Genesis 5 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 5:1-32

Mibado Kuyambira pa Adamu Mpaka Nowa

1Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi:

Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu. 2Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”

3Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti. 4Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 5Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.

6Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi. 7Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 8Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.

9Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani. 10Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 11Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.

12Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli. 13Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 14Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.

15Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi. 16Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 17Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.

18Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki. 19Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 20Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.

21Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela. 22Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 23Zaka zonse za Enoki zinali 365. 24Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.

25Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki. 26Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 27Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.

28Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna. 29Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.” 30Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi. 31Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.

32Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.

Swedish Contemporary Bible

1 Moseboken 5:1-32

1Här följer en förteckning över Adams släkt.

Människan var lik Gud när hon skapades. 2Gud skapade dem till man och kvinna, och välsignade dem och kallade dem människor5:2 På hebreiska adám. när de skapades.

3Adam var 130 år när hans son Set föddes. Denne liknade honom och var hans avbild.5:3 Jfr v. 1 och 1:26 4Sedan levde Adam ytterligare 800 år, fick söner och döttrar 5och dog 930 år gammal.

6Set var 105 år när hans son Enosh föddes. 7Sedan levde han ytterligare 807 år och fick söner och döttrar 8och dog 912 år gammal.

9Enosh var 90 år när hans son Kenan föddes. 10Sedan levde han ytterligare 815 år och fick söner och döttrar 11och dog 905 år gammal.

12Kenan var 70 år när hans son Mahalalel föddes. 13Sedan levde han ytterligare 840 år och fick söner och döttrar 14och dog 910 år gammal.

15Mahalalel var 65 år när hans son Jered föddes. 16Sedan levde han ytterligare 830 år och fick söner och döttrar 17och dog 895 år gammal.

18Jered var 162 år när hans son Henok föddes. 19Sedan levde han ytterligare 800 år och fick söner 20och döttrar och dog 962 år gammal.

21Henok var 65 år när hans son Metushelach föddes. 22Sedan levde han ytterligare 300 år i gemenskap med Gud5:22 levde… i gemenskap med Gud. Ordagrant: vandrade med Gud.Detta uttryck används även på många andra ställen. och fick söner och döttrar. 23Han blev 365 år. 24Henok vandrade i gemenskap med Gud och fanns sedan inte mer, för Gud tog bort honom.

25Metushelach var 187 år när hans son Lemek föddes. 26Sedan levde han ytterligare 782 år och fick söner och döttrar 27och dog 969 år gammal.

Noa

28Lemek var 182 år när han fick en son. 29Lemek kallade honom för Noa5:29 Namnet anspelar på både vila och tröst i hebreiskan., för han sa: ”Han kommer att ge oss tröst under det hårda arbetet med den jord som Herren har förbannat.” 30Sedan levde Lemek 595 år och fick söner och döttrar 31och dog 777 år gammal. 32När Noa var 500 år fick han tre söner, Sem, Ham och Jafet.