Habakuku 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 1:1-17

1Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

2Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,

koma wosayankha?

Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”

koma wosatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?

Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?

Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;

pali ndewu ndi kukangana kwambiri.

4Kotero malamulo anu atha mphamvu,

ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oyipa aposa olungama,

kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

5“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,

ndipo muthedwe nazo nzeru.

Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu

zimene inu simudzazikhulupirira,

ngakhale wina atakufotokozerani.

6Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,

anthu ankhanza ndiponso amphamvu,

amene amapita pa dziko lonse lapansi

kukalanda malo amene si awo.

7Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;

amadzipangira okha malamulo

ndi kudzipezera okha ulemu.

8Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku

ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.

Okwerapo awo akuthamanga molunjika;

a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,

akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;

9onse akubwera atakonzekera zachiwawa.

Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu

ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Akunyoza mafumu

ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.

Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;

akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.

11Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,

anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?

Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.

Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;

Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;

Inu simulekerera cholakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?

Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa

akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?

14Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,

ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.

15Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,

amawakola mu ukonde wake,

amawasonkhanitsa mu khoka lake;

kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.

16Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake

ndiponso kufukizira lubani khoka lake,

popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba

ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.

17Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,

kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

New Serbian Translation

Књига пророка Авакума 1:1-17

1Пророштво које је видео пророк Авакум:

Авакумова жалопојка

2О, Господе, докле да вапим за помоћ,

а ти ме не чујеш!

Вичем о насиљу,

а ти не спасаваш!

3Зашто дајеш да гледам поквареност,

да видим невољу?

Разарање и насиље су пред очима мојим.

Ено, и насиље и неслога се дижу.

4Зато Закон губи снагу,

зато правди никада нема места.

Злотвор опкољава праведника

и зато има места за правду искварену.

Господњи одговор

5„У народе погледајте,

чудите се и дивите,

јер, ево, учинићу нешто у ваше дане,

у шта не бисте веровали

да вам ко исприча.

6Јер, ево подижем Халдејце,

суров и нагао народ

да широм земље

осваја туђа насеља.

7Страховит је и ужасан;

он одлучује шта је правда,

а шта достојанство.

8Коњи су им хитрији од рисова

и свирепији од вукова у сумрак.

Коњаници им галопирају,

долазе издалека њихови коњаници;

лете, обрушавају се као лешинар

што би да ждере.

9Сви долазе због насиља,

хорде су им окренуте истоку,

а заробљенике сакупљају

као да су песак.

10Он се руга и царевима

и са владарима се шегачи.

Сваком се утврђењу смеје

док земљане насипе прави и осваја их.

11Као ветар тада завиори и мине,

али крив је тај коме је божанство његова снага.“

Авакумова друга жалопојка

12О, Господе, зар ти ниси од давнина, мој Боже свети?

Нећемо ми умрети!

О, Господе, за суд си их одредио.

О, Стено, за прекор си их учврстио.

13Пречисте су очи твоје да би зло проматрале,

ти пакост не можеш да гледаш.

Зашто онда трпиш невернике,

ћутиш док зликовац прождире праведнијег од себе?

14Створио си људе као рибе у мору

и као гмизавце што владара немају међу собом.

15И он их све удицом вади,

вуче их својом мрежом

и у мрежу их скупља.

Зато се и радује и ликује.

16Зато својој мрежи жртвује,

пали тамјан мрежи својој,

јер му она даје мастан оброк

и обиље хране.

17И хоће ли због тога да празни мрежу своју,

да истрајно сатирате народе без задршке?