Genesis 7 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 7:1-24

1Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu. 2Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso. 3Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi. 4Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”

5Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.

6Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600. 7Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula. 8Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo. 9Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu. 10Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.

11Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka. 12Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.

13Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo. 14Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake. 15Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse. 16Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.

17Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko. 18Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo. 19Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa. 20Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri. 21Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu. 22Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa. 23Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.

24Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

New Serbian Translation

1. Мојсијева 7:1-24

1Тада Господ рече Ноју: „Уђи у пловило ти и цела твоја породица, јер видим да си ти једини праведан преда мном у овом нараштају. 2Од свих чистих животиња узми са собом по седам парова: мужјака са женком, а од животиња које нису чисте узми по пар: мужјака са женком. 3Исто тако и од свих птица небеских узми по седам парова: мужјака са женком, да би им се сачувало потомство на целој земљи. 4Наиме, за седам дана ћу пустити кишу да пада на земљу четрдесет дана и четрдесет ноћи, те ћу истребити с лица земље свако живо биће које сам начинио.“

5Ноје учини све како му је Господ заповедио.

6Ноју је било шест стотина година када је потоп дошао на земљу. 7Због вода потопа Ноје уђе у пловило са својим синовима, својом женом и женама својих синова. 8Од свих чистих животиња и од животиња које нису чисте, од птица и од свега што пузи по земљи, 9уђе к Ноју у пловило по двоје, мужјак и женка, као што је Бог заповедио Ноју. 10Када се навршило седам дана, навале воде потопа на земљу.

11Шестстоте године Нојевог живота, другог месеца, седамнаестога дана тог месеца, провале сви извори великог бездана и отворе се сва окна на небесима. 12Киша је пљуштала по земљи четрдесет дана и четрдесет ноћи.

13Тог истог дана7,13 Изворни приповедачки стил наизглед противуречи времену уласка Ноја и породице у пловило, према стиховима 1-4. уђу у пловило Ноје и његови синови: Сим, Хам и Јафет, Нојева жена и три жене његових синова. 14Са њима су ушле све животиње по својим врстама: стока, гмизавци што пузе по земљи и свакојаке птице, све што има крила. 15Ушли су к Ноју у пловило двоје по двоје од сваког бића што у себи има дах живота. 16Животиње које су ушле унутра биле су пар: мушко и женско од сваког бића, баш као што је Бог заповедио Ноју. Затим је Господ затворио врата за њим.

17Потоп је трајао на земљи четрдесет дана. Вода је непрестано расла, тако да је понела пловило које се одигло од земље. 18Вода је наваљивала и подигла се високо над земљом, па је пловило почело да плови по површини воде. 19Вода је наваљивала све јаче и јаче над земљом, те је прекрила све највише горе под целим небом. 20Набујала вода се уздигла петнаест лаката7,20 Око 7.5 m. поврх гора. 21Тако су изгинула сва бића која се крећу по земљи: птице, стока, звери, сви гмизавци и сви људи. 22Све што је у својим ноздрвама имало дах живота, све што је било на копну, изгинуло је. 23Господ је истребио сва жива бића с лица земље: људе, животиње, гмизавце и птице на небу – све њих је истребио са земље. Остао је само Ноје и они што су били с њим у пловилу.

24Стотину педесет дана је вода господарила земљом.