15It was the 24th day of the sixth month.

The New Temple Will Be Beautiful

In the second year of King Darius,