Habakuku 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 3:1-19

Pemphero la Habakuku

1Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.

2Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu;

Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa.

Muzichitenso masiku athu ano,

masiku athu ano zidziwike;

mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.

3Mulungu anabwera kuchokera ku Temani,

Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani.

Sela

Ulemerero wake unaphimba mlengalenga

ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.

4Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa;

kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake,

mʼmene anabisamo mphamvu zake.

5Patsogolo pake pankagwa mliri;

nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.

6Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi;

anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera.

Mapiri okhazikika anagumuka

ndipo zitunda zakalekale zinatitimira.

Njira zake ndi zachikhalire.

7Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto,

mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.

8Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje?

Kodi munakalipira timitsinje?

Kodi munapsera mtima nyanja

pamene munakwera pa akavalo anu

ndiponso magaleta anu achipulumutso?

9Munasolola uta wanu mʼchimake,

munayitanitsa mivi yambiri.

Sela

Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;

10mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka.

Madzi amphamvu anasefukira;

nyanja yozama inakokoma

ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.

11Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga,

pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo,

pa kunyezimira kwa mkondo wanu.

12Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali,

ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.

13Munapita kukalanditsa anthu anu,

kukapulumutsa wodzozedwa wanu.

Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa,

munawononga anthu ake onse.

Sela

14Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake

pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa,

ankasangalala ngati kuti akudzawononga

osauka amene akubisala.

15Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu,

kuvundula madzi amphamvu.

16Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri,

milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo;

mafupa anga anaguluka,

ndipo mawondo anga anawombana.

Komabe ndikuyembekezera mofatsa,

tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.

17Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa,

ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa.

Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso,

ndipo mʼminda musatuluke kanthu.

Ngakhale nkhosa

ndi ngʼombe zithe mʼkhola,

18komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova,

ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.

19Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga;

amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi,

amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri.

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

哈巴谷书 3:1-19

哈巴谷的祷告

1以下是哈巴谷先知的祷告,采用流离调3:1 流离调是希伯来诗歌的一种曲调。

2耶和华啊,我听过你的威名;

耶和华啊,我对你的作为充满敬畏。

求你如今再次彰显你的作为,

求你发怒的时候仍以怜悯为念。

3上帝从提幔来,

圣者从巴兰山来。(细拉)

祂的荣耀遮蔽诸天,

颂赞祂的声音响彻大地。

4祂的荣光犹如太阳的光辉,

祂的手射出光芒,

其中蕴藏着大能。

5瘟疫行在祂前面,

灾病跟在祂脚后。

6祂停下,大地就震动;

祂观看,万民就战栗。

古老的山岳崩裂,

远古的丘陵塌陷,

但祂的作为永远不变。

7我看见古珊的帐篷遭难,

米甸人的幔子颤抖。

8耶和华啊,你是向江河发怒吗?

你乘着得胜的战车而来,

是向江河生气吗?

是向海洋发怒吗?

9你拿出弓,要射出许多箭羽。(细拉)

你以江河分开大地。

10群山看见你就战栗,

大雨倾盆,

深渊翻腾,波浪滔天。

11你射出的箭闪闪发光,

你的枪熠熠生辉,

以致日月都停在天上。

12你怀着烈怒走遍大地,

践踏万国。

13你出来是为了拯救你的子民,

拯救你膏立的王。

你打垮邪恶之人的首领,

从头到脚彻底毁灭他们。(细拉)

14他们的军队如旋风而至,

要驱散我们,

他们以暗中吞噬贫民为乐,

但你用他们的矛刺透他们的头颅。

15你骑马践踏汹涌的大海。

16我听到这些,

就胆战心惊,嘴唇哆嗦,

四肢无力,双腿发抖。

但我仍要静候灾难临到入侵者的日子。

17即使无花果树不发芽,

葡萄树不结果,

橄榄树无收成,

田地不产粮,

圈里没有羊,

棚里没有牛,

18我仍要因耶和华而欢欣,

因拯救我的上帝而喜乐。

19主耶和华是我的力量,

祂使我的脚如母鹿的蹄,

稳行在高处。

这首歌交给乐长,用弦乐器伴奏。