Genesis 49 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 49:1-33

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

1Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

mverani abambo anu Israeli.

3“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,

wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.

4Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

iwe unagona pa bedi la abambo ako,

ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

5“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.

6Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,

pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo

ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.

7Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

ndi ukali wawo wankhanza choterewu!

Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo

ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

8“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;

abale ako adzakugwadira iwe.

9Yuda ali ngati mwana wa mkango;

umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.

Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,

ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?

10Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,

mpaka mwini wake weniweni atabwera

ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.

11Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.

Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;

ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.

12Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;

malire ake adzafika ku Sidoni.

14“Isakara ali ngati bulu wamphamvu

wogona pansi pakati pa makola.

15Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

ndi kukongola kwa dziko lake,

iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake

ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.

17Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

songo yokhala mʼnjira

imene imaluma chidendene cha kavalo

kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

koma iye adzawathamangitsa.

20“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,

nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.

23Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

anamuthamangitsa ndi mauta awo.

24Koma uta wake sunagwedezeke,

ndi manja ake amphamvu aja analimbika,

chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,

chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.

25Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa

ndi mvula yochokera kumwamba,

ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,

ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.

26Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

madalitso a mapiri akale

oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.

Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,

pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,

ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

Bibelen på hverdagsdansk

1. Mosebog 49:1-33

Jakobs sidste ord til sine 12 sønner

1Derefter tilkaldte Jakob alle sine sønner, og de samlede sig omkring ham: „Nu skal jeg fortælle jer, hvordan det vil gå jer fremover.

2Kom og hør, I Jakobs sønner,

lyt til Israel, jeres far!

3Ruben, du min ældste søn,

det første skud på stammen,

ypperlig i rang og styrke,

4men uregerlig som havets bølger.

Du mistede din forret som førstefødt,

for du gik i seng med din fars kone.

Hvilken skændig handling

at vanære sin far sådan.

5Simeon og Levi, to alen af ét stykke,

mænd af vold og vrede ord.

6Jeres planer og motiver kan jeg ikke acceptere,

i galskab myrdede I mennesker og lemlæstede okser for sjov.

7Forbandet være jeres hidsighed,

forbandet jeres vrede og vold.

I bliver adskilt i Israel,

spredt ud over landet.

8Juda, dine brødre vil juble,

når du tilintetgør dine fjender.

Ja, dine brødre skal bøje sig for dig.

9Juda er en løve, der vogter over sit bytte.

Når han hviler sig, hvem tør da vække ham?

10Scepteret skal tilhøre Juda,

og han skal herske,

indtil den rette hersker kommer,49,10 Betydningen af det hebraiske shilo er omstridt, men det henviser nok til den Messiaskonge, der skulle komme fra Judas slægt.

han, som alle folkeslag skal lyde.

11Han binder sit æsel til en vinstok

og vasker sit tøj i druesaft.

12Hans øjne er mørkere end rødvin,

hans tænder hvidere end mælk.

13Zebulon vil havne ved havet,

hans land bliver hjemsted for skibe,

det strækker sig helt til Sidon.

14Issakar er stærk som et æsel,

han hviler sig mellem kvægfoldene.

15Når han opdager, hvor godt et sted, han har fundet

og hvor frugtbart landet er,

tager han villigt åget på skuldrene

og arbejder hårdt for føden.

16Dan skaffer sit folk deres ret

så godt som nogen af Israels stammer.

17Han er som en slange på stien,

hugger i hestens hæl, så rytteren styrter.

18Åh Gud, du er vores redning!

19Gad bliver angrebet af omstrejfende bander,

men han forfølger og udplyndrer dem.

20Asher får en overflod af afgrøder

og kan levere til kongens hof.

21Naftali løber frit omkring,

kommer gerne med smukke ord.49,21 Eller: „smukt afkom”. Oversættelsen er usikker i flere af disse korte, poetiske vers.

22Josef er som en vinstok, plantet ved kilden,

hvis ranker spreder sig over muren.

23Han blev beskudt med bitterheds pile,

hans modstandere behandlede ham hårdt,

24men han holdt sin bue med fasthed,

hans stærke arme rystede ikke.

Han blev hjulpet af Jakobs mægtige Gud,

og igennem det blev han en hyrde,

en frelser for Israels folk.

25Din fars Gud er din hjælper,

og den Almægtige velsigner dig

med himlens velsignelser ovenfra

og jordens velsignelser nedenfra,

med ægteskabelige glæder

og med mange børn.

26Den velsignelse, du får fra din far,

overgår de ældgamle bjerges velsignelser

og det, de evige høje kan tilbyde.

Må disse velsignelser hvile på Josefs hoved,

på issen af fyrsten blandt brødre.

27Benjamin er som en ulv på rov.

Han æder af sit bytte om morgenen

og deler ud af sit overskud om aftenen.”

28Det var, hvad Jakob sagde til Israels 12 stammeoverhoveder. Hver især fik de deres særlige ord med på vejen.

Jakobs død og begravelse

29Til sidst sagde Jakob til sine sønner: „Nu skal jeg dø. Begrav mig hos mine forfædre i Kana’ans land i hulen på Makpela-marken øst for Mamre, den mark, som Abraham købte af hittitten Efron. 30-32I den gravhule ligger Abraham og Sara begravet. Der ligger også Isak og Rebekka, og der har jeg selv begravet Lea.” 33Med disse ord til sine sønner udtrykte Jakob sin sidste vilje. Så lagde han sig til rette i sengen og drog sit sidste åndedrag.