Genesis 48 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 48:1-22

Manase ndi Efereimu

1Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo. 2Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.

3Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa, 4nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’

5“Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni. 6Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo. 7Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).

8Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”

9Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.”

Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”

10Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.

11Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”

12Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi. 13Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo. 14Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.

15Kenaka anadalitsa Yosefe nati,

“Mulungu amene makolo anga

Abrahamu ndi Isake anamutumikira,

Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga

moyo wanga wonse kufikira lero,

16mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse,

ameneyo adalitse anyamata awa.

Kudzera mwa iwowa

dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka.

Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu

pa dziko lapansi.”

17Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase, 18nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”

19Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.” 20Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati,

“Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati:

Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.”

Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.

21Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu. 22Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”

Bibelen på hverdagsdansk

1. Mosebog 48:1-22

Jakob velsigner Josefs sønner

1Kort efter fik Josef meddelelse om, at det gik hurtigt ned ad bakke med hans fars helbred. Han tog derfor straks af sted for at besøge ham sammen med sine to sønner Manasse og Efraim. 2Da Jakob hørte, at Josef var kommet, satte han sig med en kraftanstrengelse op og svingede benene ud over sengekanten. 3Derpå sagde han til Josef: „Gud den almægtige viste sig for mig i Luz i Kana’an og velsignede mig. 4Han sagde: ‚Jeg vil gøre dig til et stort folk og give Kana’ans land til dig og dine efterkommere, og det skal for altid være jeres ejendom.’ ”

5„Nu vil jeg adoptere dine to sønner, Efraim og Manasse, som blev født her i Egypten, før jeg kom hertil,” fortsatte Jakob. „De skal være mine egne sønner og arve på lige fod med Ruben og Simeon og mine andre sønner. 6Men de sønner, du får i fremtiden, bliver dine egne, og det land de skal arve, bliver indenfor Efraims og Manasses område. 7Da vi kom tilbage fra Paddan-Aram døde Rakel i Kana’an, inden vi ankom til Efrat—og jeg begravede hende der ved siden af vejen til Efrat.” (Efrat hedder nu Betlehem.) 8Så kiggede Jakob over på de to drenge. „Er det dine sønner?” spurgte han.

9„Ja,” svarede Josef, „det er de sønner, Gud har givet mig her i Egypten.”

„Bring dem herhen til mig,” sagde Jakob, „så jeg kan velsigne dem.” 10Jakob kunne ikke se særlig godt, for han var gammel og halvblind. Så førte Josef drengene hen til ham, og Jakob kyssede dem på kinden og omfavnede dem, 11og han sagde til Josef: „Jeg havde aldrig troet, at jeg skulle få dig at se igen. Men nu har Gud tilmed ladet mig se dine børn.”

12Så førte Josef drengene væk fra deres bedstefars knæ og bøjede sig dybt til jorden for ham. 13Derefter førte han med sin højre hånd Efraim hen til Jakobs venstre side og med sin venstre hånd Manasse hen til Jakobs højre side. 14Jakob lagde dog sin højre hånd på Efraims hoved, selvom han var den yngste, og sin venstre hånd på Manasses hoved, selvom han var den ældste, så han sad med armene over kors. 15Derpå velsignede han Josef og hans to sønner med følgende ord: „Må den Gud, som min bedstefar Abraham og min far Isak vandrede med, den Gud, som har været min hyrde livet igennem, 16den engel, som har bevaret mig fra alt ondt—må han velsigne de to drenge her! Må de føre min slægt videre, som jo udgår fra Abraham og Isak, og må de blive til et mægtigt folk.”

17Da Josef så, at hans far havde lagt sin højre hånd på Efraims hoved, kunne han ikke lide det, og han greb sin fars hånd for at lægge den på Manasses hoved. 18„Far,” sagde han. „Det er ham her, der er den ældste. Læg din højre hånd på hans hoved.”

19Men det nægtede hans far. „Jeg ved, hvad jeg gør, min søn,” svarede han. „Manasse vil blive stamfar til et mægtigt folk, men hans yngre bror vil blive endnu mægtigere. Hans efterkommere vil blive til mange folkeslag.” 20Den dag velsignede Jakob drengene med følgende velsignelse:

„Israelitterne vil bruge jeres navne til at velsigne hinanden. De vil sige: ‚Må Gud velsigne jer, som han velsignede Efraim og Manasse!’ ” På den måde satte han Efraim over Manasse.

21Derefter sagde Jakob til Josef: „Jeg skal snart dø, men Gud vil være med jer og føre jer til Kana’an, det land, han lovede jeres forfædre. 22Og da du har en højere position end dine brødre, overdrager jeg dig højlandet omkring Sikem, som vi tog fra amoritterne med sværd og bue.”