Hagai 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hagai 1:1-15

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

1Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

2Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

3Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, 4“Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

5Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. 6Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

7Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. 8Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. 9“Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

哈該書 1:1-15

耶和華命令百姓重建聖殿

1大流士王執政第二年六月一日,耶和華藉著先知哈該撒拉鐵的兒子猶大省長所羅巴伯約撒答的兒子大祭司約書亞說:

2「萬軍之耶和華說,『這些百姓說,重建耶和華殿的時候還沒到。』」 3因此,耶和華對先知哈該說: 4「這殿還是一片廢墟,你們卻住在華麗的房子裡。 5萬軍之耶和華說,你們要認真反省自己的行為。 6你們種多收少,吃不飽,喝不足,穿不暖,掙來的工錢卻放在漏口袋中。」

7萬軍之耶和華說:「你們要認真反省自己的行為。 8你們要上山伐木,重建這殿,好讓我歡喜並得到尊崇。這是耶和華說的。 9你們盼望豐收,結果收的很少;你們把收成帶回家,我卻把它們吹走。這是什麼緣故?萬軍之耶和華告訴你們,『因為你們都忙於建自家的房子,任由我的殿一片廢墟。 10所以,天不降雨露,地無出產。 11我讓旱災臨到大地、群山、五穀、葡萄、橄欖等地裡的出產以及人畜,使你們一切的勞碌付諸東流。』」

12撒拉鐵的兒子猶大省長所羅巴伯約撒答的兒子大祭司約書亞和所有的餘民1·12 餘民」指「從流亡之地歸回的人」。聽到他們的上帝耶和華藉先知哈該所講的話,都順服耶和華的話。百姓都敬畏耶和華。 13耶和華的使者哈該向百姓傳達耶和華的話,說:「耶和華說,『我與你們同在。』」 14耶和華感動撒拉鐵的兒子猶大省長所羅巴伯約撒答的兒子大祭司約書亞和所有的餘民,他們就動工建造他們的上帝萬軍之耶和華的殿, 15時值大流士王執政第二年六月二十四日。