Genesis 7 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 7:1-24

1Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu. 2Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso. 3Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi. 4Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”

5Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.

6Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600. 7Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula. 8Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo. 9Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu. 10Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.

11Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka. 12Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.

13Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo. 14Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake. 15Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse. 16Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.

17Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko. 18Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo. 19Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa. 20Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri. 21Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu. 22Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa. 23Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.

24Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

La Bible du Semeur

Genèse 7:1-24

L’embarquement

1Puis l’Eternel dit à Noé : Entre dans le bateau, toi et toute ta famille car je ne vois que toi qui sois juste parmi tes contemporains. 2Prends sept couples des animaux purs7.2 C’est-à-dire les animaux que la Loi de Moïse déclarera aptes à être mangés ou offerts en sacrifice (voir Lv 11). Certains seront offerts en sacrifice à la fin du déluge (8.20)., sept mâles et sept femelles, et un couple de tous les animaux qui ne sont pas purs, le mâle et sa femelle. 3Prends aussi sept couples de chaque espèce d’oiseaux pour en perpétuer la race sur toute la terre. 4Car dans sept jours, je vais faire pleuvoir sur la terre durant quarante jours et quarante nuits et j’effacerai de la surface de la terre tous les êtres que j’ai créés.

5Noé fit tout ce que l’Eternel lui avait ordonné.

6Noé était âgé de six cents ans quand le déluge vint sur la terre. 7Il entra dans le bateau avec ses fils, sa femme et ses belles-filles pour échapper aux eaux du déluge7.7 Cité en Mt 24.38 ; Lc 17.27.. 8Un couple d’animaux – un mâle et une femelle de ceux qui sont purs et de ceux qui ne le sont pas – ainsi que des oiseaux et de tout ce qui se meut à ras de terre 9deux par deux, vinrent trouver Noé pour entrer dans le bateau, comme Dieu l’avait prescrit à Noé. 10Au bout de sept jours, les eaux du déluge s’abattirent sur la terre.

Le déluge

11L’an 600 de la vie de Noé, le dix-septième jour du deuxième mois de l’année, quand toutes les sources d’eaux souterraines jaillirent et les écluses du ciel s’ouvrirent, 12et la pluie tomba sur la terre durant quarante jours et quarante nuits. 13Ce même jour, Noé entra dans le bateau ainsi que ses fils, Sem, Cham et Japhet, sa femme et ses trois belles-filles. 14Avec eux était entrée chaque espèce d’animaux sauvages, de bestiaux, de bêtes qui se meuvent à ras de terre, d’oiseaux, de petits oiseaux et tous les volatiles. 15Un couple de tout être vivant était venu trouver Noé pour entrer dans le bateau. 16Ils étaient arrivés deux par deux, mâle et femelle, comme Dieu l’avait ordonné. Puis l’Eternel referma la porte derrière Noé, 17et le déluge s’abattit durant quarante jours sur la terre, les eaux montèrent et soulevèrent le bateau, qui se mit à flotter au-dessus de la terre.

18Les eaux montèrent, grossirent considérablement sur la terre et le bateau vogua sur les flots. 19Le niveau de l’eau montait de plus en plus, de sorte que toutes les hautes montagnes sous tous les cieux furent submergées. 20Les eaux s’élevèrent de sept à huit mètres7.20 L’hébreu a : quinze coudées. au-dessus des montagnes qui disparurent sous les flots, 21et toute créature qui bougeait sur la terre périt : les oiseaux, le bétail et les animaux sauvages, toutes les bestioles qui pullulaient sur la terre, et tous les hommes. 22Tout ce qui respirait sur la terre ferme mourut. 23Ainsi l’Eternel effaça de la surface du sol tous les êtres vivants, depuis l’homme jusqu’au bétail, jusqu’aux animaux qui se meuvent à ras de terre et jusqu’aux oiseaux du ciel. Ils furent effacés de la terre et il ne resta que Noé et ceux qui étaient avec lui dans le bateau. 24La crue des eaux au-dessus de la terre dura cent cinquante jours.