Genesis 45 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 45:1-28

Yosefe Adziwulula kwa Abale Ake

1Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake. 2Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.

3Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.

4Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto! 5Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu. 6Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola. 7Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.

8“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine. 9Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe. 10Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine. 11Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’

12“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu. 13Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”

14Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira. 15Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.

16Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera. 17Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani. 18Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’ ”

19“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno. 20Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’ ”

21Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo. 22Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu. 23Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake. 24Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”

25Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani. 26Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira. 27Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka. 28Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Начало 45:1-28

Юсуф открывается своим братьям

1Тогда Юсуф не мог более сдержать себя перед слугами и воскликнул:

– Уходите все прочь от меня! – и никого не было с Юсуфом, когда он открылся своим братьям.

2Он так громко зарыдал, что услышали египтяне, и слух об этом дошёл до двора фараона.

3Юсуф сказал своим братьям:

– Я – Юсуф! Жив ли ещё мой отец?

Но братья ничего не могли ответить, так они были ошеломлены.

4Тогда Юсуф сказал братьям:

– Подойдите же ко мне.

И когда они подошли, он сказал:

– Я ваш брат Юсуф, которого вы продали в Египет! 5Но не тревожьтесь и не обвиняйте больше себя за то, что продали меня сюда: это Всевышний послал меня перед вами для спасения вашей жизни. 6Уже два года, как в стране голод, и ещё пять лет не будет ни пахоты, ни жатвы. 7Но Всевышний послал меня перед вами, чтобы сохранить ваш род на земле и великим избавлением спасти ваши жизни.

8Итак, не вы послали меня сюда, но Всевышний: Он сделал меня отцом фараону, господином над всем его домом и правителем всего Египта. 9Поспешите вернуться к моему отцу и скажите ему: «Вот что говорит твой сын Юсуф: „Всевышний сделал меня правителем всего Египта. Приходи ко мне, не медли; 10ты будешь жить в области Гошен и будешь рядом со мной: и ты, и твои дети и внуки, и твой крупный и мелкий скот, и всё, что у тебя есть. 11Там я смогу прокормить тебя – ведь предстоят ещё пять лет голода, – а иначе и ты, и твой дом, и все, кто принадлежат тебе, будете в нужде“».

12Вы видите своими глазами, и вы, и мой брат Вениамин, что это действительно я говорю с вами. 13Расскажите же моему отцу о том, как я прославлен в Египте, и обо всём, что вы видели. И поскорее приведите сюда моего отца.

14Он обнял своего брата Вениамина и заплакал, и Вениамин плакал, обнимая его. 15Он поцеловал всех братьев и с плачем обнимал их. Потом братья беседовали с ним.

Фараон позволяет Якубу переселиться в Египет

16Слух о том, что пришли братья Юсуфа, дошёл до двора фараона. Фараон обрадовался, и его придворные тоже, 17и фараон сказал Юсуфу:

– Скажи своим братьям: «Сделайте вот что: навьючьте своих животных, возвращайтесь в землю Ханона 18и приведите ко мне отца и ваши семьи. Я дам вам лучшую землю в Египте, и вы будете жить её плодами». 19Ещё повелеваю тебе сказать им: «Сделайте вот что: возьмите в Египте колесницы для ваших детей и жён, привезите своего отца и приходите сами. 20Не жалейте о вашем имуществе, потому что всё лучшее в Египте будет вашим».

21Сыновья Исроила так и сделали. Юсуф дал им колесницы, как приказал фараон, и припасы в дорогу. 22Каждому он подарил новую одежду, а Вениамину дал три с половиной килограмма45:22 Букв.: «триста шекелей». серебра и пять смен одежды. 23Отцу он послал десять ослов, нагруженных лучшим добром Египта, и десять ослиц, нагруженных зерном, хлебом и другими припасами для путешествия. 24После этого он отпустил братьев, и когда они уходили, сказал им:

– Ни о чём не тревожьтесь в пути!

25Они отправились в путь из Египта, пришли к своему отцу Якубу в землю Ханона 26и сказали ему:

– Юсуф жив! Юсуф – правитель всего Египта!

У Якуба замерло сердце, и он не поверил им. 27Но когда они передали ему всё, что сказал Юсуф, и когда он увидел колесницы, которые Юсуф послал, чтобы перевезти его, душа Якуба ожила. 28И Исроил сказал:

– Довольно! Мой сын Юсуф жив. Пойду и увижу его, прежде чем умру.