Genesis 7 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 7:1-24

1Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu. 2Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso. 3Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi. 4Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”

5Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.

6Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600. 7Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula. 8Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo. 9Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu. 10Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.

11Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka. 12Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.

13Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo. 14Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake. 15Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse. 16Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.

17Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko. 18Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo. 19Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa. 20Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri. 21Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu. 22Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa. 23Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.

24Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

Nueva Versión Internacional

Génesis 7:1-24

1El Señor dijo a Noé: «Entra en el arca con toda tu familia porque tú eres el único hombre justo que he encontrado de esta generación. 2De todos los animales puros, lleva siete machos y siete hembras; pero de los impuros, solo un macho y una hembra. 3Lleva también siete machos y siete hembras de las aves del cielo, para conservar su especie sobre la tierra. 4Porque dentro de siete días haré que llueva sobre la tierra durante cuarenta días y cuarenta noches, y así borraré de la superficie de la tierra a todo ser viviente que hice».

5Noé hizo todo de acuerdo con lo que el Señor había mandado.

6Tenía Noé seiscientos años cuando las aguas del diluvio inundaron la tierra. 7Entonces, para salvarse de las aguas del diluvio, entró en el arca junto con sus hijos, su esposa y sus nueras. 8De los animales puros e impuros, de las aves y de todos los seres que se arrastran por el suelo, 9entraron con Noé por parejas, el macho y su hembra, tal como Dios se lo había mandado. 10Al cabo de los siete días, las aguas del diluvio comenzaron a caer sobre la tierra.

11Cuando Noé tenía seiscientos años, precisamente en el día diecisiete del mes segundo, se reventaron las fuentes del mar profundo y se abrieron las compuertas del cielo. 12Cuarenta días y cuarenta noches llovió sobre la tierra.

13Ese mismo día entraron en el arca Noé, sus hijos Sem, Cam y Jafet, su esposa y sus tres nueras. 14Junto con ellos entró toda clase de animales salvajes y domésticos, de animales que se arrastran por el suelo y de aves. 15Así entraron en el arca con Noé parejas de todos los seres vivientes; 16entraron un macho y una hembra de cada especie, tal como Dios se lo había mandado a Noé. Luego el Señor cerró la puerta del arca.

17El diluvio cayó sobre la tierra durante cuarenta días. Cuando crecieron las aguas, elevaron el arca por encima de la tierra. 18Las aguas crecían y aumentaban cada vez más, pero el arca se mantenía a flote sobre ellas. 19Tanto crecieron las aguas, que cubrieron las montañas más altas que hay debajo de los cielos. 20El nivel del agua subió más de quince codos7:20 Es decir, aprox. 7 m. por encima de las montañas. 21Así murió todo ser viviente que se movía sobre la tierra: las aves, los animales salvajes y domésticos, todo tipo de animal que se arrastraba por el suelo y todo ser humano. 22Pereció todo ser que habitaba la tierra seca y tenía aliento de vida. 23Dios borró de la faz de la tierra a todo ser viviente, desde los seres humanos hasta los ganados, los reptiles y las aves del cielo. Todos fueron borrados de la faz de la tierra. Solo quedaron Noé y los que estaban con él en el arca.

24Y la tierra quedó inundada ciento cincuenta días.