Genesis 49 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 49:1-33

Yakobo Adalitsa Ana ake Aamuna

1Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.

2“Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo;

mverani abambo anu Israeli.

3“Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa;

mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga,

wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.

4Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana,

iwe unagona pa bedi la abambo ako,

ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.

5“Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo,

anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.

6Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri,

kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo,

pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo

ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.

7Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi

ndi ukali wawo wankhanza choterewu!

Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo

ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.

8“Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda;

dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako;

abale ako adzakugwadira iwe.

9Yuda ali ngati mwana wa mkango;

umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga.

Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi,

ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?

10Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda,

udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse,

mpaka mwini wake weniweni atabwera

ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.

11Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa,

ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino.

Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo;

ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.

12Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo,

mano ake woyera chifukwa cha mkaka.

13“Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja;

adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi;

malire ake adzafika ku Sidoni.

14“Isakara ali ngati bulu wamphamvu

wogona pansi pakati pa makola.

15Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira

ndi kukongola kwa dziko lake,

iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake

ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.

16“Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake

monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.

17Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu,

songo yokhala mʼnjira

imene imaluma chidendene cha kavalo

kuti wokwerapoyo agwe chagada.

18“Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.

19“Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo,

koma iye adzawathamangitsa.

20“Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma,

ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.

21“Nafutali ali ngati mbawala yayikazi

yokhala ndi ana okongola kwambiri.

22“Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso,

mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe,

nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.

23Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza;

anamuthamangitsa ndi mauta awo.

24Koma uta wake sunagwedezeke,

ndi manja ake amphamvu aja analimbika,

chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo,

chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.

25Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza;

chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa

ndi mvula yochokera kumwamba,

ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka,

ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.

26Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa

madalitso a mapiri akale

oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona.

Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe,

pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.

27“Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa;

umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha,

ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”

28Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.

Kumwalira kwa Yakobo

29Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti. 30Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda. 31Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya. 32Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”

33Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.

La Bible du Semeur

Genèse 49:1-33

Jacob bénit les douze tribus d’Israël

1Jacob convoqua ses fils et leur dit :

Réunissez-vous et je vous révélerai ce qui vous arrivera dans les temps à venir.

2Rassemblez-vous et écoutez, ╵fils de Jacob !

Ecoutez ce que dit ╵Israël, votre père.

3Ruben, tu es mon premier-né,

le premier fruit de ma vigueur, ╵du temps où j’étais plein de force,

toi, tu es supérieur ╵en dignité ╵et supérieur en force.

4Bouillonnant comme l’eau, ╵tu n’auras pas le premier rang !

Car tu as profané ╵la couche de ton père, ╵en entrant dans mon lit49.4 Voir Gn 35.22..

5Siméon et Lévi sont frères,

ils se sont mis d’accord ╵pour semer la violence.

6Non, je ne veux pas m’associer ╵à leur complot !

Je mets un point d’honneur ╵à ne pas approuver ╵leurs délibérations !

Car mus par leur colère, ╵ils ont tué des hommes ;

poussés par leur caprice, ╵ils ont mutilé des taureaux49.6 Voir Gn 34.25..

7Que leur colère soit maudite, ╵car elle est violente.

Maudit soit leur emportement, ╵car il est implacable !

Moi je les éparpillerai ╵au milieu de Jacob,

je les disperserai ╵en Israël.

8O toi, Juda, ╵tes frères te rendront hommage,

ta main fera ployer ╵la nuque de tes ennemis,

et les fils de ton père ╵se prosterneront devant toi.

9Oui, Juda est un jeune lion49.9 Voir Nb 24.9 ; Ap 5.5..

Mon fils, tu reviens de la chasse

et tu t’es accroupi ╵et couché comme un lion,

comme une lionne : ╵qui te ferait lever ?

10Le sceptre ne s’écartera ╵pas de Juda,

et l’insigne de chef ╵ne sera pas ôté ╵d’entre ses pieds

jusqu’à la venue de celui ╵auquel ils appartiennent49.10 Nom diversement traduit : le Pacifique, le Dominateur, l’Envoyé. celui… appartiennent: rend un mot hébreu dont l’interprétation est discutée. Ez 21.32 semble confirmer la lecture adoptée ici. Cette prophétie est généralement rapportée au Messie qui devait naître de la tribu de Juda.

et à qui tous les peuples ╵rendront obéissance.

11Son âne, il l’attache à la vigne,

et, à un cep de choix, ╵le petit de l’ânesse.

Il lave dans le vin ╵son vêtement,

dans le jus des raisins ╵il nettoie son manteau49.11 Image soulignant l’abondance (voir Ap 7.14 ; 19.13)..

12Il a les yeux plus rouges que le vin,

les dents plus blanches que le lait49.12 Autre traduction : Ses yeux ont été rendus sombres par le vin, et ses dents blanches par le lait..

13Zabulon aura sa demeure ╵sur le rivage de la mer,

il aura sur sa côte ╵un port pour les navires,

son territoire s’étendra ╵jusqu’à Sidon.

14Issacar est un âne ╵très vigoureux

couché au beau milieu ╵de deux enclos.

15Il a trouvé ╵que le repos est bon,

que le pays est agréable,

il tend l’épaule ╵pour porter le fardeau,

et il s’assujettit ╵à la corvée.

16Dan jugera son peuple,

comme les autres tribus d’Israël.

17Que Dan soit un serpent ╵sur le chemin,

qu’il soit une vipère ╵sur le sentier,

mordant les jarrets du cheval,

pour que le cavalier ╵en tombe à la renverse.

18Je compte sur toi, Eternel ╵pour accorder la délivrance.

19Gad agressé par une troupe ╵l’assaillira

et c’est sa troupe à lui ╵qui poursuivra la troupe adverse.

20Aser a une riche nourriture.

C’est lui qui fournira ╵des mets dignes d’un roi.

21Nephtali est semblable ╵à une biche en liberté ╵qui donne de beaux faons.

22Joseph est un rameau fertile

d’un arbre plein de fruits ╵planté près d’une source.

Ses branches grimpent et s’élancent ╵par-dessus la muraille.

23Des archers le provoquent, ╵le prennent à partie,

et le harcèlent de leurs flèches.

24Mais son arc reste ferme

car ses bras pleins de force ╵conservent leur souplesse

grâce au secours ╵du Puissant de Jacob,

qui est le berger et le Roc ╵sur lequel Israël se fonde.

25Oui, le Dieu de ton père ╵viendra à ton secours,

le Tout-Puissant te bénira.

Qu’il veuille te bénir d’en haut ╵par des pluies abondantes

et par des eaux d’en bas ╵où repose l’abîme,

par de nombreux enfants ╵et beaucoup de troupeaux.

26Les bénédictions de ton père surpassent

celles des montagnes antiques

et les meilleurs produits ╵des collines anciennes.

Que ces bénédictions ╵soient sur la tête de Joseph,

et sur le front ╵du prince de ses frères49.26 Voir Dt 33.15. !

27Benjamin est semblable ╵à un loup qui déchire.

Dès le matin, ╵il dévore sa proie,

et sur le soir encore, ╵répartit le butin.

28Tous ceux-là ont formé les douze tribus d’Israël, c’est ainsi que leur parla leur père et qu’il les bénit, en prononçant pour chacun sa bénédiction propre.

La mort de Jacob

29Jacob leur donna ses instructions : Je vais aller rejoindre mes ancêtres, enterrez-moi auprès de mes pères dans la caverne qui se trouve dans le champ d’Ephrôn le Hittite, 30dans la caverne du champ de Makpéla, vis-à-vis de Mamré, au pays de Canaan, la caverne qu’Abraham a achetée, avec le champ, à Ephrôn le Hittite en propriété funéraire49.30 Voir Gn 23.3-18.. 31C’est là qu’on a enterré Abraham et sa femme Sara ; c’est là qu’on a enterré Isaac et sa femme Rébecca. C’est là aussi que j’ai enterré Léa. 32Le champ et la caverne qui s’y trouve ont été achetés aux Hittites.

33Lorsque Jacob eut achevé d’énoncer ses instructions à ses fils, il ramena ses pieds sur son lit, expira et fut réuni à ses ancêtres49.33 Voir Ac 7.15..