Genesis 6 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 6:1-22

Kuyipa kwa Mtundu wa Anthu

1Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi, 2ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha. 3Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”

4Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.

5Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha, 6Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima. 7Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.” 8Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.

Nowa ndi Chigumula

9Mbiri ya Nowa inali yotere:

Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu. 10Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.

11Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu. 12Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi. 13Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko. 14Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja. 15Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake. 16Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba. 17Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa. 18Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho. 19Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe. 20Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo. 21Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”

22Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.

Thai New Contemporary Bible

ปฐมกาล 6:1-22

น้ำท่วมโลก

1เมื่อมนุษย์เริ่มทวีจำนวนขึ้นบนโลกและให้กำเนิดบุตรสาว 2บรรดาบุตรชายของพระเจ้าเห็นว่าบรรดาบุตรสาวของมนุษย์สวยงามก็เลือกเอามาเป็นภรรยาตามใจชอบ 3แล้วองค์พระผู้เป็นเจ้าตรัสว่า “จิตวิญญาณของเราจะไม่คงอยู่กับมนุษย์ตลอดไป เพราะเขาเป็นเพียงมนุษย์ที่ต้องตาย6:3 หรือเสื่อมทราม เขาจะมีอายุขัย 120 ปี”

4ในสมัยนั้นและสืบต่อมาภายหลัง มีคนเนฟิลอาศัยอยู่ในโลก คือสมัยที่บุตรชายของพระเจ้าไปอยู่กินกับบุตรสาวของมนุษย์และมีลูกหลานกับเขา คนเหล่านี้เป็นคนใหญ่คนโตที่มีชื่อเสียงในยุคโบราณ

5องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงเห็นว่าความชั่วร้ายของมนุษย์ในโลกทวีมากยิ่งขึ้น และความคิดจิตใจของเขาก็โน้มเอียงไปในทางชั่วอยู่เสมอ 6องค์พระผู้เป็นเจ้าจึงทรงเสียพระทัยยิ่งนักที่ได้ทรงสร้างมนุษย์ขึ้นมาในโลก และพระองค์ทรงปวดร้าวพระทัย 7ดังนั้นองค์พระผู้เป็นเจ้าจึงตรัสว่า “เราจะกวาดล้างมนุษยชาติที่เราได้สร้างขึ้นออกจากผืนแผ่นดิน ทั้งมนุษย์และสัตว์ทั้งปวง สัตว์ที่เลื้อยคลาน และนกในอากาศ เพราะเราเสียใจที่ได้สร้างพวกนี้ขึ้นมา” 8แต่โนอาห์เป็นที่โปรดปรานในสายพระเนตรขององค์พระผู้เป็นเจ้า

9นี่คือเรื่องราวเชื้อสายของโนอาห์

โนอาห์เป็นคนชอบธรรม เป็นคนดีพร้อมเมื่อเทียบกับคนในยุคของเขาและดำเนินชีวิตไปกับพระเจ้า 10โนอาห์มีบุตรชายสามคนคือ เชม ฮาม และยาเฟท

11ในขณะนั้นโลกเสื่อมทรามในสายพระเนตรของพระเจ้าและเต็มไปด้วยความโหดร้ายทารุณ 12พระเจ้าทรงเห็นว่าโลกเสื่อมทรามมากเพราะสิ่งมีชีวิตทั้งปวงล้วนดำเนินชีวิตอย่างเสื่อมทราม 13พระเจ้าจึงตรัสกับโนอาห์ว่า “เรากำลังจะนำจุดจบมาถึงคนทั้งปวง เพราะสิ่งมีชีวิตทั้งปวงทำให้โลกเต็มไปด้วยความโหดร้ายทารุณ เราจะทำลายสิ่งเหล่านี้และโลกอย่างแน่นอน 14ดังนั้นจงต่อเรือขึ้นลำหนึ่งด้วยไม้ไซเปรส และกั้นเป็นห้องๆ แล้วยาด้วยชันตลอดทั้งนอกและใน 15เรือนี้ยาว 300 ศอก กว้าง 50 ศอก และสูง 30 ศอก 16จงทำหลังคาคลุมและระหว่างหลังคากับตัวเรือให้เว้นช่องสูง 1 ศอก6:16 คือ ประมาณครึ่งเมตรโดยรอบ จงทำประตูบานหนึ่งไว้ด้านข้างของเรือ และต่อเรือเป็นชั้นล่าง ชั้นกลาง ชั้นบน 17เรากำลังจะให้น้ำท่วมโลกเพื่อทำลายสิ่งมีชีวิตทั้งมวลภายใต้ฟ้าสวรรค์ คือทุกสิ่งที่มีลมหายใจแห่งชีวิต ทุกสิ่งบนแผ่นดินโลกจะพินาศสิ้น 18แต่เราจะทำพันธสัญญาอันมั่นคงกับเจ้า เจ้าจะเข้าไปในเรือ คือทั้งตัวเจ้า ภรรยา บุตรชาย และบุตรสะใภ้ของเจ้า 19จงนำสัตว์ทุกชนิดมาเป็นคู่ๆ ทั้งตัวผู้และตัวเมียเข้ามาในเรือเพื่อรักษาชีวิตของมันให้รอดด้วยกันกับเจ้า 20นกทุกชนิด สัตว์ทุกชนิด สัตว์ที่เลื้อยคลานทุกชนิดจะมาหาเจ้าอย่างละคู่เพื่อรักษาชีวิตของพวกมันไว้ 21จงสะสมเสบียงทุกอย่างเพื่อเก็บไว้เป็นอาหารสำหรับเจ้าและสัตว์เหล่านั้น”

22โนอาห์ก็ทำทุกสิ่งตามที่พระเจ้าทรงบัญชา