Genesis 9 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 9:1-29

Pangano la Mulungu ndi Nowa

1Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi. 2Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire. 3Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.

4“Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda. 5Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.

6“Aliyense wopha munthu,

adzaphedwanso ndi munthu;

pakuti Mulungu analenga munthu

mʼchifanizo chake.

7Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”

8Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti, 9“Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo, 10pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe. 11Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”

12Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo. 13Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi. 14Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka, 15ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi. 16Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

17Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”

Ana Aamuna a Nowa

18Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani. 19Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.

20Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa. 21Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche. 22Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja. 23Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.

24Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira, 25anati,

“Atembereredwe Kanaani!

Adzakhala kapolo

wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”

26Anatinso,

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu!

Kanaani akhale kapolo wa Semu.

27Mulungu akulitse dziko la Yafeti;

Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu,

ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”

28Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350. 29Anamwalira ali ndi zaka 950.

Nueva Versión Internacional

Génesis 9:1-29

El pacto de Dios con Noé

1Dios bendijo a Noé y a sus hijos con estas palabras: «¡Sean fructíferos, multiplíquense y llenen la tierra! 2Todos los animales de la tierra tendrán temor y miedo ante ustedes: las aves, las bestias salvajes, los animales que se arrastran por el suelo y los peces del mar. Todos estarán bajo su dominio. 3Todo lo que se mueve y tiene vida, al igual que las verduras, les servirá de alimento. Yo les doy todo esto.

4»Pero no deberán comer carne con sangre; la sangre es vida. 5Por cierto, de la sangre de ustedes yo habré de pedirles cuentas. A todos los animales y a todos los seres humanos pediré cuentas de la vida de sus semejantes.

6»Si alguien derrama la sangre de un ser humano,

otro ser humano derramará la suya,

porque el ser humano ha sido creado

a imagen de Dios mismo.

7»En cuanto a ustedes, sean fructíferos y multiplíquense; sí, multiplíquense y llenen la tierra».

8Dios habló otra vez a Noé y a sus hijos y dijo: 9«Yo establezco mi pacto con ustedes, con sus descendientes 10y con todos los seres vivientes que están con ustedes, es decir, con todos los seres vivientes de la tierra que salieron del arca: las aves, y los animales domésticos y salvajes. 11Este es mi pacto con ustedes: Nunca más serán exterminados todos los seres vivientes por las aguas de un diluvio; nunca más habrá un diluvio que destruya la tierra».

12Y Dios añadió: «Esta es la señal del pacto que establezco para siempre con ustedes y con todos los seres vivientes que los acompañan: 13He colocado mi arcoíris en las nubes, el cual servirá como señal de mi pacto con la tierra. 14Cuando yo cubra la tierra de nubes y en ellas aparezca el arcoíris, 15me acordaré del pacto que he establecido con ustedes y con todos los seres vivientes. Nunca más las aguas se convertirán en un diluvio para destruir a todos los mortales. 16Cada vez que aparezca el arcoíris entre las nubes, yo lo veré y me acordaré del pacto que establecí para siempre con todos los seres vivientes que hay sobre la tierra».

17Dios concluyó diciéndole a Noé: «Esta es la señal de mi pacto, que establezco con todos los seres vivientes que hay en la tierra».

Los hijos de Noé

18Los hijos de Noé que salieron del arca fueron: Sem, Cam y Jafet. Cam fue el padre de Canaán. 19Estos fueron los tres hijos de Noé que con su descendencia poblaron toda la tierra.

20Noé se dedicó a cultivar la tierra y plantó una viña. 21Un día, bebió vino y se embriagó, quedándose desnudo dentro de su tienda de campaña. 22Cam, el padre de Canaán, vio la desnudez de su padre y fue a contárselo a sus hermanos que estaban afuera. 23Entonces Sem y Jafet tomaron un manto, se lo echaron sobre los hombros y caminando hacia atrás, cubrieron la desnudez de su padre. Como miraban en dirección opuesta, no vieron la desnudez de su padre.

24Cuando Noé despertó de su borrachera y se enteró de lo que su hijo menor había hecho, 25declaró:

«¡Maldito sea Canaán!

Será de sus dos hermanos

el más bajo de sus esclavos».

26Y agregó:

«¡Bendito sea el Señor, Dios de Sem!

¡Que Canaán sea su esclavo!

27¡Que Dios extienda el territorio de Jafet!9:27 En hebreo, el nombre propio Jafet suena como el verbo que significa extender.

¡Que habite Jafet en los campamentos de Sem

y que Canaán sea su esclavo!».

28Después del diluvio Noé vivió trescientos cincuenta años más, 29de modo que murió a la edad de novecientos cincuenta años.