Genesis 49 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 49:1-33

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

1Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

mverani abambo anu Israeli.

3“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,

wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.

4Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

iwe unagona pa bedi la abambo ako,

ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

5“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.

6Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,

pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo

ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.

7Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

ndi ukali wawo wankhanza choterewu!

Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo

ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

8“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;

abale ako adzakugwadira iwe.

9Yuda ali ngati mwana wa mkango;

umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.

Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,

ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?

10Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,

mpaka mwini wake weniweni atabwera

ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.

11Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.

Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;

ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.

12Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;

malire ake adzafika ku Sidoni.

14“Isakara ali ngati bulu wamphamvu

wogona pansi pakati pa makola.

15Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

ndi kukongola kwa dziko lake,

iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake

ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.

17Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

songo yokhala mʼnjira

imene imaluma chidendene cha kavalo

kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

koma iye adzawathamangitsa.

20“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,

nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.

23Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

anamuthamangitsa ndi mauta awo.

24Koma uta wake sunagwedezeke,

ndi manja ake amphamvu aja analimbika,

chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,

chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.

25Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa

ndi mvula yochokera kumwamba,

ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,

ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.

26Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

madalitso a mapiri akale

oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.

Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,

pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,

ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

O Livro

Génesis 49:1-33

Jacob abençoa os filhos

1Então Jacob chamou todos os seus filhos e disse-lhes: “Juntem-se aqui, perto de mim e dir-vos-ei o que será de vocês no futuro.

2Ouçam-me, ó filhos de Jacob,

escutem Israel, o vosso pai!

3Rúben, tu és o mais velho,

o filho que eu tive na maturidade do meu vigor;

és o primeiro em categoria e em honra.

4Mas inconstante como és, semelhante às vagas do mar,

deixarás de ser o mais excelente porque me desonraste,

deitando-te com uma das minhas mulheres,

profanando o meu leito.

5Simeão e Levi são dois da mesma espécie;

são homens de violência e injustiça.

6A minha alma manteve-se afastada deles,

não quis participar nos seus intentos secretos,

porque no seu ódio mataram homens,

na sua excitação mutilaram bois.

7Maldita seja a sua fúria, pois foi feroz e cruel.

Por isso, espalharei os seus descendentes por todo o Israel.

8Judá, os teus irmãos te louvarão.

Destruirás os teus inimigos.

Os filhos do teu pai se inclinarão perante ti.

9És como um pequeno leão

que acabou de tragar a sua presa.

Assenta-se como um forte leão e deita-se como uma leoa;

quem ousará despertá-lo?

10O cetro real não deixará de lhe pertencer,

até que venha Silo, a quem todo o mundo obedecerá.

11Ele amarra o seu jumentinho à melhor videira,

e lava os seus fatos no vinho.

12Seus olhos são mais escuros do que o vinho,

seus dentes mais brancos que o leite.

13Zebulão habitará à beira do mar

e terá os portos de que se servirão os navios.

Os seus limites estender-se-ão até Sídon.

14Issacar é um possante animal de carga

que repousa no meio dos fardos.

15Quando vê que o seu repouso é bom,

e a terra é agradável para se viver,

de boa vontade se entregou ao trabalho

e aceitou a tarefa que lhe era imposta.

16Dan governará o seu povo

tal como qualquer outra tribo de Israel.

17Ele será como uma serpente no caminho,

como uma víbora à beira da estrada

que morde as patas do cavalo,

o qual lança o cavaleiro ao chão.

18Eu confio na tua salvação, Senhor!

19Gad será atacado por um bando de guerrilheiros,

mas ele os atacará pelos calcanhares.

20Aser produzirá alimento abundante

e de finíssima qualidade, próprio de reis.

21Naftali é como uma gazela à solta,

produzindo lindas crias.

22José é como uma árvore frutífera,

produzindo frutos junto duma fonte.

Os seus ramos passam acima do muro.

23Foi gravemente ferido por aqueles

que se atiraram sobre ele e o perseguiram.

24Mas o seu arco permeneceu firme,

e os seus braços jamais esmoreceram,

diante do Poderoso de Jacob,

o seu Pastor, o Rochedo de Israel.

25Que o Deus dos teus pais, o Todo-Poderoso,

te abençoe com as bênçãos dos céus

e também com as da Terra,

as bênçãos dos seios, assim como as da madre,

26Que as bênçãos do teu pai ultrapassem as bênçãos das antigas montanhas,

que chegam às alturas das colinas eternas.

Estas serão as bênçãos que descerão sobre a cabeça de José,

que teve de se separar dos irmãos.

27Benjamim é um lobo que devora a sua presa.

Devora os seus inimigos logo de manhã

e pela tarde reparte os despojos.”

28Estas são as bênçãos que Israel deu aos doze filhos.

A morte de Jacob

29-30Depois disse-lhes: “Vou morrer em breve. Vocês deverão pôr-me junto dos meus pais na terra de Canaã, na gruta que está no campo de Macpela, diante de Mamre, o campo que Abraão comprou a Efrom, o hitita, como terreno para sepultura. 31Foi lá que sepultaram Abraão e Sara, a sua mulher; e ainda Isaque mais a sua mulher Rebeca; eu próprio ali coloquei o corpo de Leia. 32Essa gruta e o campo foram comprados pelo meu avô Abraão aos filhos de Hete.”

33Tendo acabado de dar aquelas profecias e estas indicações aos filhos, deitou-se, acomodou-se na cama, deu um último suspiro e faleceu, juntando-se aos seus antepassados.