Genesis 45 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 45:1-28

Yosefe Adziwulula kwa Abale Ake

1Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake. 2Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.

3Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.

4Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto! 5Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu. 6Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola. 7Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.

8“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine. 9Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe. 10Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine. 11Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’

12“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu. 13Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”

14Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira. 15Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.

16Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera. 17Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani. 18Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’ ”

19“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno. 20Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’ ”

21Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo. 22Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu. 23Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake. 24Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”

25Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani. 26Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira. 27Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka. 28Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”

La Bible du Semeur

Genèse 45:1-28

Joseph révèle son identité à ses frères

1Alors Joseph, ne pouvant plus dominer son émotion devant tous ceux qui étaient présents, s’écria : Faites sortir tout le monde !

Ainsi personne de son entourage n’était en sa présence lorsqu’il fit connaître son identité à ses frères45.1 Voir Ac 7.13.. 2Mais il sanglotait si fort en parlant que les Egyptiens l’entendirent, et la nouvelle parvint jusqu’au palais du pharaon. 3Il dit à ses frères : Je suis Joseph ! Mon père est-il encore en vie ?

Mais ses frères étaient incapables de lui répondre tant ils avaient peur de lui. 4Alors Joseph leur dit : Venez près de moi !

Ils s’approchèrent.

– Je suis Joseph, leur dit-il, votre frère, que vous avez vendu pour être emmené en Egypte. 5Et maintenant, ne vous tourmentez pas et ne soyez pas fâchés de m’avoir vendu comme esclave. C’est pour vous sauver la vie que Dieu m’a envoyé devant vous. 6Car voici deux ans que la famine sévit dans ce pays et pendant cinq ans encore, il n’y aura ni labour ni moisson. 7Dieu m’a envoyé devant vous pour vous faire subsister sur la terre, pour préserver votre vie par une très grande délivrance. 8C’est pourquoi ce n’est pas vous qui m’avez envoyé ici, c’est Dieu. Et il m’a élevé au rang de « Père pour le pharaon45.8 Titre officiel des vizirs et des ministres. Certains pensent que Joseph était devenu le conseiller du pharaon. Voir 41.42. », faisant de moi le maître de toute sa cour et le dirigeant de toute l’Egypte. 9Retournez donc au plus vite auprès de mon père et dites-lui : « Ton fils Joseph te fait dire ceci : Dieu m’a établi maître de toute l’Egypte ; viens auprès de moi sans tarder. 10Tu habiteras dans la région de Goshen45.10 Près de la frontière nord-est de l’Egypte, dans le delta du Nil, une région très fertile (v. 18) et propre à l’élevage., pour être proche de moi, toi, tes enfants et tes petits-enfants, tes moutons, tes chèvres et tes bovins, tout ce qui t’appartient. 11Et là, je pourvoirai à tes besoins pour que tu ne restes pas sans ressources, toi, ta famille et tout ce qui t’appartient. Car il y aura encore cinq ans de famine45.11 Voir Ac 7.14.. » 12Vous voyez de vos yeux, et mon frère Benjamin également, que c’est bien moi qui vous parle. 13Informez mon père de tous les honneurs dont je suis comblé en Egypte, racontez-lui tout ce que vous avez vu et dépêchez-vous de le faire venir ici.

14Puis il se jeta au cou de Benjamin, son frère, et tous deux pleurèrent sur les épaules l’un de l’autre. 15Ensuite, il embrassa tous ses frères en pleurant. Après quoi, ses frères s’entretinrent avec lui.

Le pharaon invite Jacob en Egypte

16La nouvelle de l’arrivée des frères de Joseph se répandit aussitôt au palais du pharaon. Elle fit plaisir au pharaon et à ses hauts fonctionnaires. 17Le pharaon dit à Joseph : Tu diras à tes frères : « Voilà ce que vous allez faire : Chargez vos bêtes et retournez au pays de Canaan, 18pour aller y chercher votre père ainsi que vos familles. Puis vous reviendrez chez moi et je vous donnerai les bonnes terres d’Egypte et vous mangerez les meilleurs produits du pays. » 19Quant à toi, transmets-leur l’ordre suivant : « Emmenez avec vous d’Egypte des chariots pour vos enfants et vos femmes, faites-y monter aussi votre père et revenez. 20N’ayez pas de regret pour ce que vous laisserez, car ce qu’il y a de meilleur dans toute l’Egypte sera à votre disposition. »

21Les fils d’Israël firent ce qu’on leur avait dit. Joseph leur procura des chariots, selon ce qu’avait déclaré le pharaon, et il leur donna des provisions pour le voyage. 22Il offrit un habit de rechange à chacun de ses frères ; quant à Benjamin, il lui donna trois cents pièces d’argent et cinq habits de rechange. 23Il envoya à son père dix ânes chargés des meilleurs produits de l’Egypte, et dix ânesses chargées de blé, de pain et de vivres pour son voyage. 24Il prit congé de ses frères en leur recommandant de ne pas se disputer45.24 Autre traduction : de ne pas se presser ou de se faire du souci. en chemin. Et ils s’en allèrent.

Les frères de Joseph reviennent auprès de Jacob

25Ils retournèrent donc d’Egypte au pays de Canaan auprès de Jacob, leur père. 26Ils lui annoncèrent la nouvelle : « Joseph vit encore, et c’est même lui qui gouverne toute l’Egypte. » Mais il ne réagit pas parce qu’il ne les croyait pas. 27Ils lui répétèrent tout ce que Joseph avait dit. Puis Jacob vit les chariots que Joseph avait envoyés pour le transporter. Alors il reprit vie. 28Israël déclara : Assez parlé : Joseph mon fils est encore en vie, j’irai le voir avant de mourir.