Habakuku 2 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 2:1-20

1Ndidzakhala pa malo anga aulonda,

ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo;

ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze,

ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.

Yankho la Yehova

2Tsono Yehova anandiyankha, nati:

“Lemba masomphenyawa

ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale

kuti wowerenga awawerenge mosavuta.

3Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake;

masomphenyawa akunena zamʼtsogolo

ndipo sizidzalephera kuchitika.

Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere;

zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.

4“Taona, mdani wadzitukumula;

zokhumba zake sizowongoka,

koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.

5Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo;

ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika.

Pakuti ngodzikonda ngati manda,

ngosakhutitsidwa ngati imfa,

wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu

ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse.

6“Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti,

“Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake

ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda!

Kodi izi zidzachitika mpaka liti?

7Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi?

Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha?

Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.

8Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu,

mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

9“Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo,

kukweza malo ake okhalapo,

kuthawa mavuto!

10Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu,

kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.

11Mwala pa khoma udzafuwula,

ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.

12“Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi

ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!

13Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize

kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto,

ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?

14Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova,

monga momwe madzi amadzazira nyanja.

15“Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa,

kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera,

kuti aone umaliseche wawo.

16Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero.

Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere!

Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe,

ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.

17Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni,

ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga.

Pakuti wakhetsa magazi a anthu;

wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.

18“Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu,

kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza?

Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake;

amapanga mafano amene samatha kuyankhula.

19Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’

Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’

Kodi zimenezi zingathe kulangiza?

Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva;

mʼkati mwake mulibe mpweya.

20Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika;

dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”

Luganda Contemporary Bible

Kaabakuuku 2:1-20

Obulamu eri Abatuukirivu

12:1 a Is 21:8 b Zab 48:13 c Zab 85:8 d Zab 5:3Kale ndiyimirira mu kifo kyange we ntera okubeera

ntunule nga ndi waggulu eyo ku ggulumu

nnindirire ky’aliŋŋamba,

era ne kye ndimuddamu ekikwata ku kwemulugunya kw’abantu.

22:2 Kub 1:19Awo Mukama n’anziramu n’ayogera nti,

“Wandiika okwolesebwa okwo ku bipande.

Kuwandiike bulungi

ate omubaka gwe banaatuma, akutwale bunnambiro.

32:3 a Dan 8:17; 10:14 b Zab 27:14 c Ez 12:25; Beb 10:37-38Kubanga okwolesebwa okwo kujja mu kiseera kyakwo ekigere.

Kwogera ku by’enkomerero

ate si kwa bulimba.

Bwe kunaaba ng’okuluddewo, mukulindirire,

kujja kutuukirira, tekugya kulwa.

42:4 Bar 1:17*; Bag 3:11*; Beb 10:37-38*“Laba oyo ow’emmeeme eteri nnongoofu wa kugwa,

naye omutuukirivu aliba mulamu olw’obwesigwa bwe.”

Akabi eri Aboonoonyi

52:5 a Nge 20:1 b Nge 27:20; 30:15-16Weewaawo, omwenge mulimba

guleetera omuntu amalala, ate taguwummulako.

Ate olwokubanga gwa mululu ng’emagombe, mu butakkuta gufaanana okufa.

Era okufaanana ng’olumbe, tegukkuta,

amawanga gonna gugeekuŋŋanyizaako

ne gugafuula abasibe.

62:6 a Is 14:4 b Am 2:8“Bano bonna si be balimugererako engero bamusekerere nga bagamba nti,

“ ‘Zimusanze oyo eyeyongeza ebitali bibye!

Oyo eyeetuumako obugagga obuva mu nguzi!’

72:7 Nge 29:1Abakubanja tebalikuyimukirako nga tomanyiridde,

era tebalizuukuka ne bakweraliikiriza?

Oliba togudde mu mikono gyabwe?

82:8 a Is 33:1; Zek 2:8-9 b nny 17Kubanga onyaze amawanga mangi,

abantu abasigaddewo balikunyaga;

Oyiye omusaayi gw’abantu,

n’oyonoona ensi n’ebibuga n’abantu bonna ababibeeramu.”

92:9 Yer 22:13Zimusanze oyo azimbira amaka ge ku bikolwa ebibi,

azimba ekisu kye waggulu,

okwekuuma obutatuukwako kabi!

102:10 a Yer 26:19 b nny 16Wategeka okuzikirira kw’abantu bangi,

n’oswaza ennyumba yo ne weefiiriza obulamu bwo.

112:11 Yos 24:27; Luk 19:40Amayinja g’oku bbugwe galikaaba,

n’emikiikiro gy’ebibajje girikyasanguza.

122:12 Mi 3:10Zimusanze oyo azimba ekibuga n’omusaayi,

atandika ekibuga n’obutali butuukirivu.

132:13 a Is 50:11 b Is 47:13Tekyategekebwa Mukama ow’Eggye

nti okutegana kw’abantu nku buku za muliro,

n’amawanga geemalamu ensa olw’ebintu ebitaliimu?

142:14 a Kbl 14:21 b Is 11:9Kubanga ensi erijjula okumanya ekitiibwa kya Mukama,

ng’amazzi bwe ganjaala ku nnyanja.

15Zimusanze oyo awa baliraanwa be ekitamiiza

n’akibafukira okuva mu kita n’abawa banywe okutuusa lwe batamiira

asobole okutunuulira ensonyi zaabwe!

162:16 a nny 10 b Kgb 4:21 c Is 51:22Olijjuzibwa ensonyi mu kifo ky’ekitiibwa.

Naawe olinywa n’oswala.

Ekikompe eky’omu mukono gwa Mukama ogwa ddyo kirikyusibwa kidde gy’oli,

n’ensonyi ez’obuwemu zisaanikire ekitiibwa kyo.

172:17 a Yer 51:35 b Yer 50:15 c nny 8Ebikolwa eby’obukambwe bye watuusa ku Lebanooni,

n’okutta ensolo, birikutiisa.

Osse abantu

n’ozikkiriza ensi n’ebibuga n’abantu ababibeeramu.

182:18 a Yer 5:21 b Zab 115:4-5; Yer 10:14“Ekifaananyi ekyole kigasa ki? Anti kibajje bubazzi.

Oba ekifaananyi eky’ekyuma, ekisomesa obulimba?

Kubanga omuweesi yeesiga mirimu gya mikono gye

nga akola ebifaananyi ebitayogera!

192:19 a 1Bk 18:27 b Yer 10:4Zimusanze oyo agamba omuti nti, ‘Lamuka;’

agamba ejjinja nti, ‘Golokoka!’

Kino kisobola okuluŋŋamya?

Kibikiddwa zaabu ne ffeeza,

so tekiriimu bulamu n’akatono.

202:20 a Zab 11:4 b Is 41:1Naye Mukama ali mu yeekaalu ye entukuvu:

ensi zonna zisiriikirire mu maaso ge.”